< Obadiáš 1 >

1 Vidění Abdiášovo. Takto praví Panovník Hospodin o zemi Idumejské: Pověst jsme slyšeli od Hospodina, a legáta k národům vyslaného: Nuže, povstaňmež k boji proti ní.
Masomphenya a Obadiya. Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti, Tamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti, “Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”
2 Aj, způsobím to, abys byl nejšpatnější mezi národy, a abys byl v náramném pohrdání.
“Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina; udzanyozedwa kwambiri.
3 Pýcha srdce tvého zklamá tě, ó ty, kterýž bydlíš v rozsedlinách skalních, v převysokém obydlí svém, říkaje v srdci svém: Kdož by mne strhl na zem?
Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali, iwe amene umanena mu mtima mwako kuti, ‘Ndani anganditsitse pansi?’
4 Bys pak vysoko udělal jako orlice, nýbrž bys mezi hvězdami položil hnízdo své, i odtud strhnu tě, praví Hospodin.
Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
5 Kterak jsi popléněn? Zdali zloději přišli na tebe? Zdali loupežníci noční? Zdaliž by kradli přes spotřebu svou? Kdyby ti, kteříž zbírají víno, přišli na tebe, zdaž by nepozůstavili aspoň paběrků?
“Anthu akuba akanabwera kwa iwe, kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku, aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe! Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha? Ngati anthu othyola mphesa akanafika, kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
6 Jakť jsou vystiženy věci Ezau, vyhledáni pokladové jeho!
Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse, chuma chake chobisika chidzabedwa!
7 Až ku pomezí vystrčí tě všickni, s kterýmiž smlouvu máš; podvedou tě, zmocní se tebe ti, s nimiž pokoj máš; náchlebníci tvoji udělajíť ránu zrádně, již nebude lze vyrozuměti.
Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire; abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa; amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha, koma iwe sudzazindikira zimenezi.”
8 Zdaliž v ten den, praví Hospodin, nevyhladím moudrých z země Idumejské, a rozumných s hory Ezau?
Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo, kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu, anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?
9 I budou se děsiti udatní tvoji, ó Temane, proto, že poraženi jsouce, vypléněni budou všickni s hory Ezau.
Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha, ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau adzaphedwa pa nkhondo.
10 Pro nátisk bratru tvému Jákobovi činěný přikryje tě hanba, a vypléněn budeš na věčnost.
Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo, udzakhala wamanyazi; adzakuwononga mpaka muyaya.
11 Stál jsi v ten den naproti, a když zajímali cizí vojsko jeho, a když cizozemci vcházeli do bran jeho, a o Jeruzalém metali losy, ty jsi také byl jako jeden z nich.
Pamene adani ankamulanda chuma chake pamene alendo analowa pa zipata zake ndi kuchita maere pa Yerusalemu, pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.
12 Nedívejž se tedy na den bratra svého, na den zajetí jeho, aniž se vesel nad syny Judskými v den zahynutí jejich, aniž pyšně mluv ústy svými v den uzkosti.
Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako pa nthawi ya tsoka lake, kapena kunyogodola Ayuda chifukwa cha chiwonongeko chawo, kapena kuwaseka pa nthawi ya mavuto awo.
13 Nevcházej do brány lidu mého v den bídy jejich, aniž se dívej trápení jeho v den bídy jeho, a nechtěj sahati na statek jeho v den bídy jeho.
Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga pa nthawi ya masautso awo, kapena kuwanyogodola pa tsiku la tsoka lawo, kapena kulanda chuma chawo pa nthawi ya masautso awo.
14 Aniž stůj při mezeře, abys hubil ty, kteříž z nich ucházejí, aniž vydávej nepříteli v moc těch, kteříž z nich pozůstali v den úzkosti.
Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu kuti uphe Ayuda othawa, kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka pa nthawi ya mavuto awo.”
15 Nebo blízko jest den Hospodinův proti všechněm těm národům. Jakž jsi činil, tak se stane tobě, odplata tvá navrátí se na hlavu tvou.
“Tsiku la Yehova layandikira limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu. Adzakuchitira zomwe unawachitira ena; zochita zako zidzakubwerera wekha.
16 Nebo poněvadž vy na mé hoře svaté píti bedete, nadtoť píti budou všickni národové ustavičně. Píti, pravím, a požírati budou, až budou, jako by jich nebylo.
Iwe unamwa pa phiri langa loyera, koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza; iwo adzamwa ndi kudzandira ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.
17 Na hoře pak Sion bude vysvobození, a bude svatá, a tak dědičně držeti bude dům Jákobův dědictví svá.
Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso; phirilo lidzakhala lopatulika, ndipo nyumba ya Yakobo idzalandira cholowa chake.
18 I bude dům Jákobův oheň, a dům Jozefův plamen, dům pak Ezau plevy, i rozpálí se na ně a sehltí je, aniž kdo pozůstane z domu Ezau; nebo Hospodin mluvil.
Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto; nyumba ya Esau idzasanduka chiputu, ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza. Sipadzakhala anthu opulumuka kuchokera mʼnyumba ya Esau.” Yehova wayankhula.
19 A tak děditi budou v krajině polední s horou Ezau, i v rovině s Filistinskými; vládnouti také budou krajinou Efraimovou i krajinou Samařskou, a Beniaminovou i Galádskou.
Anthu ochokera ku Negevi adzakhala ku mapiri a Esau, ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri adzatenga dziko la Afilisti. Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya, ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.
20 I zajaté vojsko toto synů Izraelských v tom, což bylo Kananejských až do Sarepty, zajatí pak Jeruzalémští v tom, což jest na konci panství, děditi budou s městy na poledne.
Aisraeli amene ali ku ukapolo adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati; a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi adzalandira mizinda ya ku Negevi.
21 I vstoupí vysvoboditelé na horu Sion, aby soudili horu Ezau, a tak bude Hospodinovo království.
Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni ndipo adzalamulira mapiri a Esau. Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.

< Obadiáš 1 >