< Filipským 2 >
1 Protož jest-li jaké potěšení v Kristu, jest-li které utěšení lásky, jest-li která společnost Ducha svatého, jsou-li která milosrdenství a slitování,
Ngati muli ndi chilimbikitso chilichonse chifukwa cholumikizana ndi Khristu, ngati muli ndi chitonthozo chifukwa cha chikondi chake, ngati muli ndi mtima umodzi mwa Mzimu, ndipo ngati mumakomerana mtima ndi kuchitirana chifundo,
2 Naplňte radost mou v tom, abyste jednostejného smyslu byli, jednostejnou lásku majíce, jednodušní jsouce, jednostejně smýšlejíce,
tsono tsirizani chimwemwe changa pokhala amaganizo ofanana, achikondi chimodzimodzi, amodzi mu mzimu ndi acholinga chimodzinso.
3 Nic nečiňte skrze svár anebo marnou chválu, ale v pokoře jedni druhé za důstojnější sebe majíce.
Musachite kalikonse ndi mtima odzikonda chabe kapena odzitukumula chabe. Koma khalani odzichepetsa ndipo aliyense aziona mnzake ngati womuposa iyeyo.
4 Nehledejte jeden každý svých věcí, ale každý také toho, což jest jiných.
Musamangofuna zokomera inu nokha koma aliyense azifuna zokomeranso ena.
5 Budiž tedy tatáž mysl při vás, jakáž byla při Kristu Ježíši,
Pa ubale wanu wina ndi mnzake, mukhale ndi mtima wofanana ndi wa Khristu Yesu:
6 Kterýž jsa v způsobu Božím, nepoložil sobě toho za loupež rovný býti Bohu,
Iyeyu, pokhala Mulungu ndithu, sanatenge kufanana ndi Mulungu kukhala chinthu choyenera kuchigwiritsa.
7 Ale samého sebe zmařil, způsob služebníka přijav, podobný lidem učiněn.
Koma anadzichepetsa kotheratu nakhala ndi khalidwe ngati la kapolo ndi kukhala munthu ngati anthu ena onse.
8 A v způsobu nalezen jako člověk, ponížil se, poslušný jsa učiněn až do smrti, a to do smrti kříže.
Ndipo pokhala munthu choncho anadzichepetsa yekha ndipo anamvera mpaka imfa yake, imfa yake ya pamtanda!
9 Protož i Bůh povýšil ho nade vše a dal jemu jméno, kteréž jest nad každé jméno,
Choncho Mulungu anamukweza Iye kukhala wapamwamba kwambiri, ndipo anamupatsa dzina loposa dzina lina lililonse
10 Aby ve jménu Ježíše každé koleno klekalo, těch, kteříž jsou na nebesích, a těch, jenž jsou na zemi, i těch, jenž jsou pod zemí,
kuti pakumva dzina la Yesu, bondo lililonse limugwadire, kumwamba ndi pa dziko lapansi ndi pansi pa dziko,
11 A každý jazyk aby vyznával, že Ježíš Kristus jest Pánem v slávě Boha Otce.
ndipo lilime lililonse livomereze kuti Yesu Khristu ndi Ambuye kuchitira ulemu Mulungu Atate.
12 A tak, moji milí, jakož jste vždycky poslušni byli, netoliko v přítomnosti mé, ale nyní mnohem více, když jsem vzdálen od vás, s bázní a s třesením spasení své konejte.
Tsono, abwenzi anga okondedwa, monga mwakhala omvera nthawi zonse, osati pamene ndinali nanu pokha, koma tsopano koposa pamene ndili kutali. Pitirizani kugwira ntchito ya chipulumutso chanu mwa mantha ndi kunjenjemera,
13 Bůh zajisté jest, kterýž působí v vás i chtění i skutečné činění, podle dobře libé vůle své.
pakuti ndi Mulungu amene amagwira ntchito mwa inu kuti mufune ndi kuchita zimene zimamukondweretsa Iyeyo.
14 Všecko pak čiňte bez reptání a bez pochybování,
Muzichita zonse mosawiringula kapena mosatsutsapo,
15 Abyste byli bez úhony, a upřímí synové Boží, bez obvinění uprostřed národu zlého a převráceného; mezi kterýmižto svěťte jakožto světla na světě,
kuti mukhale wopanda cholakwa ndi angwiro, ana a Mulungu wopanda cholakwika mu mʼbado uno wachinyengo ndi wosocheretsa. Mukatero mudzawala pakati pawo ngati nyenyezi zakumwamba
16 Slovo života zachovávajíce, k chloubě mé v den Kristův, aby bylo vidíno, že jsem ne nadarmo běžel, ani nadarmo pracoval.
powawuza mawu amoyo. Ndipo ine ndidzatha kunyadira pa tsiku la Khristu kuti sindinathamange kapena kugwira ntchito pachabe.
