< 3 Mojžišova 7 >

1 Tento pak bude řád oběti za provinění; svatá svatých jest.
“‘Malamulo a nsembe yopepesera kupalamula imene ndi nsembe yopatulika kwambiri ndi awa:
2 Na kterémž místě zabijí se obět zápalná, na témž zabijí i obět za vinu, a pokropí krví její oltáře svrchu vůkol.
Nsembe yopepesera machimo iziphedwa pamalo pomwe amaphera nsembe yopsereza ndipo awaze magazi ake mbali zonse za guwa.
3 Všecken pak tuk její obětovati bude z ní, ocas i tuk střeva přikrývající.
Tsono apereke mafuta ake onse: mchira wamafuta ndi mafuta amene amakuta matumbo.
4 Též obě dvě ledvinky s tukem, kterýž jest na nich i na slabinách; a branici, kteráž jest na jatrách, s ledvinkami odejme.
Aperekenso impsyo ziwiri, mafuta ake pamodzi ndi mafuta onse amene ali chamʼchiwuno, ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi.
5 I bude páliti to kněz na oltáři v obět ohnivou Hospodinu; obět za provinění jest.
Wansembe azitenthe pa guwa kuti zikhale nsembe yotentha pa moto, yoperekedwa kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo lopalamula.
6 Všeliký pohlaví mužského mezi kněžími jísti bude ji, na místě svatém jedena bude; svatá svatých jest.
Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kudyako nsembeyo koma adyere ku malo opatulika. Imeneyi ndi nsembe yopatulika kwambiri.
7 Jakož obět za hřích, tak obět za vinu, jednostejné právo míti budou; knězi, kterýž by ho očišťoval, přináležeti bude.
“‘Nsembe yopepesera tchimo lopalamula ndi yofanana ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo. Ndipo nsembe ziwiri zonsezi zili ndi lamulo limodzi lokha. Wansembe amene wachita mwambo wa nsembe yopepesera machimo a kupalamula atenge nyamayo ngati yake.
8 Knězi pak, kterýž by něčí obět zápalnou obětoval, kůže té oběti zápalné, kterouž obětoval, přináležeti bude.
Wansembe wopereka nsembe yopsereza ya munthu wina aliyense, atenge chikopa cha nsembe yopserezayo kuti chikhale chake.
9 Nadto všeliká obět suchá, kteráž v peci pečena bude, a všecko, což na pánvici aneb v kotlíku strojeno bude, knězi, kterýž to obětuje, přináležeti bude.
Chopereka chilichonse cha chakudya chophika mu uvuni kapena chokazinga mu mʼphika kapena mu chiwaya ndi cha wansembe amene wapereka nsembezo.
10 Tolikéž všeliká obět suchá olejem zadělaná aneb upražená, všechněm synům Aronovým přináležeti bude, a to jednomu jako druhému.
Ndipo chopereka china chilichonse cha chakudya chosakaniza ndi mafuta kapena chowuma, chikhale cha ana onse a Aaroni ndipo anawo achigawane mofanana.
11 Tento pak bude řád oběti pokojné, kterouž by obětoval Hospodinu:
“‘Malamulo a nsembe ya chiyanjano imene munthu angathe kupereka kwa Yehova ndi awa:
12 Jestliže by ji obětoval v oběti chvály, tedy obětovati bude v obět chvály koláče nekvašené, olejem zadělané a oplatky nekvašené, olejem pomazané a mouku bělnou smaženou, s těmi koláči olejem zadělanými.
“‘Ngati munthuyo apereka chifukwa cha kuthokoza, apereke nsembeyo pamodzi ndi makeke wopanda yisiti, osakaniza ndi mafuta; timitanda ta buledi wopanda yisiti, topyapyala, topaka mafuta, ndiponso makeke a ufa wosalala wophikidwa bwino, wosakaniza ndi mafuta.
13 Mimo ty koláče také chléb kvašený obětovati bude obět svou, v obět chvály pokojných obětí svých.
Pamodzi ndi nsembe yachiyanjano yothokozerayo abwerenso ndi makeke opangidwa ndi yisiti ngati chopereka chake.
14 A budeť obětovati z něho jeden pecník, ze vší té oběti Hospodinu obět ku pozdvižení, a ten přináležeti bude tomu knězi, kterýž kropil krví té oběti pokojné.
