< 4 Mojžišova 28 >

1 Mluvil také Hospodin k Mojžíšovi, řka:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Přikaž synům Izraelským a rci jim: Obětí mých, chleba mého, v obětech mých ohnivých u vůni spokojující mne, nezanedbávejte mi přinášeti v čas k tomu vyměřený.
“Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
3 Díš tedy jim: Tato jest obět ohnivá, kterouž obětovati budete Hospodinu: Beránky roční bez poškvrny dva, každého dne v obět zápalnou ustavičně.
Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
4 Beránka jednoho obětovati budeš ráno, a beránka druhého obětovati budeš k večerou.
Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
5 Desátý také díl míry efi mouky bělné, v obět suchou, zadělané olejem nejčistším, čtvrtou částkou míry hin.
Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
6 Ta jest obět zápalná ustavičná, kteráž obětována jest na hoře Sinai u vůni příjemnou, v obět ohnivou Hospodinu.
Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
7 A obět mokrá její, čtvrtý díl míry hin na každého beránka; v svatyni obětuj obět mokrou silného nápoje Hospodinu.
Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
8 Beránka pak druhého obětovati budeš k večerou, tak jako obět suchou jitřní, a jako obět mokrou její obětovati budeš v obět ohnivou, u vůni spokojující Hospodina.
Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
9 Dne také sobotního dva beránky roční bez poškvrny, a dvě desetiny mouky bělné, olejem zadělané v obět suchou s obětí její mokrou.
“‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
10 Ta bude obět zápalná sobotní každého dne sobotního, mimo zápalnou obět ustavičnou a mokrou obět její.
Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
11 Také na nov měsíců vašich obětovati budete obět zápalnou Hospodinu, volky mladé dva, skopce jednoho, beránků ročních bez poškvrny sedm;
“Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
12 A tři desetiny mouky bělné, olejem zadělané v obět suchou při každém volku, a dvě desetiny mouky bělné, olejem zadělané v obět suchou při každém skopci;
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
13 A jednu desetinu mouky bělné olejem zadělané v obět suchou při každém beránku, k oběti zápalné u vůni příjemnou, v obět ohnivou Hospodinu.
ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
14 Tyto pak oběti mokré jejich z vína: Půl míry hin bude při každém volku, a třetí částka hin při skopci, a čtvrtá částka hin při každém beránku. Ta jest obět zápalná k nov měsíci, každého měsíce přes celý rok.
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
15 Kozla také jednoho v obět za hřích, mimo obět ustavičnou, obětovati budete Hospodinu s mokrou obětí jeho.
Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
16 Měsíce pak prvního, čtrnáctý den téhož měsíce velikanoc bude Hospodinu,
“‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
17 A v patnáctý den téhož měsíce slavnost; za sedm dní chleby nekvašené jísti budete.
Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
18 Prvního dne shromáždění svaté bude, žádného díla robotného nebudete dělati v něm.
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
19 Obětovati pak budete obět ohnivou v zápal Hospodinu, volky mladé dva, skopce jednoho, a sedm beránků ročních; bez poškvrny budou.
Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
20 A suchou obět při nich, totiž mouku bělnou, olejem zadělanou, tři desetiny při každém volku, a dvě desetiny při každém skopci obětovati budete.
Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
21 A jednu desetinu obětovati budeš při každém beránku z těch sedmi beránků,
Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
22 A kozla v obět za hřích jednoho k očištění vás.
Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
23 Mimo obět zápalnou jitřní, kteráž jest obět ustavičná, obětovati budete to.
Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
24 Tak obětovati budete každého dne za těch sedm dní pokrm oběti ohnivé, u vůni spokojující Hospodina, mimo zápalnou obět ustavičnou, a obět mokrou její.
Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
25 Sedmého pak dne shromáždění svaté míti budete, žádného díla robotného nebudete dělati.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
26 V den také prvotin, když obětovati budete novou obět suchou Hospodinu, vyplníc téhodny vaše, shromáždění svaté míti budete; žádného díla robotného nebudete dělati.
“‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
27 A obětovati budete obět zápalnou, u vůni spokojující Hospodina, volky mladé dva, skopce jednoho, beránků ročních sedm,
Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
28 A obět suchou jejich, mouky bělné olejem zadělané tři desetiny při každém volku, dvě desetiny při každém skopci,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
29 Jednu desetinu při každém beránku z těch sedmi beránků,
Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
30 Kozla jednoho k očištění vašemu.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
31 To mimo obět zápalnou ustavičnou, a obět suchou její obětovati budete; bez poškvrny ať jsou s obětmi svými mokrými.
Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.

< 4 Mojžišova 28 >