< Príslovia 22 >

1 Vzácnější jest jméno dobré než bohatství veliké, a přízeň lepší než stříbro a zlato.
Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
2 Bohatý a chudý potkávají se, učinitel obou jest Hospodin.
Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
3 Opatrný vida zlé, vyhne se, ale hloupí předce jdouce, těžkosti docházejí.
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
4 Pokory a bázně Hospodinovy odplata jest bohatství a sláva i život.
Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
5 Trní a osídla jsou na cestě převráceného; kdož ostříhá duše své, vzdálí se od nich.
Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
6 Vyučuj mladého podlé způsobu cesty jeho; nebo když se i zstará, neuchýlí se od ní.
Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
7 Bohatý nad chudými panuje, a vypůjčující bývá služebníkem toho, jenž půjčuje.
Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
8 Kdo rozsívá nepravost, žíti bude trápení; prut zajisté prchlivosti jeho přestane.
Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
9 Oko dobrotivé, onoť požehnáno bude; nebo udílí z chleba svého chudému.
Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
10 Vyvrz posměvače, a odejdeť svada, anobrž přestane svár a lehkost.
Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
11 Kdo miluje čistotu srdce, a v čích rtech jest příjemnost, takového král přítelem bývá.
Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
12 Oči Hospodinovy ostříhají umění, ale snažnosti ošemetného převrací.
Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
13 Říká lenoch: Lev jest vně, naprostřed ulic byl bych zabit.
Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
14 Jáma hluboká ústa postranních; ten, na kohož se hněvá Hospodin, vpadne tam.
Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
15 Bláznovství přivázáno jest k srdci mladého, ale metla kázně vzdálí je od něho.
Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
16 Kdo utiská nuzného, aby rozmnožil své, a dává bohatému, jistotně bude v nouzi.
Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
17 Nakloň ucha svého, a slyš slova moudrých, a mysl svou přilož k učení mému.
Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
18 Nebo to bude utěšenou věcí, jestliže je složíš v srdci svém, budou-li spolu nastrojena ve rtech tvých.
Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
19 Aby bylo v Hospodinu doufání tvé, oznamujiť to dnes. I ty také ostříhej toho.
Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
20 Zdaližť jsem nenapsal znamenitých věcí z strany rad a umění,
Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
21 Aťbych v známost uvedl jistotu řečí pravých, tak abys vynášeti mohl slova pravdy těm, kteříž by k tobě poslali?
malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
22 Nelup nuzného, proto že nuzný jest, aniž potírej chudého v bráně.
Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
23 Nebo Hospodin povede při jejich, a vydře duši těm, kteříž vydírají jim.
pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
24 Nebývej přítelem hněvivého, a s mužem prchlivým neobcuj,
Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
25 Abys se nenaučil stezkám jeho, a nevložil osídla na duši svou.
kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
26 Nebývej mezi rukojměmi, mezi slibujícími za dluhy.
Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
27 Nemáš-li, čím bys zaplatil, proč má kdo bráti lůže tvé pod tebou?
ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
28 Nepřenášej mezníku starodávního, kterýž učinili otcové tvoji.
Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
29 Vídáš-li, že muž snažný v díle svém před králi stává? Nestává před nepatrnými.
Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.

< Príslovia 22 >