< Žalmy 27 >

1 Davidův. Hospodin světlo mé a spasení mé, kohož se budu báti? Hospodin síla života mého, kohož se budu strašiti?
Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
2 Útok učinivše na mne zlostníci, k sežrání těla mého, protivníci moji a nepřátelé moji, sami se potkli a padli.
Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
3 Protož byť i stany své proti mně rozbili, nebude se lekati srdce mé; byť se pozdvihla proti mně i válka, na toť se já spouštím.
Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
4 Jedné věci žádal jsem od Hospodina, téť vždy hledati budu: Abych přebýval v domě Hospodinově po všecky dny života svého, a spatřoval okrasu Hospodinovu, a zpytoval v chrámě jeho.
Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
5 Nebo tu mne ukryje v stánku svém, v den zlý schová mne v skrýši stanu svého, a na skálu vyzdvihne mne.
Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
6 A tak vyvýšena bude hlava má nad nepřátely mými, kteříž mne obklíčili; i budu obětovati v stánku jeho oběti plésání, prozpěvovati a chvály vzdávati budu Hospodinu.
Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
7 Slyš mne, Hospodine, hlasem volajícího, a smiluj se nade mnou, i vyslyš mne.
Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
8 O tobě přemýšlí srdce mé, že velíš, řka: Hledejte tváři mé, a protož tváři tvé, Hospodine, hledati budu.
Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
9 Neskrývejž tváři své přede mnou, aniž zamítej v hněvě služebníka svého; spomožení mé býval jsi, neopouštěj mne, aniž se mne zhošťuj, Bože spasení mého.
Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
10 Ačkoli otec můj a matka má mne opustili, Hospodin však mne k sobě přivine.
Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
11 Vyuč mne, Hospodine, cestě své, a veď mne po stezce přímé pro ty, jenž mne střehou.
Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
12 Nevydávejž mne líbosti protivníků mých, neboť by ostáli proti mně svědkové lživí, i ten, jenž dýše ukrutností.
Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
13 Bychť nevěřil, že užívati budu dobroty Hospodinovy v zemi živých, nikoli bych neostál.
Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
14 Očekávejž na Hospodina, posilň se, a onť posilní srdce tvého; protož očekávej na Hospodina.
Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.

< Žalmy 27 >