< Žalmy 113 >

1 Halelujah. Chvalte služebníci Hospodinovi, chvalte jméno Hospodinovo.
Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
2 Budiž jméno Hospodinovo požehnáno od tohoto času až na věky.
Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 Od východu slunce až do západu jeho chváleno buď jméno Hospodinovo.
Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
4 Vyvýšenť jest nade všecky národy Hospodin, a nad nebesa sláva jeho.
Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
5 Kdo jest rovný Hospodinu Bohu našemu, kterýž vysoko bydlí?
Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
6 Kterýž snižuje se, aby všecko spatřoval, což jest na nebi i na zemi.
amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
7 Vyzdvihuje z prachu nuzného, a z hnoje vyvyšuje chudého,
Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
8 Aby jej posadil s knížaty, s knížaty lidu svého.
amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
9 Kterýž vzdělává neplodnou v čeled, a matku veselící se z dítek. Halelujah.
Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.

< Žalmy 113 >