< 3 Mojžišova 4 >

1 Mluvil také Hospodin k Mojžíšovi, řka:
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
2 Mluv synům Izraelským a rci: Když by kdo zhřešil z poblouzení proti některému ze všech přikázaní Hospodinových, čině, čehož býti nemá, a přestoupil by jedno z nich;
“Awuze Aisraeli kuti, ‘Munthu akachimwa mosadziwa ndi kuchita chilichonse chimene Yehova walamula kuti asachite, azichita izi:
3 Jestliže by kněz pomazaný zhřešil hříchem jiných lidí: tedy obětovati bude za hřích svůj, kterýmž zhřešil, volka mladého bez poškvrny Hospodinu v obět za hřích.
“‘Ngati wansembe wodzozedwa achimwa, ndi kuchimwitsa anthu onse, iyeyu ayenera kupereka mwana wangʼombe wamphongo wopanda chilema chifukwa cha tchimo limene wachitalo. Imeneyi ndi nsembe ya Yehova yopepesera tchimo lake.
4 I přivede volka toho ke dveřím stánku úmluvy před oblíčej Hospodinův, a položí ruku svou na hlavu volka toho, a zabije ho před oblíčejem Hospodinovým.
Wansembeyo abwere nayo ngʼombeyo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova. Asanjike dzanja lake pamutu pa ngʼombeyo ndipo ayiphe pamaso pa Yehova.
5 Tedy vezme kněz pomazaný krve z toho volka, a vnese ji do stánku úmluvy.
Kenaka wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano.
6 Potom omočí kněz prst svůj v té krvi, a kropiti jí bude sedmkráte před Hospodinem, před oponou svatyně.
Iye aviyike chala chake mʼmagazi, ndipo awawaze kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova, patsogolo pa katani yotchinga malo wopatulika.
7 Pomaže také kněz tou krví rohů oltáře, na němž se kadí vonnými věcmi před Hospodinem, kterýž jest v stánku úmluvy, a ostatek krve volka toho vyleje k spodku oltáře zápalu, kterýž jest u dveří stánku úmluvy.
Kenaka wansembe apake magaziwo pa nyanga za guwa lofukizira lubani limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza, limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
8 Všecken pak tuk volka toho za hřích vyjme z něho, totiž tuk přikrývající střeva a všecken tuk, kterýž jest na nich,
Pambuyo pake achotse mafuta onse a ngʼombe yayimuna yopepesera machimoyo: mafuta okuta zamʼkati kapena mafuta onse amʼkatimo.
9 Též obě dvě ledvinky s tukem, kterýž jest na nich i na slabinách, tolikéž i branici, kteráž jest na jatrách, s ledvinkami odejme ji,
Achotsenso ndi kubwera ndi impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta onse ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi ndi impsyo
10 Tak jako se odjímá od volka oběti pokojné, a páliti to bude kněz na oltáři zápalu.
monga momwe amachotsera mafuta a ngʼombe yoperekedwa kuti ikhale chopereka chachiyanjano. Tsono wansembe atenthe zimenezi pa guwa lansembe zopsereza.
11 Kůži pak volka toho, i všecko maso jeho s hlavou i s nohami jeho, střeva jeho i s lejny jeho,
Koma chikopa cha ngʼombe yayimunayo ndi mnofu wake wonse, pamodzi ndi mutu ndi miyendo, zamʼkati ndi matumbo,
12 A tak celého volka vynese ven za stany na místo čisté, tam kdež se popel vysýpá, a spálí jej na dříví ohněm; na místě, kdež se popel vysýpá, spálen bude.
kapena kuti ngʼombe yonse yotsalayo apite nayo kunja kwa msasa ku malo woyeretsedwa, kumene amatayako phulusa ndi kuyitentha pa nkhuni, pa phulusapo.
13 Jestliže by pak všecko množství Izraelské pobloudilo, a byla by ta věc skrytá před očima shromáždění toho, a učinili by proti některému ze všech přikázaní Hospodinových, čehož by býti nemělo, tak že by vinni byli,
“‘Ngati gulu lonse la Aisraeli lichimwa mosadziwa, nachita chomwe ndi choletsedwa ndi Yehova, ngakhale kuti gulu lonselo silikudziwa kuti lachimwa, anthuwo ndi olakwa ndithu.
14 A byl by poznán hřích, kterýmž zhřešili: tedy obětovati bude shromáždění volka mladého v obět za hřích, a přivedou ho před stánek úmluvy.
Akazindikira tchimo limene achita, gulu lonse lipereke mwana wangʼombe wamphongo kuti akhale chopereka chopepesera tchimo ndipo abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
15 I položí starší shromáždění toho ruce své na hlavu volka před Hospodinem, a zabije volka před Hospodinem.
Akuluakulu a anthuwo asanjike manja awo pa mutu pa ngʼombe pamaso pa Yehova, ndipo ayiphe pomwepo pamaso pa Yehova.
16 I vnese kněz pomazaný z krve volka toho do stánku úmluvy,
Tsono wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano.
17 A omoče kněz prst svůj v té krvi, kropiti jí bude sedmkráte před Hospodinem, před oponou.
Aviyike chala chake mʼmagaziwo ndi kuwawaza pamaso pa Yehova kasanu ndi kawiri patsogolo pa nsalu yotchinga.
18 Pomaže také kněz tou krví rohů oltáře, kterýž jest před Hospodinem v stánku úmluvy; potom všecku krev pozůstávající vyleje k spodku oltáře zápalu, kterýž jest u dveří stánku úmluvy.
