< 4 Mojžišova 26 >

1 I stalo se po té ráně, že mluvil Hospodin k Mojžíšovi a Eleazarovi, synu Arona kněze, řka:
Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni,
2 Sečtěte všecko množství synů Izraelských, od dvadcítiletých a výše po domích otců jejich, všecky, kteříž by mohli jíti k boji v Izraeli.
“Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.”
3 Tedy mluvil Mojžíš a Eleazar kněz k nim na polích Moábských, při Jordánu proti Jerichu, řka:
Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti,
4 Sečtěte lid od dvadceti let majících a výše, jakž rozkázal Hospodin Mojžíšovi a synům Izraelským, kteříž byli vyšli z země Egyptské.
“Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.” Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:
5 Ruben prvorozený byl Izraelův. Synové Rubenovi: Enoch, z něhož pošla čeled Enochitská; Fallu, z něhož čeled Fallutská;
Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi: kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki; kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;
6 Ezron, z něhož čeled Ezronitská; Charmi, z něhož čeled Charmitská.
kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.
7 Ty jsou čeledi Rubenovy. A bylo jich sečtených čtyřidceti tři tisíce, sedm set a třidceti.
Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.
8 A syn Fallův Eliab.
Mwana wa Palu anali Eliabu,
9 Synové pak Eliabovi: Nemuel, a Dátan, a Abiron. To jsou ti, Dátan a Abiron, přední z shromáždění, kteříž se vadili s Mojžíšem a s Aronem v spiknutí Chóre, když odporni byli Hospodinu.
ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova.
10 Pročež otevřela země ústa svá, a požřela je i Chóre, tehdáž když zemřela ta rota, a oheň spálil těch dvě stě a padesáte mužů, kteříž byli za příklad jiným.
Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo.
11 Synové pak Chóre nezemřeli.
Koma ana a Kora sanafe nawo.
12 Synové Simeonovi po čeledech svých: Namuel, z něhož čeled Namuelitská; Jamin, z něhož čeled Jaminská; Jachin, z něhož čeled Jachinská;
Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele; kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini; kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;
13 Sohar, z něhož čeled Soharská; Saul, z něhož čeled Saulitská.
kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera; kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.
14 Ty jsou čeledi Simeonovy, jichž bylo dvamecítma tisíců a dvě stě.
Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.
15 Synové Gád po čeledech svých: Sefon, z něhož čeled Sefonitská; Aggi, z něhož čeled Aggitská; Suni, z něhož čeled Sunitská;
Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi: kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni; kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi; kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;
16 Ozni, z něhož čeled Oznitská; Heri, z něhož čeled Heritská;
kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini; kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;
17 Arodi, z něhož čeled Aroditská; Areli, z něhož čeled Arelitská.
kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi; kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.
18 Ty jsou čeledi synů Gád, podlé toho, jakž sečteni jsou, čtyřidceti tisíců a pět set.
Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.
19 Synové Judovi: Her a Onan; ale zemřeli Her i Onan v zemi Kanánské.
Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.
20 Byli pak synové Judovi po čeledech svých: Séla, z něhož čeled Sélanitská; Fáres, z něhož čeled Fáresská; Zára, z něhož čeled Záretská.
Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Sela, fuko la Asera; kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi; kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.
21 Byli pak synové Fáresovi: Ezron, z něhož čeled Ezronitská; Hamul, z něhož čeled Hamulská.
Zidzukulu za Perezi zinali izi: kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.
22 Ty jsou čeledi Judovy, podlé toho, jakž sečteni jsou, sedmdesáte šest tisíců a pět set.
Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.
23 Synové Izacharovi po čeledech svých: Tola, z něhož čeled Tolatská; Fua, z něhož čeled Fuatská;
Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Tola, fuko la Atola; kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;
24 Jasub, z něhož čeled Jasubská; Simron, z něhož čeled Simronská.
kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu. Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.
25 Ty jsou čeledi Izacharovy, podlé toho, jakž sečteni jsou, šedesáte čtyři tisíce a tři sta.
Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.
26 Synové Zabulonovi po čeledech svých: Sared, z něhož čeled Saredská; Elon, z něhož čeled Elonská; Jahelel, z něhož čeled Jahelelská.
Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi; kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni; kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.
27 Ty jsou čeledi Zabulonovy, podlé toho jakž sečteni jsou, šedesáte tisíc a pět set.
Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.
28 Synové Jozefovi po čeledech svých: Manasses a Efraim.
Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:
29 Synové Manassesovi: Machir, z něhož čeled Machirská. A Machir zplodil Galáda, z něhož čeled Galádská.
Zidzukulu za Manase: kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi); kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.
30 Ti jsou synové Galád: Jezer, z něhož čeled Jezerská; Helek, z něhož čeled Helekitská;
Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi; kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri; kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;
31 Asriel, z něhož čeled Asrielská; Sechem, z něhož čeled Sechemská;
kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli; kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;
32 Semida, z něhož čeled Semidatská; Hefer, z něhož čeled Heferská.
kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida; kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.
33 A Salfad, syn Heferův, neměl synů, než toliko dcery, jichž jsou tato jména: Mahla, Noa, Hegla, Melcha a Tersa.
(Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)
34 Ty jsou čeledi Manassesovy, a načteno jich padesáte dva tisíce a sedm set.
Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.
