< Žalmy 25 >

1 Žalm Davidův. K toběť, Hospodine, duše své pozdvihuji.
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 Bože můj, v toběť naději skládám, nechť nejsem zahanben, aby se neradovali nepřátelé moji nade mnou.
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 A takť i všickni, kteříž na tě očekávají, zahanbeni nebudou; zahanbeni budou, kteříž se převráceně mají bez příčiny.
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Cesty své, Hospodine, uveď mi v známost, a stezkám svým vyuč mne.
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 Dejž, ať chodím v pravdě tvé, a poučuj mne; nebo ty jsi Bůh spasitel můj, na tebeť očekávám dne každého.
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Rozpomeň se na slitování svá, Hospodine, a na milosrdenství svá, kteráž jsou od věků.
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 Hříchů mladosti mé a přestoupení mých nezpomínej, ale podlé milosrdenství svého pamětliv buď na mne pro dobrotu svou, Hospodine.
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 Dobrý a přímý jest Hospodin, a protož vyučuje hříšníky cestě své.
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 Působí to, aby tiší chodili v soudu, a vyučuje tiché cestě své.
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 Všecky stezky Hospodinovy jsou milosrdenství a pravda těm, kteříž ostříhají smlouvy jeho a svědectví jeho.
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 Pro jméno své, Hospodine, odpusť nepravost mou, neboť jest veliká.
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 Který jest člověk, ješto se bojí Hospodina, jehož vyučuje, kterou by cestu vyvoliti měl?
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 Duše jeho v dobrém přebývati bude, a símě jeho dědičně obdrží zemi.
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 Tajemství Hospodinovo zjevné jest těm, kteříž se jeho bojí, a v známost jim uvodí smlouvu svou.
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 Oči mé vždycky patří k Hospodinu, on zajisté z leči vyvodí nohy mé.
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Popatřiž na mne, a smiluj se nade mnou, neboť jsem opuštěný a strápený.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 Ssoužení srdce mého rozmnožují se, z úzkostí mých vyveď mne.
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 Viz trápení mé a bídu mou, a odpusť všecky hříchy mé.
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 Viz nepřátely mé, jak mnozí jsou, a nenávistí nešlechetnou nenávidí mne.
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Ostříhej duše mé, a vytrhni mne, ať nejsem zahanben, neboť v tebe doufám.
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 Sprostnost a upřímnost nechať mne ostříhají, nebo na tě očekávám.
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 Vykup, ó Bože, Izraele ze všelijakých úzkostí jeho.
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!

< Žalmy 25 >