< Príslovia 8 >

1 Zdaliž moudrost nevolá, a rozumnost nevydává hlasu svého?
Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
2 Na vrchu vysokých míst, u cesty, na rozcestí stojí,
Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
3 U bran, kudy se chodí do města, a kudy se chodí dveřmi, volá, řkuci:
Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
4 Na vásť, ó muži, volám, a hlas můj jest k synům lidským.
Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
5 Poučte se hloupí opatrnosti, a blázni srozumějte srdcem.
Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
6 Poslouchejtež, nebo znamenité věci mluviti budu, a otevření rtů mých pouhou pravdu.
Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
7 Jistě žeť pravdu zvěstují ústa má, a ohavností jest rtům mým bezbožnost.
Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
8 Spravedlivé jsou všecky řeči úst mých, není v nich nic křivého ani převráceného.
Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
9 Všecky pravé jsou rozumějícímu, a přímé těm, kteříž nalézají umění.
Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
10 Přijmětež cvičení mé raději než stříbro, a umění raději než zlato nejvýbornější.
Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
11 Nebo lepší jest moudrost než drahé kamení, tak že jakékoli věci žádostivé vrovnati se jí nemohou.
Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
12 Já moudrost bydlím s opatrností, a umění pravé prozřetelnosti přítomné mám.
Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
13 Bázeň Hospodinova jest v nenávisti míti zlé, pýchy a vysokomyslnosti, i cesty zlé a úst převrácených nenávidím.
Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
14 Má jest rada i šťastný prospěch, jáť jsem rozumnost, a má jest síla.
Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
15 Skrze mne králové kralují, a knížata ustanovují věci spravedlivé.
Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
16 Skrze mne knížata panují, páni i všickni soudcové zemští.
Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
17 Já milující mne miluji, a kteříž mne pilně hledají, nalézají mne.
Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
18 Bohatství a sláva při mně jest, zboží trvánlivé i spravedlnost.
Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
19 Lepší jest ovoce mé než nejlepší zlato, i než ryzí, a užitek můj než stříbro výborné.
Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
20 Stezkou spravedlnosti vodím, prostředkem stezek soudu,
Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
21 Abych těm, kteříž mne milují, přidědila zboží věčné, a poklady jejich naplnila.
Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
22 Hospodin měl mne při počátku cesty své, před skutky svými, přede všemi časy.
“Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
23 Před věky ustanovena jsem, před počátkem, prvé než byla země.
Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
24 Když ještě nebylo propasti, zplozena jsem, když ještě nebylo studnic oplývajících vodami.
Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
25 Prvé než hory založeny byly, než byli pahrbkové, zplozena jsem;
Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
26 Ještě byl neučinil země a rovin, ani začátku prachu okršlku zemského.
lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
27 Když připravoval nebesa, byla jsem tu, když vyměřoval okrouhlost nad propastí;
Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
28 Když upevňoval oblaky u výsosti, když utvrzoval studnice propasti;
pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
29 Když ukládal moři cíl jeho, a vodám, aby nepřestupovaly rozkázaní jeho, když vyměřoval základy země:
pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
30 Tehdáž byla jsem od něho pěstována, a byla jsem jeho potěšení na každý den, anobrž hrám před ním každého času;
Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
31 Hrám i na okršlku země jeho, a rozkoše mé s syny lidskými.
Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
32 A tak tedy, synové, poslechněte mne, nebo blahoslavení jsou ostříhající cest mých.
“Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
33 Poslouchejte cvičení, a nabuďte rozumu, a nerozpakujte se.
Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
34 Blahoslavený člověk, kterýž mne slýchá, bdě u dveří mých na každý den, šetře veřejí dveří mých.
Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
35 Nebo kdož mne nalézá, nalézá život, a dosahuje lásky od Hospodina.
Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
36 Ale kdož hřeší proti mně, ukrutenství provodí nad duší svou; všickni, kteříž mne nenávidí, milují smrt.
Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”

< Príslovia 8 >