< 4 Mojžišova 2 >

1 Mluvil také Hospodin k Mojžíšovi a Aronovi, řka:
Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
2 Synové Izraelští klásti se budou jeden každý pod korouhví svou, při praporci domu otců svých; vůkol stánku úmluvy opodál klásti se budou.
“Aisraeli azimanga misasa yawo mozungulira tenti ya msonkhano motalikira pangʼono. Munthu aliyense amange pamene pali mbendera ya fuko lake.”
3 Tito pak rozbijí stany k východní straně: Korouhev vojska Judova po houfích svých, a kníže synů Juda Názon, syn Aminadabův,
Kummawa, kotulukira dzuwa, magulu a msasa wa Yuda amange pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Ayudawo ndi Naasoni mwana wa Aminadabu.
4 A u vojště jeho lidu sečteného sedmdesáte čtyři tisíce a šest set.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 74,600.
5 Podlé něho pak položí se pokolení Izachar, a kníže synů Izachar Natanael, syn Suar,
Fuko la Isakara lidzamanga pafupi ndi Yuda. Mtsogoleri wa gulu la Isakara ndi Netanieli mwana wa Zuwara.
6 A u vojště jeho lidu sečteného padesáte čtyři tisíce a čtyři sta.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 54,400.
7 Pokolení Zabulon podlé nich, a kníže synů Zabulon Eliab, syn Helonův,
Lotsatira lidzakhala fuko la Zebuloni. Mtsogoleri wa gulu la Zebuloni ndi Eliabu mwana wa Heloni.
8 A u vojště jeho lidu sečteného padesáte sedm tisíců a čtyři sta.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 57,400.
9 Summa všech sečtených u vojště Judově sto osmdesáte šest tisíců a čtyři sta, po houfích jejich. Ti napřed potáhnou.
Anthu onse aamuna mʼmisasa ya Yuda, chiwerengero chawo ndi 186,400 monga mwa magulu awo. Iwowo ndiwo aziyamba kusamuka.
10 Korouhev vojska Rubenova klásti se bude ku poledni po houfích svých, a kníže synů Ruben Elisur, syn Sedeurův,
Kummwera kudzakhala magulu a msasa wa Rubeni pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu la Rubeni ndi Elizuri mwana wa Sedeuri.
11 A u vojště jeho lidu sečteného čtyřidceti šest tisíců a pět set.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 46,500.
12 Podlé něho pak položí se pokolení Simeonovo, a kníže synů Simeon Salamiel, syn Surisaddai,
Fuko la Simeoni lidzamanga pafupi ndi Rubeni. Mtsogoleri wa gulu la Simeoni ndi Selumieli mwana wa Zurisadai.
13 A u vojště jeho lidu sečteného padesáte devět tisíců a tři sta.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 59,300.
14 Potom pokolení Gád, a kníže synů Gád Eliazaf, syn Ruelův,
Lotsatira lidzakhala fuko la Gadi. Mtsogoleri wa gulu la Gadi ndi Eliyasafu mwana wa Deuweli.
15 A u vojště jeho lidu sečteného čtyřidceti pět tisíců, šest set a padesáte.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 45,650.
16 Summa všech sečtených u vojště Rubenově sto padesáte a jeden tisíců, čtyři sta a padesáte, po houfích svých. A ti za prvními potáhnou.
Anthu onse aamuna mu msasa wa Rubeni, chiwerengero chawo monga mwa magulu awo, ndi 151,450. Iwowo azikhala achiwiri posamuka.
17 Potom půjde stánek úmluvy s vojskem Levítů u prostřed všeho vojska. Jakýmž pořádkem klásti se budou, takovým potáhnou, každý v svém šiku pod korouhví svou.
Tsono tenti ya msonkhano ndi msasa wa Alevi zidzakhala pakati pa misasayo. Iwo adzasamuka monga momwe anamangira misasa yawo, aliyense pa malo ake pamene pali mbendera yake.
