< Malachiáš 1 >

1 Břímě slova Hospodinova proti Izraelovi skrze Malachiáše.
Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.
2 Miluji vás, praví Hospodin, vy pak říkáte: V čem nás miluješ? Zdaliž Ezau nebyl bratr Jákobův? praví Hospodin. A však jsem miloval Jákoba.
Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’” Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo,
3 Ezau pak měl jsem v nenávisti; protož zanechal jsem hor jeho pustých, a dědictví jeho drakům pouště.
koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”
4 Řekne-li Idumejská země: Ochuzeniť jsme, ale navrátíme se zase, a vystavíme místa pustá, takto praví Hospodin zástupů: Oni nechť stavějí, a já budu bořiti. I budou je nazývati pomezím bezbožnosti a lidem, na nějž hněviv bude Hospodin až na věky.
Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.” Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya.
5 Což oči vaše uzří, a vy díte: Veleben buď Hospodin po pomezích Izraelských.
Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’
6 Syn ctí otce, a služebník pána svého. Protož jestližeť jsem já otec, kdež jest čest má? A jestliže jsem pán, kde jest bázeň má? Vám to mluví Hospodin zástupů, ó kněží, kteříž sobě zlehčujete jméno mé. A však říkáte: V čem zlehčujeme jméno tvé?
“Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’
7 Kteříž přinášejíce na oltář můj obět poškvrněnou, říkáte: Èímž jsme tě poškvrnili? Tím, když říkáte: Stůl Hospodinův v pohrdání jest.
“Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’ “Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka.
8 Nebo když přivodíte slepé k obětování, což to není nic zlého? A když přivodíte chromé aneb nemocné, což to není nic zlého? Daruj je medle knížeti svému, zalíbíš-li mu se tím, a přijme-li tvář tvou, praví Hospodin zástupů.
Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
9 A protož nyní kořtež se tváři Boha silného, aby nám milost učinil. Ale když to z rukou vašich jest, přijme-liž kterého z vás oblíčej? praví Hospodin zástupů.
“Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
10 Anobrž kdo jest mezi vámi, aby zavřel dvéře, aneb zapálil na oltáři mém darmo? Nemámť v vás žádné líbosti, praví Hospodin zástupů, a oběti nepřijmu z ruky vaší.
“Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu.
11 Nebo od východu slunce až na západ jeho veliké bude jméno mé mezi národy, a na všelikém místě kadění přinášíno bude jménu mému, a obět čistá. Veliké zajisté jméno mé bude mezi národy, praví Hospodin zástupů,
Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
12 Ačkoli vy ho poškvrňujete, když říkáte: Stůl Hospodinův v pohrdání jest, a což kladeno bývá na něj, že jest chaterný pokrm.
“Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’
13 Říkáte také: Ach, větší práce, ješto byste to zdmýchnouti mohli, praví Hospodin zástupů. Nebo přinášíte to, což jest vydřeno, a chromé i nemocné, přinášejíce dar. To-liž mám přijímati z ruky vaší? praví Hospodin.
Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova.
14 Anobrž zlořečený jest fortelný, kterýž maje v svém stádě samce, činí slib, a obětuje Pánu to, což jest churavého. Nebo král veliký já jsem, praví Hospodin zástupů, a jméno mé jest hrozné mezi národy.
“Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’”

< Malachiáš 1 >