Pambuyo pake iye apake magaziwo pa nyanga za guwa limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
19 Všecken také tuk jeho vyjme z něho, a páliti bude na oltáři.
Kenaka achotse mafuta onse a ngʼombeyo ndi kuwatentha pa guwa,
20 S tím pak volkem tak učiní, jako učinil s volkem za hřích obětovaným, rovně tak učiní s ním. A tak očistí je kněz, i bude jim odpuštěno.
ndipo achite ndi ngʼombe yayimunayi monga anachitira ndi ngʼombe yayimuna yopepesera machimo. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera anthu, ndipo machimo awo adzakhululukidwa.
21 Volka pak vynese ven z táboru a spálí jej, jako spálil volka prvního; nebo obět za hřích shromáždění jest.
Kenaka atulutse ngʼombeyo kunja kwa msasa ndi kuyitentha monga anatenthera ngʼombe yoyamba ija. Imeneyi ndiyo nsembe yopepesera machimo a gulu lonse.
22 Jestliže pak kníže zhřeší, a učiní proti některému ze všech přikázaní Hospodina Boha svého, čehož býti nemělo, a to z poblouzení, tak že vinen bude,
“‘Ngati mtsogoleri achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova Mulungu wake, ndiye kuti wapalamula.
23 A byl by znám hřích jeho, jímž zhřešil: tedy přivede obět svou z koz, samce bez poškvrny.
Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, iye abwere ndi mbuzi yayimuna yopanda chilema kuti ikhale chopereka chake.
24 I položí ruku svou na hlavu toho kozla a zabije ho na místě, kdež se bijí oběti zápalné před Hospodinem; obět za hřích jest.
Asanjike dzanja lake pa mutu wa mbuziyo ndi kuyiphera pamalo pamene amaphera zopereka zopsereza pamaso pa Yehova. Ichi ndi chopereka chopepesera tchimo.
25 A vezma kněz z krve oběti za hřích na prst svůj, pomaže rohů oltáře zápalu, ostatek pak krve jeho vyleje k spodku oltáře zápalu.
Pambuyo pake wansembe atengeko magazi a chopereka chopepesera tchimocho ndi chala chake, ndipo awapake pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Athire magazi otsalawo pa tsinde la guwalo.
26 Všecken také tuk jeho páliti bude na oltáři, jako i tuk obětí pokojných. A tak očistí jej kněz od hříchu jeho, a odpuštěn bude jemu.
Wansembeyo atenthe mafuta onse pa guwapo monga amatenthera chopereka chachiyanjano. Pochita zimenezi, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo, ndipo adzakhululukidwa.
27 Jestliže pak zhřeší člověk z lidu obecného z poblouzení, učině proti některému přikázaní Hospodinovu, čehož by nemělo býti, tak že vinen bude,
“‘Ngati munthu wamba achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova, ndiye kuti wapalamula.
28 A byl by znám hřích jeho, kterýmž zhřešil: tedy přivede obět svou z koz, samici bez poškvrny, za hřích svůj, jímž zhřešil.
Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, abweretse mbuzi yayikazi yopanda chilema kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo.
29 I položí ruku svou na hlavu oběti té za hřích a zabije tu obět za hřích na místě obětí zápalných.
Asanjike dzanja lake pamutu pa mbuziyo ndipo ayiphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza.
30 A vezma kněz z krve její na prst svůj, pomaže rohů oltáře zápalu, a ostatek krve její vyleje u spodku oltáře.
Ndipo wansembe atenge magazi ndi chala chake ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza ndi kuthira magazi wotsalawo pa tsinde la guwalo.
31 Všecken také tuk její odejme, jako se odjímá tuk od obětí pokojných, a páliti jej bude kněz na oltáři u vůni příjemnou Hospodinu. A tak očistí jej kněz, a bude mu odpuštěno.
Kenaka iye achotse mafuta onse monga momwe anachotsera mafuta a chopereka chachiyanjano, ndipo awatenthe pa guwa kuti akhale fungo lokomera Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo ndipo adzakhululukidwa.
32 Pakli by z ovcí přinesl obět svou za hřích, samici bez poškvrny přinese.
“‘Ngati munthu apereka mwana wankhosa ngati chopereka chopepesera tchimo lake, abwere ndi mwana wankhosa wamkazi wopanda chilema.
33 A vloží ruku svou na hlavu té oběti za hřích a zabije ji v obět za hřích na místě, kdež se bijí oběti zápalné.
Asanjike dzanja lake pa mutu wa mwana wankhosayo ndipo amuphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza.
34 Potom vezma kněz krve z oběti té za hřích na prst svůj, pomaže rohů oltáře zápalu, ostatek pak krve její vyleje k spodku oltáře.
Kenaka wansembe atengeko ndi chala chake magazi a mwana wankhosa uja ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Magazi otsalawo athire pa tsinde la guwalo.
35 Všecken také tuk její odejme, jakž se odjímá tuk beránka z obětí pokojných, a páliti jej bude kněz na oltáři v obět ohnivou Hospodinu. A tak očistí jej kněz od hříchu jeho, kterýmž zhřešil, a odpuštěn bude jemu.
Iye achotse mafuta onse, monga amachotsera mafuta a mwana wankhosa wa chopereka chachiyanjano, ndipo wansembe awatenthe pa guwa pamodzi ndi zopereka zina zopsereza za Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo limene munthuyo anachita ndipo adzakhululukidwa.

< 3 Mojžišova 4 >