< Príslovia 20 >

1 Víno činí posměvače, a nápoj opojný nepokojného; pročež každý, kdož se kochá v něm, nebývá moudrý.
Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
2 Hrůza královská jako řvání mladého lva; kdož ho rozhněvá, hřeší proti životu svému.
Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
3 Přestati od sváru jest to každému ku poctivosti, ale kdožkoli se do nich zapletá, blázen jest.
Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
4 Lenoch neoře pro zimu, pročež žebrati bude ve žni, ale nadarmo.
Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
5 Rada v srdci muže voda hluboká, muž však rozumný dosáhne jí.
Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
6 Větší díl lidí honosí se účinností svou, ale v pravdě takového kdo nalezne?
Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
7 Spravedlivý ustavičně chodí v upřímnosti své; blažení synové jeho po něm.
Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
8 Král sedě na soudné stolici, rozhání očima svýma všecko zlé.
Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
9 Kdo může říci: Očistil jsem srdce své? Èist jsem od hříchu svého?
Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
10 Závaží rozdílná a míra rozdílná, obé to ohavností jest Hospodinu.
Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
11 Po skutcích svých poznáno bývá také i pachole, jest-li upřímé a pravé dílo jeho.
Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
12 Ucho, kteréž slyší, a oko, kteréž vidí, obé to učinil Hospodin.
Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
13 Nemiluj snu, abys nezchudl, otevři oči své, a nasytíš se chlebem.
Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
14 Zlé, zlé, říká ten, kdož kupuje, a odejda, tedy se chlubí.
Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
15 Zlato a množství perel, a nejdražší klínot jsou rtové umělí.
Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
16 Vezmi roucho toho, kterýž slíbil za cizího, a kdo za cizozemku, základ jeho.
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
17 Chutný jest někomu chléb falše, ale potom ústa jeho pískem naplněna bývají.
Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
18 Myšlení radou upevňuj, a s opatrnou radou veď boj.
Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
19 Kdo vynáší tajnost, chodí neupřímě, pročež k lahodícímu rty svými nepřiměšuj se.
Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
20 Kdo zlořečí otci svému neb matce své, zhasne svíce jeho v temných mrákotách.
Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
21 Dědictví rychle z počátku nabytému naposledy nebývá dobrořečeno,
Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
22 Neříkej: Odplatím se zlým; očekávej na Hospodina, a vysvobodí tě.
Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
23 Ohavností jsou Hospodinu závaží rozdílná, a váhy falešné neoblibuje.
Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
24 Od Hospodina jsou krokové muže, ale člověk jak vyrozumívá cestě jeho?
Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
25 Osídlo jest člověku pohltiti věc posvěcenou, a po slibu zase toho vyhledávati.
Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
26 Král moudrý rozptyluje bezbožné, a uvodí na ně pomstu.
Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
27 Duše člověka jest svíce Hospodinova, kteráž zpytuje všecky vnitřnosti srdečné.
Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
28 Milosrdenství a pravda ostříhají krále, a milosrdenstvím podpírá se trůn jeho.
Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
29 Ozdoba mládenců jest síla jejich, a okrasa starců šediny.
Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
30 Modřiny ran jsou lékařství při zlém, a bití vnitřnostem života.
Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.

< Príslovia 20 >