< Žalmy 106 >

1 Halelujah. Oslavujte Hospodina, nebo dobrý jest, nebo na věky milosrdenství jeho.
Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 Kdo může vymluviti nesmírnou moc Hospodinovu, a vypraviti všecku chválu jeho?
Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
3 Blahoslavení, kteříž ostříhají soudu, a činí spravedlnost každého času.
Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
4 Pamatuj na mne, Hospodine, pro milost k lidu svému, navštěv mne spasením svým,
Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
5 Abych užíval dobrých věcí s vyvolenými tvými, a veselil se veselím národu tvého, a chlubil se spolu s dědictvím tvým.
kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
6 Zhřešili jsme i s otci svými, neprávě jsme činili, a bezbožnost páchali.
Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
7 Otcové naši v Egyptě nerozuměli předivným skutkům tvým, aniž pamatovali na množství milosrdenství tvých, ale odporni byli při moři, při moři Rudém.
Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
8 A však vysvobodil je pro jméno své, aby v známost uvedl moc svou.
Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
9 Nebo přimluvil moři Rudému, a vyschlo; i provedl je skrze hlubiny, jako po poušti.
Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
10 A tak zachoval je od ruky toho, jenž jich nenáviděl, a vyprostil je z ruky nepřítele.
Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
11 V tom přikryly vody ty, kteříž je ssužovali, nezůstalo ani jednoho z nich.
Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
12 A ačkoli věřili slovům jeho, a zpívali chválu jeho,
Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
13 Však rychle zapomenuli na skutky jeho, a nečekali na radu jeho;
Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
14 Ale jati jsouce žádostí na poušti, pokoušeli Boha silného na pustinách.
Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
15 I dal jim, čehož se jim chtělo, a však dopustil hubenost na život jejich.
Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
16 Potom, když horlili proti Mojžíšovi v vojště, a Aronovi, svatému Hospodinovu,
Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
17 Otevřevši se země, požřela Dátana, a přikryla zběř Abironovu.
Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
18 A roznícen byl oheň na rotu jejich, plamen spálil bezbožníky.
Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
19 Udělali i tele na Orébě, a skláněli se slitině.
Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
20 A změnivše slávu svou v podobiznu vola, jenž jí trávu,
Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
21 Zapomněli na Boha silného, spasitele svého, kterýž činil veliké věci v Egyptě.
Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
22 A předivné v zemi Chamově, přehrozné při moři Rudém.
zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
23 Pročež řekl, že je vypléní, kdyby se byl Mojžíš, vyvolený jeho, nepostavil v té mezeře před ním, a neodvrátil prchlivosti jeho, aby nehubil.
Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
24 Za tím zošklivili sobě zemi žádanou, nevěříce slovu jeho.
Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
25 A repcíce v staních svých, neposlouchali hlasu Hospodinova.
Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
26 A protož pozdvihl ruky své proti nim, aby je rozmetal po poušti,
Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
27 A aby rozptýlil símě jejich mezi pohany, a rozehnal je do zemí.
kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
28 Spřáhli se také byli s modlou Belfegor, a jedli oběti mrch.
Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
29 A tak dráždili Boha skutky svými, až se na ně obořila rána,
anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
30 Až se postavil Fínes, a pomstu vykonal, i přetržena jest rána ta.
Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
31 Což jest mu počteno za spravedlnost od národu do pronárodu, a až na věky.
Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
32 Opět ho byli popudili při vodách sváru, až se i Mojžíšovi zle stalo pro ně.
Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
33 Nebo k hořkosti přivedli ducha jeho, a pronesl ji rty svými.
pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
34 K tomu nevyplénili ani národů těch, o kterýchž jim byl Hospodin poručil,
Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
35 Ale směšujíce se s těmi národy, naučili se skutkům jejich,
Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
36 A sloužili modlám jejich, kteréž jim byly osídlem.
Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
37 Obětovali zajisté syny své a dcery své ďáblům.
Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
38 A vylili krev nevinnou, krev synů svých a dcer svých, kteréž obětovali trapidlům Kananejským, tak že poškvrněna jest země těmi vraždami.
Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
39 I zmazali se skutky svými, a smilnili činy svými.
Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
40 Protož rozpáliv se v prchlivosti Hospodin na lid svůj, v ošklivost vzal dědictví své.
Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
41 A vydal je v ruce pohanů. I panovali nad nimi ti, jenž je v nenávisti měli,
Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
42 A utiskali je nepřátelé jejich, tak že sníženi jsou pod ruku jejich.
Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
43 Mnohokrát je vysvobozoval, oni však popouzeli ho radou svou, pročež potlačeni jsou pro nepravost svou.
Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
44 A však patřil na úzkost jejich, a slyšel křik jejich.
Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
45 Nebo se rozpomenul na smlouvu svou s nimi, a želel toho podlé množství milosrdenství svých,
Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
46 Tak že naklonil k nim lítostí všecky, kteříž je u vězení drželi.
Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
47 Zachovej nás, Hospodine Bože náš, a shromažď nás z těch pohanů, abychom slavili jméno tvé svaté, a chlubili se v chvále tvé.
Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
48 Požehnaný Hospodin Bůh Izraelský od věků až na věky. Na to rciž všecken lid: Amen, Halelujah.
Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.

< Žalmy 106 >