Munthuyo atenge mtanda umodzi pa mtanda wa buledi wa mtundu uliwonse kuti ukhale nsembe yopereka kwa Yehova. Tsono mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe yachiyanjano.
15 Maso pak obět, z té oběti chvály, jenž jest obět pokojná, v den obětování jejího jedeno bude, aniž co zůstane z něho do jitra.
Nyama ya nsembe yachiyanjano yothokozera idyedwe pa tsiku lomwe nsembeyo yaperekedwa ndipo isatsaleko mpaka mmawa.
16 Jestliže by pak z slibu aneb z dobré vůle obětoval obět svou, tolikéž v den obětování jejího jedena bude; a jestliže by co zůstalo z toho, tedy na druhý den jísti se bude.
“‘Koma ngati nsembe yakeyo apereka chifukwa cha lumbiro kapena mwaufulu, nsembeyo adye tsiku lomwe yaperekedwalo. Koma yotsala angathe kuyidya mmawa mwake.
17 Jestliže by pak co masa z té oběti zůstalo do třetího dne, ohněm spáleno bude.
Ngati nyama ina ya nsembe yatsalabe mpaka tsiku lachitatu, imeneyo itenthedwe pa moto.
18 Pakli by kdo předce jedl maso oběti pokojné dne třetího, nebudeť příjemný ten, kterýž ji obětoval, aniž přijata bude, ale ohavnost bude, a kdož by koli jedl je, ponese nepravost svou.
Ngati munthu adya nyama yachiyanjano pa tsiku lachitatu, nsembeyo sidzalandiridwa. Amene wayipereka nsembeyo Mulungu sadzamulandira ndipo nsembeyo idzakhala yonyansa pamaso pa Mulungu, yosamupindulira kanthu woperekayo.
19 Též maso, kteréž by se dotklo něčeho nečistého, nebude jedeno, ale ohněm spáleno bude; maso pak jiné, kdož by koli čistý byl, bude moci jísti.
“‘Nyama imene yakhudza chilichonse chodetsedwa, munthu asayidye, koma itenthedwe pa moto. Aliyense amene ali woyeretsedwa angathe kudya nyama inayo.
20 Nebo člověk, kterýž by jedl maso z oběti pokojné, kteráž jest Hospodinu obětována, a byl by poškvrněný: tedy vyhlazen bude člověk ten z lidu svého.
Koma ngati munthu wina amene ndi wosayeretsedwa adya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.
21 A kdož by se dotkl něčeho nečistého, buďto nečistoty člověka, buď hovada nečistého aneb všeliké ohavnosti nečisté, a jedl by maso z oběti pokojné, kteráž jest Hospodinu posvěcena: tedy vyhlazen bude člověk ten z lidu svého.
Ndipo ngati munthu wina akhudza chinthu chodetsedwa, kaya chonyansa cha munthu kapena cha nyama, kapenanso chonyansa china chilichonse, ndipo kenaka nʼkudya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati anthu a mtundu wake.’”
22 Mluvil také Hospodin k Mojžíšovi, řka:
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
23 Mluv k synům Izraelským a rci jim: Žádného tuku z vola, aneb z ovce, aneb z kozy nebudete jísti.
“Awuze Aisraeli kuti, ‘Musadye mafuta a ngʼombe, nkhosa kapenanso mbuzi.
24 Ačkoli tuk mrtvého a tuk udáveného hovada může užíván býti k všeliké potřebě, ale jísti ho nikoli nebudete.
Mafuta a nyama yofa yokha, kapena mafuta a nyama yophedwa ndi zirombo akhoza kuwagwiritsa ntchito iliyonse, koma inu musadye mafuta amenewo.
25 Nebo kdož by koli jedl tuk z hovada, kteréž obětovati bude člověk v obět ohnivou Hospodinu, vyhlazen bude člověk ten, kterýž jedl, z lidu svého.
Pakuti munthu wakudya mafuta a nyama yoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe yotentha pa moto, ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
26 Tolikéž krve žádné jísti nebudete ve všech příbytcích svých, buď z ptactva, buď z hovada.
Ndipo kulikonse kumene mukakhale musakadye magazi a mbalame iliyonse kapena magazi a nyama iliyonse.
