< Príslovia 31 >

1 Slova proroctví Lemuele krále, kterýmž vyučovala jej matka jeho.
Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
2 Co dím, synu můj, co, synu života mého? Co, řku, dím, synu slibů mých?
Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
3 Nedávej ženám síly své, ani cest svých těm, kteréž k zahynutí přivodí krále.
Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
4 Ne králům, ó Lemueli, ne králům náleží píti víno, a ne pánům žádost nápoje opojného,
Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
5 Aby pije, nezapomněl na ustanovení, a nezměnil pře všech lidí ssoužených.
kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
6 Dejte nápoj opojný hynoucímu, a víno těm, kteříž jsou truchlivého ducha,
Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
7 Ať se napije, a zapomene na chudobu svou, a na trápení své nezpomíná více.
amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
8 Otevři ústa svá za němého, v při všech oddaných k smrti,
Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
9 Otevři, řku, ústa svá, suď spravedlivě, a veď při chudého a nuzného.
Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
10 Ženu statečnou kdo nalezne? Nebo daleko nad perly cena její.
Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
11 Dověřuje se jí srdce muže jejího; nebo tu kořistí nebude nedostatku.
Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
12 Dobře činí jemu a ne zle, po všecky dny života svého.
Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
13 Hledá pilně vlny a lnu, a dělá šťastně rukama svýma.
Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
14 Jest podobná lodi kupecké, zdaleka přiváží pokrm svůj.
Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
15 Kterážto velmi ráno vstávajíc, dává pokrm čeledi své, a podíl náležitý děvkám svým.
Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
16 Rozsuzuje pole, a ujímá je; z výdělku rukou svých štěpuje i vinici.
Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
17 Přepasuje silou bedra svá, a zsiluje ramena svá.
Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
18 Zakouší, jak jest užitečné zaměstknání její; ani v noci nehasne svíce její.
Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
19 Rukama svýma sahá k kuželi, a prsty svými drží vřeteno.
Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
20 Ruku svou otvírá chudému, a ruce své vztahuje k nuznému.
Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
21 Nebojí se za čeled svou v čas sněhu; nebo všecka čeled její obláčí se v roucho dvojnásobní.
Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
22 Koberce dělá sobě z kmentu, a z zlatohlavu jest oděv její.
Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
23 Patrný jest v branách manžel její, když sedá s staršími země.
Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
24 Plátno drahé dělá, a prodává; též i pasy prodává kupci.
Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
25 Síla a krása oděv její, nestará se o časy potomní.
Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
26 Ústa svá otvírá k moudrosti, a naučení dobrotivosti v jazyku jejím.
Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
27 Spatřuje obcování čeledi své, a chleba zahálky nejí.
Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
28 Povstanouce synové její, blahoslaví ji; manžel její také chválí ji,
Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
29 Říkaje: Mnohé ženy statečně sobě počínaly, ty pak převyšuješ je všecky.
“Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
30 Oklamavatelná jest příjemnost a marná krása; žena, kteráž se bojí Hospodina, tať chválena bude.
Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
31 Dejtež takové z ovoce rukou jejích, a nechať ji chválí v branách skutkové její.
Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.

< Príslovia 31 >