< Žalmy 147 >

1 Chvalte Hospodina, nebo dobré jest zpívati žalmy Bohu našemu, nebo rozkošné jest, a ozdobná jest chvála.
Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
2 Stavitel Jeruzaléma Hospodin, rozptýlený lid Izraelský shromažďuje,
Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
3 Kterýž uzdravuje skroušené srdcem, a uvazuje bolesti jejich,
Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
4 Kterýž sčítá počet hvězd, a každé z nich ze jména povolává.
Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
5 Velikýť jest Pán náš, a nesmírný v síle; rozumnosti jeho není počtu.
Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
6 Pozdvihuje pokorných Hospodin, ale bezbožné snižuje až k zemi.
Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
7 Zpívejte Hospodinu s díkčiněním, zpívejte žalmy Bohu našemu na citaře,
Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
8 Kterýž zastírá nebesa hustými oblaky, nastrojuje zemi déšť, a vyvodí trávu na horách.
Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
9 Kterýž dává hovadům potravu jejich, i mladým krkavcům, kteříž volají k němu.
Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
10 Nemáť v síle koně zalíbení, aniž se kochá v lejtkách muže udatného.
Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
11 Líbost má Hospodin v těch, kteříž se ho bojí, a kteříž doufají v milosrdenství jeho.
Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
12 Chval, Jeruzaléme, Hospodina, chval Boha svého, Sione.
Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
13 Nebo on utvrzuje závory bran tvých, požehnání udílí synům tvým u prostřed tebe.
pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
14 On působí v končinách tvých pokoj, a bělí pšeničnou nasycuje tě.
Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
15 On když vysílá na zemi rozkaz svůj, velmi rychle k vykonání běží slovo jeho.
Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
16 Onť dává sníh jako vlnu, jíním jako popelem posýpá.
Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
17 Hází ledem svým jako skyvami; před zimou jeho kdo ostojí?
Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
18 Vysílaje slovo své, rozpouští je; hned jakž povane větrem svým, anť tekou vody.
Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
19 Zvěstuje slovo své Jákobovi, ustanovení svá a soudy své Izraelovi.
Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
20 Neučinilť tak žádnému národu, a protož soudů jeho nepoznali. Halelujah.
Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Žalmy 147 >