< 3 Mojžišova 14 >

1 I mluvil Hospodin k Mojžíšovi, řka:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Tento bude řád při malomocném v den očišťování jeho: K knězi přiveden bude.
“Malamulo a munthu wakhate pa tsiku la kuyeretsedwa kwake ndi awa: Abwere naye kwa wansembe.
3 I vyjde kněz ven z stanů a pohledí na něj, a uzří-li, že uzdravena jest rána malomocenství malomocného:
Wansembe atuluke kunja kwa msasa ndipo amuonetsetse wodwalayo. Ngati munthu wakhateyo wachira,
4 Rozkáže kněz tomu, kterýž se očišťuje, vzíti dva vrabce živé a čisté, a dřevo cedrové, a červec dvakrát barvený, a yzop.
wansembe alamule anthu kuti amutengere wodwala woti ayeretsedweyo, mbalame zamoyo ziwiri zomwe Ayuda amaloledwa kudya, nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope.
5 I rozkáže kněz zabiti vrabce jednoho, a vycediti krev z něho do nádoby hliněné nad vodou živou.
Wansembe alamule anthuwo kuti mbalame imodzi ayiphere mu mʼphika wa dothi pamwamba pa madzi abwino.
6 A vezme vrabce živého a dřevo cedrové, též červec dvakrát barvený, a yzop, a omočí to všecko i s vrabcem živým ve krvi vrabce zabitého nad vodou živou.
Kenaka wansembe atenge mbalame yamoyo ija ndi kuyinyika pamodzi ndi nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope kaja mʼmagazi ambalame imene anayiphera pamwamba pa madzi abwino.
7 Tedy pokropí toho, kterýž se očišťuje od malomocenství, sedmkrát, a za čistého jej vyhlásí, i pustí vrabce živého na pole.
Wansembe awaze magazi kasanu ndi kawiri pa munthu woti amuyeretse khateyo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa. Kenaka wansembe awulutsire ku thengo mbalame yamoyoyo.
8 Ten pak, kterýž se očišťuje, zpéře roucho své a oholí všecky vlasy své, umyje se vodou, a čistý bude. Potom vejde do táboru, a bydliti bude vně, nevcházeje do stanu svého za sedm dní.
“Munthu amene wayeretsedwa uja achape zovala zake, amete tsitsi lake lonse, ndipo asambe mʼmadzi. Akatero adzakhala woyeretsedwa. Atatha zimenezi munthuyo apite ku msasa wake koma akhale kunja kwa msasawo kwa masiku asanu ndi awiri.
9 Dne pak sedmého sholí všecky vlasy své, hlavu i bradu svou, i obočí své, a tak všecky vlasy své sholí; zpéře také roucha svá a tělo své umyje vodou, a tak očistí se.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri amete tsitsi lake lonse: amete kumutu, ndevu zake, nsidze zake pamodzi ndi tsitsi lina lonse. Kenaka achape zovala zake ndi kusamba mʼmadzi, ndipo adzakhala woyeretsedwa.
10 Dne pak osmého vezme dva beránky bez poškvrny, a ovci jednu roční bez poškvrny, a tři desetiny efi mouky bělné k oběti suché, olejem zadělané, a oleje jednu mírku.
“Pa tsiku lachisanu ndi chitatu munthuyo atenge ana ankhosa aamuna awiri ndi mwana wankhosa wamkazi wa chaka chimodzi. Zonsezi zikhale zopanda chilema. Atengenso chopereka chachakudya cha ufa wosalala wa makilogalamu atatu wosakaniza ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita.
11 Kněz pak, kterýž očišťuje, postaví toho člověka očišťujícího se s těmi věcmi před Hospodinem u dveří stánku úmluvy.
Wansembe amene ati ayeretse munthu wodwalayo amuyimitse munthuyo ali ndi zopereka zake zonse pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
12 I vezme kněz beránka jednoho, kteréhožto obětovati bude v obět za hřích, a mírku oleje, a obraceti bude tím sem i tam v obět obracení před Hospodinem.
“Ndipo wansembe atenge mwana wankhosa wamwamuna mmodzi ndi kumupereka kuti akhale nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita. Wansembe aziweyule zonsezi pamaso pa Yehova kuti zikhale chopereka choweyula.
13 A zabije beránka toho na místě, kdež se zabijí obět za hřích a obět zápalná, totiž na místě svatém; nebo jakož obět za hřích, tak obět za vinu knězi přináleží, svatá svatých jest.
Mwana wankhosayo amuphere pa malo amene amaphera nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yopsereza, kutanthauza malo opatulika. Monga zimakhalira ndi chopereka chopepesera machimo, chopereka ichi ndi chake cha wansembe ndipo ndi chopereka choyera kopambana.