17 A bychť pak i obětován byl pro obět a službu víře vaší, raduji se a spolu raduji se se všemi vámi.
Koma ngakhale ndikuthiridwa ngati nsembe ya chakumwa yoperekedwa pa nsembe ndi pa utumiki wochokera mʼchikhulupiriro chanu, ndine wokondwa ndi wosangalala pamodzi ndi inu nonse.
18 A též i vy radujte se a spolu radujte se se mnou.
Chomwechonso, inu khalani okondwa ndi osangalala nane pamodzi.
19 Mámť pak naději v Kristu Ježíši, že Timotea brzy pošli vám, abych i já pokojné mysli byl, zvěda, kterak vy se máte.
Ngati Ambuye Yesu alola, ndikukhulupirira kuti ndidzamutuma Timoteyo msanga kwanuko, kuti mwina ndingadzasangalale ndikadzamva za moyo wanu.
20 Nebo žádného tak jednomyslného nemám, kterýž by tak vlastně o vaše věci pečoval.
Ndilibenso wina monga iyeyu amene ali ndi chidwi chenicheni pa za moyo wanu.
21 Všickni zajisté svých věcí hledají, a ne těch, kteréž jsou Krista Ježíše.
Pakuti aliyense amangofuna zokomera iye yekha osati zokomera Yesu Khristu.
22 Ale jej zkušeného býti víte, podle toho, že jakož syn s otcem se mnou přisluhoval v evangelium.
Koma inu mukudziwa kuti Timoteyo wadzionetsa yekha, chifukwa watumikira ndi ine pa ntchito ya Uthenga Wabwino monga mwana ndi abambo ake.
23 Tohoť hle, naději mám, že pošli, jakž jen porozumím, co se bude díti se mnou.
Choncho ndikuyembekezera kumutuma msanga ndikangodziwa mmene zinthu zanga ziyendere.
24 Mámť pak naději v Pánu, že i sám brzo k vám přijdu.
Ndipo ndikukhulupirira kuti Ambuye akalola ine mwini ndidzafikanso kwanuko posachedwapa.
25 Ale zdálo se mi za potřebné Epafrodita, bratra a pomocníka a spolurytíře mého, vašeho pak apoštola i služebníka, v potřebě mé poslati k vám,
Koma ndikuganiza kuti nʼkofunika kuti ndikutumizireni mʼbale wanga Epafrodito, mtumiki mnzanga ndi msilikali mnzanga, amenenso ndi mtumiki wanu amene munamutumiza kuti adzandithandize pa zosowa zanga.
26 Poněvadž takovou měl žádost vás všecky viděti, a velmi těžek nad tím byl, že jste o něm slyšeli, že by byl nemocen.
Pakuti akukulakalakani nonsenu ndipo akusauka mu mtima chifukwa munamva kuti akudwala.
27 A bylť jest jistě nemocen, i blízek smrti, ale Bůh se nad ním smiloval, a ne nad ním toliko, ale i nade mnou, abych zámutku na zámutek neměl.
Zoonadi ankadwala ndipo anatsala pangʼono kumwalira. Koma Mulungu anamuchitira chifundo, ndipo sanangomuchitira chifundo iye yekhayu komanso ine, kuti chisoni changa chisachuluke.
28 Protož tím spěšněji poslal jsem ho k vám, abyste, vidouce jej zase, zradovali se, a já abych byl bez zámutku.
Choncho khumbo langa lofulumiza kumutumiza lakula, kuti pamene mumuonenso musangalale komanso kuti nkhawa yanga ichepe.
29 Protož přijmětež jej v Pánu se vší radostí, a mějte takové v uctivosti.
Mulandireni mwa Ambuye ndi chimwemwe chachikulu, ndipo anthu onga iyeyu muziwachitira ulemu.
30 Neboť jest pro dílo Kristovo až k smrti se přiblížil, opováživ se života svého, jedné aby doplnil to, v čemž jste vy měli nedostatek při posloužení mně.
Iyeyu anatsala pangʼono kufa chifukwa cha ntchito ya Khristu, anayika moyo pa chiswe kuti akwaniritse thandizo limene inu simukanatha.