< Žalmy 105 >

1 Oslavujte Hospodina, ohlašujte jméno jeho, oznamujte mezi národy skutky jeho.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 Zpívejte jemu, žalmy prozpěvujte jemu, rozmlouvejte o všech divných skutcích jeho.
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 Chlubte se jménem svatým jeho; vesel se srdce těch, kteříž hledají Hospodina.
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Hledejte Hospodina a síly jeho, hledejte tváři jeho ustavičně.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Rozpomínejte se na divné skutky jeho, kteréž činil, na zázraky jeho a na soudy úst jeho,
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 Símě Abrahamovo, služebníka jeho, synové Jákobovi, vyvolení jeho.
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 Onť jest Hospodin Bůh náš, na vší zemi soudové jeho.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 Pamatuje věčně na smlouvu svou, na slovo, kteréž přikázal až do tisíce pokolení,
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 Kteréž upevnil s Abrahamem, a na přísahu svou učiněnou Izákovi.
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 Nebo ji utvrdil Jákobovi za ustanovení, Izraelovi za smlouvu věčnou,
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 Pravě: Tobě dám zemi Kananejskou za podíl dědictví vašeho,
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 Ješto jich byl malý počet, malý počet, a ještě v ní byli pohostinu.
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 Přecházeli zajisté z národu do národu, a z království k jinému lidu.
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 Nedopustil žádnému ublížiti jim, ano i krále pro ně trestal, řka:
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 Nedotýkejte se pomazaných mých, a prorokům mým nečiňte nic zlého.
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 Když přivolav hlad na zemi, všecku hůl chleba polámal,
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 Poslal před nimi muže znamenitého, jenž za služebníka prodán byl, totiž Jozefa.
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 Jehož nohy sevřeli pouty, železa podniknouti musil,
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 Až do toho času, když se zmínka stala o něm; řeč Hospodinova zkusila ho.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 Poslav král, propustiti ho rozkázal, panovník lidu svobodna ho učinil.
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 Ustanovil ho pánem domu svého, a panovníkem všeho vládařství svého,
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 Aby vládl i knížaty jeho podlé své líbosti, a starce jeho vyučoval moudrosti.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 Potom všel Izrael do Egypta, a Jákob pohostinu byl v zemi Chamově.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 Kdež rozmnožil Bůh lid svůj náramně, a učinil, aby silnější byl nad nepřátely své.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 Změnil mysl těchto, aby v nenávisti měli lid jeho, a aby ukládali lest o služebnících jeho.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 I poslal Mojžíše slouhu svého, a Arona, kteréhož vyvolil.
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 Kteříž předložili jim slova znamení jeho a zázraků v zemi Chamově.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 Poslal tmu, a zatmělo se, aniž odporná byla slovu jeho.
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 Obrátil vody jejich v krev, a zmořil ryby v nich.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 Vydala země jejich množství žab, i v pokoleních králů jejich.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 Řekl, i přišla směsice žížal, a stěnice na všecky končiny jejich.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 Dal místo deště krupobití, oheň hořící na zemi jejich,
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 Tak že potloukl réví jejich i fíkoví jejich, a zpřerážel dříví v krajině jejich.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 Řekl, i přišly kobylky a chroustů nesčíslné množství.
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 I sežrali všelikou bylinu v krajině jejich, a pojedli úrody země jejich.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 Nadto pobil všecko prvorozené v zemi jejich, počátek všeliké síly jejich.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 Tedy vyvedl své s stříbrem a zlatem, aniž byl v pokoleních jejich, ješto by se poklesl.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 Veselili se Egyptští, když tito vycházeli; nebo byl připadl na ně strach Izraelských.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 Roztáhl oblak k zastírání jich, a oheň k osvěcování noci.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 K žádosti přivedl křepelky, a chlebem nebeským sytil je.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 Otevřel skálu, i tekly vody, a odcházely přes vyprahlá místa jako řeka.
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 Nebo pamětliv byl na slovo svatosti své, k Abrahamovi služebníku svému mluvené.
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 Protož vyvedl lid svůj s radostí, s prozpěvováním vyvolené své.
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 A dal jim země pohanů, a tak úsilí národů dědičně obdrželi,
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 Aby zachovávali ustanovení jeho, a práv jeho ostříhali. Halelujah.
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Žalmy 105 >