< Príslovia 1 >

1 Přísloví Šalomouna syna Davidova, krále Izraelského,
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 Ku poznání moudrosti a cvičení, k vyrozumívání řečem rozumnosti,
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 K dosažení vycvičení v opatrnosti, spravedlnosti, soudu a toho, což pravého jest,
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 Aby dána byla hloupým důmyslnost, mládenečku umění a prozřetelnost.
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 Když poslouchati bude moudrý, přibude mu umění, a rozumný bude vtipnější,
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 K srozumění podobenství, a výmluvnosti řeči moudrých a pohádkám jejich.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 Bázeň Hospodinova jest počátek umění, moudrostí a cvičením pohrdají blázni.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Poslouchej, synu můj, cvičení otce svého, a neopouštěj naučení matky své.
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 Neboť to přidá příjemnosti hlavě tvé, a bude zlatým řetězem hrdlu tvému.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 Synu můj, jestliže by tě namlouvali hříšníci, nepřivoluj.
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 Jestliže by řekli: Poď s námi, úklady čiňme krvi, skryjeme se proti nevinnému bez ostýchání se;
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 Sehltíme je jako hrob za živa, a v cele jako ty, jenž sstupují do jámy; (Sheol h7585)
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
13 Všelijakého drahého zboží dosáhneme, naplníme domy své loupeží;
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 Vrz los svůj mezi nás, měšec jeden budeme míti všickni:
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 Synu můj, nevycházej na cestu s nimi, zdrž nohu svou od stezky jejich;
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 Nebo nohy jejich ke zlému běží, a pospíchají k vylévání krve.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 Jistě, že jakož nadarmo roztažena bývá sít před očima jakéhokoli ptactva,
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 Tak tito proti krvi své ukládají, skrývají se proti dušem svým.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Takovéť jsou cesty každého dychtícího po zisku, duši pána svého uchvacuje.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 Moudrost vně volá, na ulicech vydává hlas svůj.
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 V největším hluku volá, u vrat brány, v městě, a výmluvnosti své vypravuje, řka:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 Až dokud hloupí milovati budete hloupost, a posměvači posměch sobě libovati, a blázni nenáviděti umění?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Obraťtež se k domlouvání mému. Hle, vynáším vám ducha svého, a v známost vám uvodím slova svá.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Poněvadž jsem volala, a odpírali jste; vztahovala jsem ruku svou, a nebyl, kdo by pozoroval,
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 Anobrž strhli jste se všeliké rady mé, a trestání mého jste neoblíbili:
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 Pročež i já v bídě vaší smáti se budu, posmívati se budu, když přijde to, čehož se bojíte,
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 Když přijde jako hrozné zpuštění to, čehož se bojíte, a bída vaše jako bouře nastane, když přijde na vás trápení a ssoužení.
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Tehdy volati budou ke mně, a nevyslyším; ráno hledati mne budou, a nenaleznou mne.
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 Proto že nenáviděli umění, a bázně Hospodinovy nevyvolili,
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 Aniž povolili radě mé, ale pohrdali všelikým domlouváním mým.
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 Protož jísti budou ovoce skutků svých, a radami svými nasyceni budou.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 Nebo pokoj hloupých zmorduje je, a štěstí bláznů zahubí je.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 Ale kdož mne poslouchá, bydliti bude bezpečně, pokoj maje před strachem zlých věcí.
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

< Príslovia 1 >