< Žalmy 103 >

1 Davidův. Dobrořeč duše má Hospodinu, a všecky vnitřnosti mé jménu svatému jeho.
Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
2 Dobrořeč duše má Hospodinu, a nezapomínej se na všecka dobrodiní jeho,
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
3 Kterýž odpouští tobě všecky nepravosti, kterýž uzdravuje všecky nemoci tvé,
Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
4 Kterýž vysvobozuje od zahynutí život tvůj, kterýž tě korunuje milosrdenstvím a mnohým slitováním,
amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
5 Kterýž nasycuje dobrými věcmi ústa tvá, tak že se obnovuje jako orlice mladost tvá.
amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
6 Èiní, což spravedlivého jest, Hospodin, a soudy všechněm utištěným.
Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
7 Známé učinil Mojžíšovi cesty své, synům Izraelským skutky své.
Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
8 Lítostivý a milostivý jest Hospodin, dlouhoshovívající a mnohého milosrdenství.
Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
9 Nebudeť ustavičně žehrati, ani na věky hněvu držeti.
Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
10 Ne podlé hříchů našich nakládá s námi, ani vedlé nepravostí našich odplacuje nám.
satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
11 Nebo jakož jsou vysoko nebesa nad zemí, tak jest vyvýšené milosrdenství jeho nad těmi, kteříž se ho bojí.
Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
12 A jak daleko jest východ od západu, tak daleko vzdálil od nás přestoupení naše.
monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
13 Jakož se slitovává otec nad dítkami, tak se slitovává Hospodin nad těmi, kteříž se hobojí.
Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
14 Onť zajisté zná slepení naše, v paměti má, že prach jsme.
pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
15 Dnové člověka jsou jako tráva, a jako květ polní, tak kvete.
Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
16 Jakž vítr na něj povane, anť ho není, aniž ho již více pozná místo jeho.
koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
17 Milosrdenství pak Hospodinovo od věků až na věky nad těmi, kteříž se ho bojí, a spravedlnost jeho nad syny synů,
Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
18 Kteříž ostříhají smlouvy jeho, a pamatují na přikázaní jeho, aby je činili.
iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
19 Hospodin na nebesích utvrdil trůn svůj, a kralování jeho nade vším panuje.
Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
20 Dobrořečte Hospodinu andělé jeho, kteříž jste mocní v síle, a činíte slovo jeho, poslušní jsouc hlasu slova jeho.
Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
21 Dobrořečte Hospodinu všickni zástupové jeho, služebníci jeho, kteříž činíte vůli jeho.
Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
22 Dobrořečte Hospodinu všickni skutkové jeho, na všech místech panování jeho. Dobrořeč duše má Hospodinu.
Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.

< Žalmy 103 >