< Príslovia 26 >

1 Jako sníh v létě, a jako déšť ve žni, tak nepřipadá na blázna čest.
Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
2 Jako vrabec přenáší se, a vlaštovice létá, tak zlořečení bez příčiny nedojde.
Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
3 Bič na koně, uzda na osla, a kyj na hřbet blázna.
Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
4 Neodpovídej bláznu podlé bláznovství jeho, abys i ty jemu nebyl podobný.
Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
5 Odpověz bláznu podlé bláznovství jeho, aby sám u sebe nebyl moudrý.
Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
6 Jako by nohy osekal, bezpráví se dopouští ten, kdož svěřuje poselství bláznu.
Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
7 Jakož nejednostejní jsou hnátové kulhavého, tak řeč v ústech bláznů.
Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
8 Jako vložiti kámen do praku, tak jest, když kdo ctí blázna.
Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
9 Trn, kterýž se dostává do rukou opilého, jest přísloví v ústech bláznů.
Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
10 Veliký pán stvořil všecko, a dává odplatu bláznu, i odměnu přestupníkům.
Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
11 Jakož pes navracuje se k vývratku svému, tak blázen opětuje bláznovství své.
Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
12 Spatřil-li bys člověka, an jest moudrý sám u sebe, naděje o bláznu lepší jest než o takovém.
Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
13 Říká lenoch: Lev lítý jest na cestě, lev jest v ulici.
Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
14 Dvéře se obracejí na stežejích svých, a lenoch na lůži svém.
Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
15 Schovává lenivý ruku svou za ňadra; těžko mu vztáhnouti ji k ústům svým.
Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
16 Moudřejší jest lenivý u sebe sám, nežli sedm odpovídajících s soudem.
Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
17 Psa za uši lapá, kdož odcházeje, hněvá se ne v své při.
Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
18 Jako nesmyslný vypouští jiskry a šípy smrtelné,
Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
19 Tak jest každý, kdož oklamává bližního, a říká: Zdaž jsem nežertoval?
ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
20 Když není drev, hasne oheň; tak když nebude klevetníka, utichne svár.
Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
21 Uhel mrtvý k roznícení, a drva k ohni, tak člověk svárlivý k roznícení svady.
Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
22 Slova utrhače jako ubitých, ale však sstupují do vnitřností života.
Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
23 Stříbrná trůska roztažená po střepě jsou rtové protivní a srdce zlé.
Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
24 Rty svými za jiného se staví ten, jenž nenávidí, ale u vnitřnosti své skládá lest.
Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
25 Když se ochotný ukáže řečí svou, nevěř mu; nebo sedmera ohavnost jest v srdci jeho.
Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
26 Přikrývána bývá nenávist chytře, ale zlost její zjevena bývá v shromáždění.
Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
27 Kdo jámu kopá, do ní upadá, a kdo valí kámen, na něj se obrací.
Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
28 Èlověk jazyka ošemetného v nenávisti má ponížené, a ústy úlisnými způsobuje pád.
Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.

< Príslovia 26 >