< Príslovia 18 >

1 Svémyslný hledá toho, což se jemu líbí, a ve všelijakou věc plete se.
Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
2 Nezalibuje sobě blázen v rozumnosti, ale v tom, což zjevuje srdce jeho.
Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
3 Když přijde bezbožný, přichází také pohrdání, a s lehkomyslným útržka.
Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
4 Slova úst muže vody hluboké, potok rozvodnilý pramen moudrosti.
Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
5 Přijímati osobu bezbožného není dobré, abys převrátil spravedlivého v soudu.
Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
6 Rtové blázna směřují k svadě, a ústa jeho bití se domluví.
Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
7 Ústa blázna k setření jemu, a rtové jeho osídlem duši jeho.
Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
8 Slova utrhače jsou jako ubitých, ale však sstupují do vnitřností života.
Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
9 Také ten, kdož jest nedbalý v práci své, bratr jest mrhače.
Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
10 Věže pevná jest jméno Hospodinovo; k němu se uteče spravedlivý, a bude povýšen.
Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
11 Zboží bohatého jest město pevné jeho, a jako zed vysoká v mysli jeho.
Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
12 Před setřením vyvyšuje se srdce člověka, ale před povýšením bývá ponížení.
Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
13 Kdož odpovídá něco, prvé než vyslyší, počítá se to za bláznovství jemu a za lehkost.
Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
14 Duch muže snáší nemoc svou, ducha pak zkormouceného kdo snese?
Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
15 Srdce rozumného dosahuje umění, a ucho moudrých hledá umění.
Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
16 Dar člověka uprostranňuje jemu, a před oblíčej mocných přivodí jej.
Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
17 Spravedlivý zdá se ten, kdož jest první v své při, ale když přichází bližní jeho, tedy stihá jej.
Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
18 Los pokojí svady, a mezi silnými rozeznává.
Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
19 Bratr křivdou uražený tvrdší jest než město nedobyté, a svárové jsou jako závora u hradu.
Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
20 Ovocem úst jednoho každého nasyceno bývá břicho jeho, úrodou rtů svých nasycen bude.
Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
21 Smrt i život jest v moci jazyka, a ten, kdož jej miluje, bude jísti ovoce jeho.
Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
22 Kdo nalezl manželku, nalezl věc dobrou, a navážil lásky od Hospodina.
Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
23 Poníženě mluví chudý, ale bohatý odpovídá tvrdě.
Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
24 Ten, kdož má přátely, má se míti přátelsky, poněvadž přítel bývá vlastnější než bratr.
Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.

< Príslovia 18 >