14 I vezme kněz krve z oběti za hřích, a pomaže jí kraje ucha pravého člověka toho, kterýž se očišťuje, a palce ruky jeho pravé, a palce nohy jeho pravé.
Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera kupalamula ndi kuwapaka pa msonga pa khutu lakumanja la munthu woti ayeretsedweyo. Apakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndi chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
15 Vezme také kněz z té mírky oleje, a naleje na ruku svou levou.
Wansembe atengeko mafuta pangʼono, nʼkuwathira mʼdzanja lake lamanzere,
16 A omoče prst svůj pravý v tom oleji, kterýž má na ruce své levé, pokropí z něho prstem svým sedmkrát před Hospodinem.
aviyike chala chake cha ku dzanja lamanja mʼmafuta amene ali mʼdzanja lamanzerewo, ndi kuwaza mafutawo ndi chala chakecho kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
17 Z ostatku pak oleje toho, kterýž má na ruce své, pomaže kněz kraje ucha pravého člověka toho, kterýž se očišťuje, a palce pravé ruky jeho, a palce pravé nohy jeho, na krev oběti za vinu.
Wansembe apake mafuta otsala mʼdzanja lake pa khutu lakumanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Awapakenso pa chala chake chachikulu cha ku dzanja lamanja ndiponso pa chala chake chachikulu cha ku phazi lakumanja, pamalo pamene anali atapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula paja.
18 Což pak zůstane oleje, kterýž jest v ruce kněze, pomaže tím hlavy toho, kterýž se očišťuje; a tak očistí jej kněz před Hospodinem.
Mafuta onse otsala mʼdzanja la wansembe awathire pamutu pa munthu woti ayeretsedwe uja, ndipo potero adzachita mwambo womupepesera pamaso pa Yehova.
19 Učiní také kněz obět za hřích, a očistí očišťujícího se od nečistoty jeho. A potom zabije obět zápalnou.
“Kenaka wansembe apereke nsembe yopepesera machimo kuti achite mwambo womupepesera munthu woti ayeretsedwe khate lake uja. Atatha kuchita zimenezi, wansembe aphe nyama ya nsembe yopsereza
20 I bude obětovati kněz tu obět zápalnou, i obět suchou na oltáři; a tak očistí jej, i bude čistý.
ndi kuyipereka pa guwa, pamodzi ndi nsembe yachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera munthu wodzayeretsedwayo, ndipo adzakhala woyera.
21 Jestliže pak bude chudý, tak že by s to býti nemohl, tedy vezme jednoho beránka v obět za provinění, k obracení jí sem i tam pro očištění své, a desátý díl mouky bělné olejem zadělané k oběti suché, a mírku oleje,
“Ngati munthu woti ayeretsedweyo ndi wosauka ndipo sangathe kupeza zinthu zimenezi, apereke mwana wankhosa wamwamuna monga nsembe yopepesera kupalamula ndipo ayiweyule pochita mwambo womupepesera. Aperekenso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala osakaniza ndi mafuta kuti ikhale nsembe yachakudya, pamodzi ndi mafuta wokwanira limodzi mwa magawo atatu a lita.
22 Též dvě hrdličky aneb dvé holoubátek, kteréž by mohl míti, a bude jedno v obět za hřích, a druhé v obět zápalnou.
Aperekenso njiwa ziwiri kapena mawunda awiri zomwe iye angathe kuzipeza. Imodzi ikhale nsembe yopepesera machimo, ndi inayo ikhale ya nsembe yopsereza.
23 I přinese je v osmý den očišťování svého knězi, ke dveřům stánku úmluvy před Hospodina.
“Pa tsiku lachisanu ndi chitatu zonsezo abwere nazo kwa wansembe, pa khomo pa tenti ya msonkhano, pamaso pa Yehova kuti munthuyo ayeretsedwe.
24 Tedy kněz vezma beránka oběti za vinu a mírku oleje, obraceti je bude sem i tam v obět obracení před Hospodinem.
Wansembe atenge mwana wankhosa wopereka nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta aja, ndipo aziweyule kuti zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
25 I zabije beránka oběti za provinění, a vezma krve z oběti za provinění, pomaže jí kraje ucha pravého člověka toho, kterýž se očišťuje, a palce ruky jeho pravé, a palce nohy jeho pravé.