35 Ale synové Efraimovi po čeledech svých: Sutala, z něhož čeled Sutalitská; Becher, z něhož čeled Becherská; Tehen, z něhož čeled Tehenská.
Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi; kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela; kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri; kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.
36 A ti jsou synové Sutalovi: Heran, z něhož čeled Heranská.
Zidzukulu za Sutela zinali izi: kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.
37 Ty jsou čeledi synů Efraimových, podlé toho, jakž sečteni jsou, třidceti dva tisíce a pět set. Ti jsou synové Jozefovi po čeledech svých.
Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500. Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.
38 Synové pak Beniaminovi po čeledech svých: Béla, z něhož čeled Bélitská; Asbel, z něhož čeled Asbelská; Ahiram, z něhož čeled Ahiramská;
Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Bela, fuko la Abela; kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli; kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;
39 Sufam, z něhož čeled Sufamská; Hufam, z něhož čeled Hufamská.
kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu; kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;
40 Byli pak synové Béla: Ared a Náman; z Ared čeled Aredská, z Náman čeled Námanská.
Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi: kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi; kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;
41 Ti jsou synové Beniaminovi po čeledech svých, podlé toho, jakž sečteni jsou, čtyřidceti pět tisíců a šest set.
Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.
42 Tito pak synové Danovi po čeledech svých: Suham, z něhož čeled Suhamská. Ta jest rodina Danova po čeledech svých.
Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu. Izi zinali zidzukulu za Dani.
43 Všech čeledí Suhamských, jakž sečteni jsou, šedesáte čtyři tisíce a čtyři sta.
Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.
44 Synové Asser po čeledech svých: Jemna, z něhož čeled Jemnitská; Jesui, z něhož čeled Jesuitská;
Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna; kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi; kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;
45 Beria, z něhož čeled Berietská. Synové Beriovi: Heber, z něhož čeled Heberská; Melchiel, z něhož čeled Melchielská.
ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya: kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi; kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;
46 Jméno pak dcery Asser bylo Serach.
(Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)
47 Ty jsou čeledi synů Asser, tak jakž sečteni jsou, padesáte tři tisíce a čtyři sta.
Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.
48 Synové Neftalímovi po čeledech svých: Jasiel, z něhož čeled Jasielská; Guni, z něhož čeled Gunitská;
Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli; kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;
49 Jezer, z něhož čeled Jezerská; Sallem, z něhož čeled Sallemská.
kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri; kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.
50 Ta jest rodina Neftalímova po čeledech svých, tak jakž sečteni jsou, čtyřidceti pět tisíců a čtyři sta.
Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.
51 Ten jest počet synů Izraelských, šestkrát sto tisíců a jeden tisíc, sedm set a třidceti.
Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.
52 Mluvil pak Hospodin k Mojžíšovi, řka:
Yehova anawuza Mose kuti,
53 Těmto rozdělena bude země k dědictví podlé počtu jmen.
“Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo.
54 Většímu počtu větší dědictví dáš, a menšímu menší; jednomu každému vedlé počtu sečtených jeho dáno bude dědictví jeho.
Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa.
55 A však losem ať jest rozdělena země; vedlé jmen pokolení otců svých dědictví vezmou.
Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo.
56 Losem děleno bude dědictví její, buď jich mnoho neb málo.
Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”
57 Tito pak jsou sečteni z Levítů po čeledech svých: Gerson, z něhož čeled Gersonitská; Kahat, z něhož čeled Kahatská; Merari, z něhož čeled Meraritská.
Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa: kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni; kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati; kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.
58 Ty jsou čeledi Léví: Èeled Lebnitská, čeled Hebronitská, čeled Moholitská, čeled Musitská, čeled Choritská. Kahat pak zplodil Amrama.
Awanso anali mabanja a Alevi: banja la Alibini, banja la Ahebroni, banja la Amali, banja la Amusi, fuko la Kora banja la Akohati, (Kohati anali abambo a Amramu.
59 A jméno manželky Amramovy Jochebed, dcera Léví, kteráž se mu narodila v Egyptě; ona pak porodila Amramovi Arona a Mojžíše, a Marii sestru jejich.
Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo.
60 Aronovi pak zrozeni jsou: Nádab a Abiu, Eleazar a Itamar.
Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
61 Ale Nádab a Abiu zemřeli, když obětovali oheň cizí před Hospodinem.
Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).
62 I bylo jich načteno třimecítma tisíců, všech pohlaví mužského zstáří měsíce jednoho a výše; nebo nebyli počteni mezi syny Izraelskými, proto že jim nebylo dáno dědictví mezi syny Izraelskými.
Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.
63 Tito sečteni jsou od Mojžíše a Eleazara kněze; oni sečtli syny Izraelské na polích Moábských při Jordánu, naproti Jerichu.
Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko.
64 Mezi těmito pak nebyl žádný z oněch sečtených od Mojžíše a Arona kněze, když počítali syny Izraelské na poušti Sinai;
Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai;
65 (Nebo řekl byl Hospodin o nich: Smrtí zemrou na poušti; ) a žádný z nich nepozůstal, jediné Kálef, syn Jefonův, a Jozue, syn Nun.
Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.

< 4 Mojžišova 26 >