< Žalmy 31 >

1 Přednímu zpěváku, žalm Davidův. V tebe, Hospodine, doufám, nedejž mi zahanbenu býti na věky, pro spravedlnost svou vysvoboď mne.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo; musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi; mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.
2 Nakloň ke mně ucha svého, rychle vytrhni mne; budiž mi pevnou skalou a domem ohraženým, abys mne zachoval.
Tcherani khutu lanu kwa ine, bwerani msanga kudzandilanditsa; mukhale thanthwe langa lothawirapo, linga lolimba kundipulumutsa ine.
3 Nebo skála má a hrad můj ty jsi, protož pro jméno své veď i doveď mne.
Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa, chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.
4 Vyveď mne z leči, kterouž polékli na mne; nebo síla má ty jsi.
Ndimasuleni mu msampha umene anditchera pakuti ndinu pothawirapo panga.
5 V ruce tvé poroučím ducha svého, nebo jsi mne vykoupil, Hospodine, Bože silný a věrný.
Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga; womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.
6 Nenávidím těch, kteříž následují pouhých marností, nebo já v Hospodinu naději skládám.
Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe; ine ndimadalira Yehova.
7 Plésati a radovati se budu v milosrdenství tvém, že jsi vzezřel na mé trápení, a poznal jsi v ssoužení duši mou.
Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu popeza Inu munaona masautso anga ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.
8 Aniž jsi mne zavřel v ruce nepřítele, ale postavil jsi na širokosti nohy mé.
Inu simunandipereke kwa mdani koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.
9 Smiluj se nade mnou, Hospodine, nebo jsem ssoužen, tak že usvadla zámutkem tvář má, duše má, i život můj.
Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto; maso anga akulefuka ndi chisoni, mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.
10 Žalostí zajisté zhynulo zdraví mé, a léta má od úpění, zemdlena bídou mou síla má, a kosti mé vyprahly.
Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula; mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso, ndipo mafupa anga akulefuka.
11 U všech nepřátel svých jsem v pohanění, a nejvíce u sousedů, známým pak svým jsem strašidlem; kteříž mne vídají vně, utíkají přede mnou.
Chifukwa cha adani anga onse, ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga; ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga. Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.
12 Vyšel jsem z paměti tak, jako mrtvý, učiněn jsem jako nádoba rozražená.
Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira; ndakhala ngati mʼphika wosweka.
13 Nebo slýchám utrhání mnohých, strach odevšad, když se proti mně spolu puntují, lstivě přemýšlejíce, jak by odjali duši mou.
Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri; zoopsa zandizungulira mbali zonse; iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane, kuti atenge moyo wanga.
14 Ale já v tobě naději skládám, Hospodine; řekl jsem: Bůh můj jsi ty.
Koma ndikudalira Inu Yehova; ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
15 V rukou tvých jsou časové moji, vytrhni mne z ruky nepřátel mých a těch, kteříž mne stihají.
Masiku anga ali mʼmanja mwanu; ndipulumutseni kwa adani anga ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.
16 Osvěť tvář svou nad služebníkem svým, zachovej mne pro milosrdenství své.
Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu; pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.
17 Hospodine, ať nejsem zahanben, nebo jsem tě vzýval; nechať jsou zahanbeni bezbožníci, a skroceni v pekle. (Sheol h7585)
Yehova musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndalirira kwa Inu; koma oyipa achititsidwe manyazi ndipo agone chete mʼmanda. (Sheol h7585)
18 Oněmějte rtové lživí, kteříž mluví proti spravedlivému tvrdě, pyšně a s potupou.
Milomo yawo yabodzayo ikhale chete, pakuti chifukwa cha kunyada ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.
19 Ó jak veliká jest dobrotivost tvá, kterouž jsi odložil těm, jenž se bojí tebe, a kterouž jsi činíval doufajícím v tebe před syny lidskými.
Ndi waukulu ubwino wanu umene mwawasungira amene amakuopani, umene mumapereka anthu akuona kwa iwo amene amathawira kwa Inu.
20 Ty je skrýváš v skrýši oblíčeje svého před vysokomyslností člověka, skrýváš je jako v stanu před jazyky svárlivými.
Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa, kuwateteza ku ziwembu za anthu; mʼmalo anu okhalamo mumawateteza kwa anthu owatsutsa.
21 Požehnaný buď Hospodin, nebo prokázal ke mně divné milosrdenství své jako v městě ohraženém.
Matamando akhale kwa Yehova, pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.
22 Já zajisté když jsem pospíchal, řekl jsem: Zavrženť jsem od očí tvých, ale ty jsi vyslyšel hlas pokorných modliteb mých, když jsem k tobě volal.
Ndili mʼnkhawa zanga ndinati, “Ine ndachotsedwa pamaso panu!” Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.
23 Milujtež Hospodina všickni svatí jeho, neboť ostříhá věřících Hospodin, a též odplací vrchovatě tomu, kdož pýchu provodí.
Kondani Yehova oyera mtima ake onse! Yehova amasunga wokhulupirika koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.
24 Zmužile sobě čiňte, (a posilní Bůh srdce vašeho), všickni, kteříž naději máte v Hospodinu.
Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima, inu nonse amene mumayembekezera Yehova.

< Žalmy 31 >