Wansembe aphe nkhosa yopereka nsembe yopepesera kupalamula ndipo atenge magazi ake ndi kuwapaka pa msonga ya khutu lakumanja la munthu amene ayeretsedweyo. Awapakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndiponso pa chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
26 Oleje také naleje kněz na ruku svou levou.
Kenaka wansembe athire mafuta mʼdzanja lake lamanzere,
27 A omoče prst svůj pravý v oleji, kterýž bude na ruce jeho levé, pokropí jím sedmkrát před Hospodinem.
ndipo ndi chala chake cha ku dzanja lamanja awaze mafutawo kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
28 Pomaže také kněz olejem, kterýž má na ruce své, kraje ucha pravého toho, kdož se čistí, a palce pravé ruky jeho, a palce pravé nohy jeho, na místě krve z oběti za vinu.
Apakenso mafuta omwewo amene ali mʼdzanja lake lamanja pa msonga ya khutu la kudzanja lamanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Apakenso pa chala chachikulu cha phazi lakumanja, pamalo pamene anapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula.
29 Což pak zůstává oleje, kterýž jest v ruce kněze, pomaže jím hlavy toho, kterýž se očišťuje; a tak očistí jej před Hospodinem.
Mafuta onse otsala amene ali mʼdzanja la wansembe awapake pamutu pa munthu amene ayeretsedweyo kuti amuchitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.
30 Tolikéž učiní i s hrdličkou jednou aneb s holoubátkem z těch, kteréž zjednati mohl.
Ndipo munthuyo apereke njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri, molingana ndi mmene anapezeramo,
31 Z těch, kterýchž dostati mohl, obětovati bude jedno za hřích a druhé v obět zápalnou s obětí suchou; a tak očistí kněz očišťujícího se před Hospodinem.
imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza, pamodzi ndi chopereka chachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera machimo a munthu woti ayeretsedwe.
32 Ten jest zákon toho, na komž by se ukázala rána malomocenství, a kterýž by nemohl býti s ty věci k očištění svému přináležité.
“Amenewa ndi malamulo a munthu wakhate amene alibe zinthu zoti apereke pamene akuyeretsedwa.
33 I mluvil Hospodin Mojžíšovi a Aronovi, řka:
“Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
34 Když vejdete do země Kananejské, kterouž já vám za dědictví dávám, a dopustil bych ránu malomocenství na některý dům země, kterouž vládnouti budete,
Mukakalowa mʼdziko la Kanaani limene ndikukupatsani kuti likhale lanu, ndipo Ine ndikakabweretsa ndere zoyanga mʼnyumba mʼdziko limenelo,
35 Tedy přijde hospodář domu a oznámí knězi řka: Zdá mi se, jako by byla rána malomocenství na domě.
mwini wake nyumbayo adzapite kwa wansembe ndi kukamuwuza kuti, ‘Ndaona chinthu chooneka ngati ndere mʼnyumba mwanga.’
36 I rozkáže kněz vyprázdniti dům, dříve než by všel do něho hleděti na tu ránu, aby nebylo poškvrněno něco z těch věcí, kteréž v domě jsou. Potom pak vejde, aby pohleděl na ten dům.
Tsono wansembe alamule kuti anthu atulutse zinthu zonse mʼnyumbamo iye asanalowemo ndi kukaonetsetsa ndereyo kuti mʼnyumbamo musapezeke chinthu choti achitchule chodetsedwa. Izi zitachitika, wansembe alowe mʼnyumbamo ndi kukaonamo.
37 Tedy vida ránu tu, uzří-li, že rána jest na stěnách domu, totiž důlkové názelení aneb náčervení, a na pohledění jsou nižší než stěna jinde:
Iye aonetsetse nderezo. Tsono akapeza kuti nderezo zili mʼkhoma la nyumba, ndipo ngati zili ndi mawanga obiriwira kapena ofiirira, komanso zikuoneka kuti zalowerera mpaka mʼkati mwa khoma,
38 Vyjde kněz z domu toho ke dveřím jeho, a dá zavříti dům ten za sedm dní.
wansembe atuluke mʼnyumbamo ndi kupita pa khomo, ndipo ayitseke nyumbayo masiku asanu ndi awiri.
39 A v den sedmý navrátí se kněz, a uzří-li, ano se rozmohla rána na stěnách domu toho:
Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri wansembe abwerenso kudzayangʼana mʼnyumbamo. Ngati ndere yafalikira mʼmakoma a nyumbayo,
40 Rozkáže vyníti kamení, na němž by rána taková byla, a vyvrci je ven za město na místo nečisté.
wansembe alamule kuti anthu agumule miyala imene muli nderezo ndipo akayitaye kudzala la kunja kwa mzinda.
41 Dům pak rozkáže vystrouhati vnitř všudy vůkol; a vysypou prach ten, kterýž sstrouhali, vně za městem na místo nečisté.
