< Príslovia 10 >

1 Syn moudrý obveseluje otce, ale syn bláznivý zámutkem jest matce své.
Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
2 Neprospívají pokladové bezbožně nabytí, ale spravedlnost vytrhuje od smrti.
Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
3 Nedopustí lačněti Hospodin duši spravedlivého, statek pak bezbožných rozptýlí.
Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
4 K nouzi přivodí ruka lstivá, ruka pak pracovitých zbohacuje.
Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
5 Kdo shromažďuje v létě, jest syn rozumný; kdož vyspává ve žni, jest syn, kterýž hanbu činí.
Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
6 Požehnání jest nad hlavou spravedlivého, ale ústa bezbožných přikrývají ukrutnost.
Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
7 Památka spravedlivého požehnaná, ale jméno bezbožných smrdí.
Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
8 Moudré srdce přijímá přikázaní, ale blázen od rtů svých padne.
Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
9 Kdo chodí upřímě, chodí doufanlivě; kdož pak převrací cesty své, vyjeven bude.
Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
10 Kdo mhourá okem, uvodí nesnáz; a kdož jest bláznivých rtů, padne.
Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
11 Pramen života jsou ústa spravedlivého, ale ústa bezbožných přikrývají ukrutnost.
Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
12 Nenávist vzbuzuje sváry, ale láska přikrývá všecka přestoupení.
Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
13 Ve rtech rozumného nalézá se moudrost, ale kyj na hřbetě blázna.
Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
14 Moudří skrývají umění, úst pak blázna blízké jest setření.
Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
15 Zboží bohatého jest město pevné jeho, ale nouze jest chudých setření.
Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
16 Práce spravedlivého jest k životu, nábytek pak bezbožných jest k hříchu.
Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
17 Stezkou života jde, kdož přijímá trestání; ale kdož pohrdá domlouváním, bloudí.
Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
18 Kdož přikrývá nenávist rty lživými, i kdož uvodí v lehkost, ten blázen jest.
Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
19 Mnohé mluvení nebývá bez hříchu, kdož pak zdržuje rty své, opatrný jest.
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
20 Stříbro výborné jest jazyk spravedlivého, ale srdce bezbožných za nic nestojí.
Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
21 Rtové spravedlivého pasou mnohé, blázni pak pro bláznovství umírají.
Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
22 Požehnání Hospodinovo zbohacuje, a to beze všeho trápení.
Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
23 Za žert jest bláznu činiti nešlechetnost, ale muž rozumný moudrosti se drží.
Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
24 Èeho se bojí bezbožný, to přichází na něj; ale čehož žádají spravedliví, dává Bůh.
Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
25 Jakož pomíjí vichřice, tak nestane bezbožníka, spravedlivý pak jest základ stálý.
Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
26 Jako ocet zubům, a jako dým očima, tak jest lenivý těm, kteříž jej posílají.
Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
27 Bázeň Hospodinova přidává dnů, léta pak bezbožných ukrácena bývají.
Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
28 Očekávání spravedlivých jest potěšení, naděje pak bezbožných zahyne.
Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
29 Silou jest upřímému cesta Hospodinova, a strachem těm, kteříž činí nepravost.
Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
30 Spravedlivý na věky se nepohne, bezbožní pak nebudou bydliti v zemi.
Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
31 Ústa spravedlivého vynášejí moudrost, ale jazyk převrácený vyťat bude.
Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32 Rtové spravedlivého znají, což jest Bohu libého, ústa pak bezbožných převrácené věci.
Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.

< Príslovia 10 >