18 Korouhev vojska Efraimova po houfích svých bude k západu, a kníže synů Efraimových Elisama, syn Amiudův,
Kumadzulo kudzakhala magulu a msasa wa Efereimu pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Aefereimuwo ndi Elisama mwana wa Amihudi.
19 A u vojště jeho lidu sečteného čtyřidceti tisíc a pět set.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 40,500.
20 Podlé něho pak položí se pokolení Manassesovo, a kníže synů Manassesových Gamaliel, syn Fadasurův,
Fuko la Manase lidzakhala pafupi ndi Efereimu. Mtsogoleri wa Amanase ndi Gamalieli mwana wa Pedazuri.
21 A u vojště jeho lidu sečteného třidceti dva tisíce a dvě stě.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 32,200.
22 Potom položí se pokolení Beniaminovo, a kníže synů Beniamin Abidan, syn Gedeonův,
Lotsatira lidzakhala fuko la Benjamini. Mtsogoleri wa Abenjamini ndi Abidani mwana wa Gideoni.
23 A u vojště jeho lidu sečteného třidceti pět tisíců a čtyři sta.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 35,400.
24 Summa všech sečtených u vojště Efraimově sto osm tisíců a sto osob, po houfích jejich. A tito za druhými potáhnou.
Anthu onse aamuna mu msasa wa Efereimu, chiwerengero chawo ndi 108,100 monga mwa magulu awo. Iwowo azikhala achitatu posamuka.
25 Korouhev vojska Dan bude k straně půlnoční, po houfích svých, a kníže synů Dan Ahiezer, syn Amisaddai,
Kumpoto kudzakhala msasa wa magulu a Dani pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Adani ndi Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
26 A u vojště jeho lidu sečteného šedesáte dva tisíce a sedm set.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 62,700.
27 Podlé něho položí se pokolení Asser, a kniže Asser Fegiel, syn Ochranův,
Fuko la Aseri lidzamanga pafupi ndi iwowo. Mtsogoleri wa Aaseri ndi Pagieli mwana wa Okirani.
28 A u vojště jeho lidu sečteného čtyřidceti jeden tisíc a pět set.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 41,500.
29 Za nimi pokolení Neftalímovo, a kníže synů Neftalímových Ahira, syn Enanův,
Lotsatira lidzakhala fuko la Nafutali. Mtsogoleri wa Anafutali ndi Ahira mwana wa Enani.
30 A u vojště jeho lidu sečteného padesáte tři tisíce a čtyři sta.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 53,400.
31 Summa všech sečtených u vojště Dan sto padesáte sedm tisíců a šest set. Oni nazad potáhnou při praporcích svých.
Anthu onse aamuna mu msasa wa Dani chiwerengero chawo ndi 157,600. Iwo azidzanyamuka pomaliza, ndi mbendera zawo.
32 Ta jest summa synů Izraelských po domích otců jejich, všech sečtených v celém vojště po houfích jejich, šestkrát sto tisíců, tři tisíce, pět set a padesáte.
Amenewa ndi Aisraeli monga mwa mabanja a makolo awo. Chiwerengero cha Aisraeli onse mʼmisasa chinali 603,550, mwa magulu awo.
33 Levítové pak nejsou počítáni mezi syny Izraelské, jakož přikázal Hospodin Mojžíšovi.
Koma Alevi sanawawerenge pamodzi ndi Aisraeli enawo monga momwe Yehova analamulira Mose.
34 I učinili synové Izraelští všecko; jakž přikázal Hospodin Mojžíšovi, tak rozbijeli stany při korouhvech svých, a tak táhli jeden každý po čeledech svých a po domích otců svých.
Choncho Aisraeli anachita zonse zomwe Yehova analamulira Mose. Umo ndi momwe amamangira misasa yawo pamene panali mbendera zawo, ndipo ankasamuka monga mwa mafuko a makolo awo.

< 4 Mojžišova 2 >