< Príslovia 2 >

1 Synu můj, přijmeš-li slova má, a přikázaní má schováš-li u sebe;
Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
2 Nastavíš-li moudrosti ucha svého, a nakloníš-li srdce svého k opatrnosti;
ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
3 Ovšem, jestliže na rozumnost zavoláš, a na opatrnost zvoláš-li;
ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
4 Budeš-li jí hledati jako stříbra, a jako pokladů pilně vyhledávati jí:
ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
5 Tehdy porozumíš bázni Hospodinově, a známosti Boží nabudeš;
ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
6 Nebo Hospodin dává moudrost, z úst jeho umění a opatrnost.
Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
7 Chová upřímým dlouhověkosti, pavézou jest chodícím v sprostnosti,
Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
8 Ostříhaje stezek soudu; on cesty svatých svých ostříhá.
pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
9 Tehdy porozumíš spravedlnosti a soudu, a upřímosti i všeliké cestě dobré,
Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
10 Když vejde moudrost v srdce tvé, a umění duši tvé se zalíbí.
Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
11 Prozřetelnost ostříhati bude tebe, a opatrnost zachová tě,
Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
12 Vysvobozujíc tě od cesty zlé, a od lidí mluvících věci převrácené,
Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
13 Kteříž opouštějí stezky přímé, aby chodili po cestách tmavých,
amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
14 Kteříž se veselí ze zlého činění, plésají v převrácenostech nejhorších,
amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
15 Jejichž stezky křivolaké jsou, anobrž zmotaní jsou na cestách svých;
Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
16 Vysvobozujíc tě i od ženy postranní, od cizí, kteráž řečmi svými lahodí,
Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
17 Kteráž opouští vůdce mladosti své, a na smlouvu Boha svého se zapomíná;
amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
18 K smrti se zajisté nachyluje dům její, a k mrtvým stezky její;
Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
19 Kteřížkoli vcházejí k ní, nenavracují se zase, aniž trefují na cestu života;
Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
20 Abys chodil po cestě dobrých, a stezek spravedlivých abys ostříhal.
Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
21 Nebo upřímí bydliti budou v zemi, a pobožní zůstanou v ní;
Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
22 Bezbožní pak z země vyťati budou, a přestupníci vykořeněni budou z ní.
Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.

< Príslovia 2 >