< Žalmy 102 >

1 Modlitba chudého, když sevřín jsa, před Hospodinem vylévá žádosti své. Hospodine, slyš modlitbu mou, a volání mé přijdiž k tobě.
Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
2 Neskrývej tváři své přede mnou, v den ssoužení mého nakloň ke mně ucha svého; když k tobě volám, rychle vyslyš mne.
Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
3 Nebo mizejí jako dým dnové moji, a kosti mé jako ohniště vypáleny jsou.
Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
4 Poraženo jest jako bylina, a usvadlo srdce mé, tak že jsem chleba svého jísti zapomenul.
Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
5 Od hlasu lkání mého přilnuly kosti mé k kůži mé.
Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
6 Podobný jsem učiněn pelikánu na poušti, jsem jako výr na pustinách.
Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
7 Bdím, a jsem jako vrabec osamělý na střeše.
Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
8 Každý den utrhají mi nepřátelé moji, a posměvači moji proklínají mnou.
Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
9 Nebo jídám popel jako chléb, a k nápoji svému slz přiměšuji,
Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
10 Pro rozhněvání tvé a zažžený hněv tvůj; nebo zdvihna mne, hodils mnou.
chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
11 Dnové moji jsou jako stín nachýlený, a já jako tráva usvadl jsem.
Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
12 Ale ty, Hospodine, na věky zůstáváš, a památka tvá od národu až do pronárodu.
Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
13 Ty povstana, smiluješ se nad Sionem, nebo čas jest učiniti milost jemu, a čas uložený přišel.
Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
14 Nebo líbost mají služebníci tvoji v kamení jeho, a nad prachem jeho slitují se,
Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
15 Aby se báli pohané jména Hospodinova, a všickni králové země slávy tvé,
Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
16 Když by Hospodin vzdělal Sion, a ukázal se v slávě své,
Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
17 Když by popatřil k modlitbě poníženého lidu, nepohrdaje modlitbou jejich.
Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
18 Budeť to zapsáno pro budoucí potomky, a lid, kterýž má stvořen býti, chváliti bude Hospodina,
Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
19 Že shlédl s výsosti svatosti své. Hospodin s nebe na zemi že popatřil,
“Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
20 Aby vyslyšel vzdychání vězňů, a rozvázal ty, kteříž již k smrti oddání byli,
kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
21 Aby vypravovali na Sionu jméno Hospodinovo, a chválu jeho v Jeruzalémě,
Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
22 Když se spolu shromáždí národové a království, aby sloužili Hospodinu.
pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
23 Ztrápilť jest na cestě sílu mou, ukrátil dnů mých,
Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
24 Až jsem řekl: Můj Bože, nebeř mne u prostřed dnů mých; od národu zajisté až do pronárodu jsou léta tvá,
Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
25 I prvé nežlis založil zemi, a dílo rukou svých, nebesa.
Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
26 Onať pominou, ty pak zůstáváš; všecky ty věci jako roucho zvetšejí, jako oděv změníš je, a změněny budou.
Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
27 Ty pak jsi tentýž, a léta tvá nikdy nepřestanou.
Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
28 Synové služebníků tvých bydliti budou, a símě jejich zmocní se před tebou.
Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”

< Žalmy 102 >