< Žalmy 32 >

1 Žalm Davidův vyučující. Blahoslavený jest ten, jemuž odpuštěno přestoupení, a jehož hřích přikryt jest.
Salimo la Davide. Malangizo. Ngodala munthu amene zolakwa zake zakhululukidwa; amene machimo ake aphimbidwa.
2 Blahoslavený člověk, jemuž nepočítá Hospodin nepravosti, a v jehož duchu lsti není.
Ngodala munthu amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
3 Já když jsem mlčel, prahly kosti mé v úpění mém každého dne.
Pamene ndinali chete, mafupa anga anakalamba chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
4 Nebo dnem i nocí obtížena byla nade mnou ruka tvá, tak že přirozená vlhkost má obrátila se v sucho letní. (Sélah)
Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu linandipsinja; mphamvu zanga zinatha monga nthawi yotentha yachilimwe. (Sela)
5 Protož hřích svůj oznámil jsem tobě, a nepravosti své jsem neukryl. Řekl jsem: Vyznám na sebe Hospodinu přestoupení svá, a ty jsi odpustil nepravost hříchu mého. (Sélah)
Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu, sindinabise mphulupulu zanga. Ndinati, “Ine ndidzawulula zolakwa zanga kwa Yehova, ndipo Inu munandikhululukira mlandu wa machimo anga.” (Sela)
6 Za to se tobě bude modliti každý svatý, v času příhodném k nalezení tebe; pročež vody mnohé v rozvodnění k němu nedosáhnou.
Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo pomwe mukupezeka; ndithu pamene madzi amphamvu auka, sadzamupeza.
7 Ty jsi skrýše má, od ssoužení zachováš mne, a plésáním vítězným obdaříš. (Sélah)
Inu ndi malo anga obisala; muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga ndi nyimbo zachipulumutso. (Sela)
8 Já tobě k srozumění posloužím, a vyučím tě cestě, po níž bys choditi měl; dámť radu, oči své na tě obrátě.
Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo; ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
9 Nebývejte jako kůň a jako mezek, kteříž rozumu nemají, jejichž ústa uzdou a udidly sevříti musíš, aby tobě neškodili.
Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
10 Mnohé bolesti jsou bezbožníka, ale toho, jenž naději skládá v Hospodinu, milosrdenství obklíčí.
Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa koma chikondi chosatha cha Yehova chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
11 Radujte se v Hospodinu, a plésejte spravedliví, a prozpěvujte všickni srdce upřímého.
Kondwerani mwa Yehova inu olungama; imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!

< Žalmy 32 >