< Žalmy 115 >

1 Ne nám, Hospodine, ne nám, ale jménu svému dej čest, pro milosrdenství své a pro pravdu svou.
Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
2 Proč mají říkati pohané: Kdež jest nyní Bůh jejich?
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
3 Ješto Bůh náš jest na nebi, čině všecko, což se mu líbí.
Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
4 Modly pak jejich jsou stříbro a zlato, dílo rukou lidských.
Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
5 Ústa mají, a nemluví, oči mají, a nevidí.
Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
6 Uši mají, a neslyší, nos mají, a nečijí.
makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
7 Ruce mají, a nemakají, nohy mají, a nechodí, aniž volati mohou hrdlem svým.
manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
8 Nechať jsou jim podobni, kteříž je dělají, a kdožkoli v nich doufají.
Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
9 Izraeli, doufej v Hospodina, nebo spomocníkem a štítem takových on jest.
Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 Dome Aronův, doufej v Hospodina, spomocníkem a štítem takových on jest.
Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 Kteříž se bojíte Hospodina, doufejte v Hospodina, spomocníkem a štítem takových on jest.
Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
12 Hospodin rozpomena se na nás, požehná; požehná domu Izraelovu, požehná i domu Aronovu.
Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 Požehná bojícím se Hospodina, malým, i velikým.
adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
14 Rozmnoží Hospodin vás, vás i syny vaše.
Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 Požehnaní vy od Hospodina, kterýž učinil nebesa i zemi.
Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Nebesa jsou nebesa Hospodinova, zemi pak dal synům lidským.
Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 Ne mrtví chváliti budou Hospodina, ani kdo ze všech těch, kteříž sstupují do místa mlčení,
Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
18 Ale my dobrořečiti budeme Hospodinu od tohoto času až na věky. Halelujah.
ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.

< Žalmy 115 >