< Žalmy 139 >

1 Přednímu zpěváku, žalm Davidův. Hospodine, ty jsi mne zkusil a seznal.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
2 Ty znáš sednutí mé i povstání mé, rozumíš myšlení mému zdaleka.
Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
3 Chození mé i ležení mé ty obsahuješ, a všech mých cest svědom jsi.
Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
4 Než ještě mám na jazyku slovo, aj, Hospodine, ty to všecko víš.
Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
5 Z zadu i z předu obklíčils mne, a vzložils na mne ruku svou.
Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
6 Divnější jest umění tvé nad můj vtip; vysoké jest, nemohu k němu.
Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
7 Kamž bych zašel od ducha tvého? Aneb kam bych před tváří tvou utekl?
Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
8 Jestliže bych vstoupil na nebe, tam jsi ty; pakli bych sobě ustlal v hrobě, aj, přítomen jsi. (Sheol h7585)
Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol h7585)
9 Vzal-li bych křídla záře jitřní, abych bydlil při nejdalším moři:
Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
10 I tamť by mne ruka tvá provedla, a pravice tvá by mne popadla.
kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
11 Dím-li pak: Aspoň tmy, jako v soumrak, přikryjí mne, ale i noc jest světlem vůkol mne.
Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
12 Aniž ty tmy před tebou ukryti mohou, anobrž noc jako den tobě svítí, rovně tma jako světlo.
komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
13 Ty zajisté v moci máš ledví má, přioděl jsi mne v životě matky mé.
Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
14 Oslavuji tě, proto že se hrozným a divným skutkům tvým divím, a duše má zná je výborně.
Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
15 Neníť ukryta žádná kost má před tebou, jakž jsem učiněn v skrytě, a řemeslně složen, v nejhlubších místech země.
Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
16 Trupel můj viděly oči tvé, v knihu tvou všickni oudové jeho zapsáni jsou, i dnové, v nichž formováni byli, když ještě žádného z nich nebylo.
Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
17 Protož u mne ó jak drahá jsou myšlení tvá, Bože silný, a jak jest jich nesčíslná summa!
Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
18 Chtěl-li bych je sčísti, více jest jich než písku; procítím-li, a já jsem vždy s tebou.
Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
19 Zabil-li bys, ó Bože, bezbožníka, tehdážť by muži vražedlní odstoupili ode mne,
Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
20 Kteříž mluví proti tobě nešlechetně; marně vyvyšují nepřátely tvé.
Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
21 Zdaliž těch, kteříž tě v nenávisti mají, ó Hospodine, v nenávisti nemám? A ti, kteříž proti tobě povstávají, zdaž mne nemrzejí?
Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
22 Úhlavní nenávistí jich nenávidím, a mám je za nepřátely.
Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
23 Vyzpytuj mne, Bože silný, a poznej srdce mé; zkus mne, a poznej myšlení má.
Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
24 A popatř, chodím-liť já cestou odpornou tobě, a veď mne cestou věčnou.
Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.

< Žalmy 139 >