27 Všeliký člověk, kterýž by jedl jakou krev, vyhlazen bude z lidu svého.
Ngati munthu aliyense adya magazi achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.’”
28 Mluvil opět Hospodin k Mojžíšovi, řka:
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
29 Mluv k synům Izraelským a rci: Kdož by obětoval obět svou pokojnou Hospodinu, on sám přinese obět svou Hospodinu z obětí pokojných svých.
“Awuze Aisraeli kuti, Aliyense amene apereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, abwere ndi gawo la nsembeyo kwa Yehova.
30 Ruce jeho obětovati budou obět ohnivou Hospodinu. Tuk s hrudím přinese, a hrudí aby bylo v obět sem i tam obracení před Hospodinem.
Atenge ndi manja ake zigawo za chopereka zoyenera kuzitentha pa moto ngati chopereka kwa Yehova. Abweretse mafuta, pamodzi ndi chidale chomwe, ndipo chidalecho achiweyule kuti chikhale chopereka choweyula kwa Yehova.
31 Páliti pak bude kněz tuk na oltáři, ale hrudí to zůstane Aronovi i synům jeho.
Wansembe atenthe mafutawo pa guwa koma chidalecho chikhale cha Aaroni ndi ana ake.
32 A plece pravé dáte knězi ku pozdvižení z obětí pokojných vašich.
Mumupatse wansembe ntchafu ya kumanja ya nsembe yanu yachiyanjano kuti ikhale chopereka chanu kwa iye.
33 Kdožkoli z synů Aronových obětovati bude krev obětí pokojných a tuk, tomu se dostane plece pravé na díl jeho.
Mwana wa Aaroni amene amapereka magazi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano, adzitenga ntchafu ya kumanja kukhala gawo lake.
34 Nebo hrudí sem i tam obracení a plece vzhůru pozdvižení vzal jsem od synů Izraelských z obětí pokojných jejich, a dal jsem je Aronovi knězi i synům jeho právem věčným od synů Izraelských.
Choncho pa zopereka zachiyanjano za Aisraeli, Ine ndatengapo chidale chomwe amaweyula ndi ntchafu zimene amapereka nsembe ndipo ndazipereka kwa wansembe Aaroni ndi ana ake. Izi ndizo gawo lawo nthawi zonse pa zopereka za Aisraeli.”
35 Toť jest díl pomazání Aronova, a pomazání synů jeho z ohnivých obětí Hospodinových, ode dne toho, v kterémž jim přistoupiti rozkázal k vykonávání kněžství Hospodinu,
Zimenezi ndi chigawo cha Aaroni ndi ana ake chotapidwa pa zopereka kwa Yehova zoti zitenthedwe pa moto zimene zinaperekedwa pa tsiku limene anapatulidwa kuti akhale ansembe otumikira Yehova.
36 Kterýž přikázal Hospodin, aby jim ode dne, v kterémž jich pomazal, dáván byl od synů Izraelských právem věčným po rodech jejich.
Yehova ndiye analamulira kuti pa zopereka za Aisraeli azitapapo zimenezi ndi kuwapatsa ansembe ngati gawo lawo. Yehovayo analamula zimenezi pa tsiku limene ansembewo anapatulidwa ndipo anachikhazikitsa ngati lamulo la nthawi zonse.
37 Tenť jest řád oběti zápalné, oběti suché, oběti za hřích, oběti za vinu, a posvěcování i obětí pokojných,
Awa ndi malamulo a nsembe izi: nsembe yopsereza, nsembe yachakudya, nsembe yopepesera machimo, nsembe yopepesera kupalamula, nsembe ya mwambo wodzoza ndi nsembe yachiyanjano.
38 Kteréž přikázal Hospodin Mojžíšovi na hoře Sinai toho dne, když přikázal synům Izraelským, aby obětovali oběti své Hospodinu na poušti Sinai.
Malamulo amenewa Yehova anapereka kwa Mose pa Phiri la Sinai pa tsiku limene Yehova analamulira Aisraeli kuti abwere ndi zopereka za kwa Yehova, ku chipululu cha Sinai kuja.

< 3 Mojžišova 7 >