Wansembe awuze anthu kuti apale makoma onse a mʼkati mwa nyumbayo, ndipo zopalidwazo akazitaye ku malo odetsedwa a kunja kwa mudzi.
42 A vezmouce jiné kamení, vyplní jím místo onoho kamení; tolikéž hliny jiné vezmouce, vymaží dům.
Tsono anthuwo atenge miyala ina ndi kuyilowetsa mʼmalo mwa miyala imene anagumula ija ndipo atenge dothi latsopano ndi kumata nyumbayo.
43 Pakliť by se navrátila rána, a vzrostla by v tom domě po vyvržení kamení a vystrouhání domu, i po vymazání jeho,
“Ngati ndere iwonekanso mʼnyumbamo atagumula kale miyala ndiponso atayipala kale ndi kuyimatanso,
44 Tedy vejda kněz, uzří-li, an se rozmohla rána v domě, malomocenství rozjídající se jest v tom domě, nečistý jest.
wansembe apite kukayionetsetsenso ndipo ngati nderezo zafalikira mʼnyumbamo, ndiye kuti ndere zimenezo ndi zoopsa. Nyumba imeneyo ndi yodetsedwa.
45 I rozboří ten dům a kamení jeho, i dříví jeho, a všecko mazání domu toho, a vynosí ven za město na místo nečisté.
Agwetse nyumbayo, ndipo miyala yake, matabwa pamodzi ndi dothi lake lonse, zonse akazitaye kudzala lodetsedwa, kunja kwa mzinda.
46 Jestliže by pak kdo všel do domu toho v ten čas, když zavřín byl, nečistý bude až do večera.
“Aliyense amene alowa mʼnyumbamo itatsekedwa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
47 A jestliže by kdo spal v tom domě, zpéře roucha svá; tolikéž jestliže by kdo jedl v tom domě, zpéře roucha svá.
Munthu amene wagona mʼnyumbamo kapena kudyeramo ayenera kuchapa zovala zake.
48 Jestliže by pak kněz vejda tam, uzřel, že se nerozmohla rána v domě po obnovení jeho, tedy za čistý vyhlásí dům ten; nebo uzdravena jest rána jeho.
“Koma ngati pambuyo pa kuyimata, wansembe abwera kudzaonetsetsa mʼnyumbamo napeza kuti ndereyo sinafalikire, iye alengeze kuti nyumbayo ndi yoyeretsedwa, chifukwa ndereyo yatha.
49 A vezma k očištění domu toho dva vrabce a dřevo cedrové, a červec dvakrát barvený a yzop,
Kuti nyumbayo iyeretsedwe, mwini wake atenge mbalame ziwiri, kanthambi kamkungudza, kansalu kofiirira ndi kachitsamba ka hisope.
50 I zabije vrabce jednoho, a vycedí krev do nádoby hliněné nad vodou živou.
Wansembe aphe mbalame imodzi pamwamba pa madzi abwino mu mʼphika wa dothi.
51 A vezme dřevo cedrové a yzop, a červec dvakrát barvený, a vrabce živého, omočí to všecko ve krvi vrabce zabitého a u vodě živé, a pokropí domu toho sedmkrát.
Kenaka atenge kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope, kansalu kofiirira pamodzi ndi mbalame yamoyo ija, zonsezi aziviyike mʼmagazi a mbalame yophedwa ija, ndiponso mʼmadzi abwino aja, ndipo awaze nyumbayo kasanu ndi kawiri
52 A tak když očistí dům ten krví vrabce a vodou živou a ptákem živým, dřevem cedrovým, yzopem a červcem dvakrát barveným:
Akatero ndiye kuti wayeretsa nyumbayo ndi magazi a mbalame, madzi abwino, mbalame yamoyo, kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope ndi kansalu kofiirira.
53 Vypustí ven vrabce živého z města na pole, a očistí dům ten, i budeť čistý.
Kenaka ayiwulutsire mbalame yamoyo ija kuthengo, kunja kwa mzinda. Pamenepo ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera nyumbayo, ndipo idzakhala yoyeretsedwa.”
54 Ten jest zákon o všeliké ráně malomocenství a poškvrny černé,
Amenewa ndiwo malamulo a nthenda ya khate, bala lonyerenyetsa,
55 A malomocenství roucha i domu,
nguwi za pa zovala, ndere za mʼnyumba,
56 I otekliny, prašiviny a poškvrny pobělavé,
khate la chithupsa, khate la mʼbuko ndi khate la banga
57 K ukázání, kdy jest kdo čistý, aneb kdy jest kdo nečistý. Tenť jest zákon malomocenství.
kuti mudziwe ngati chinthucho ndi choyeretsedwa kapena chodetsedwa. Amenewa ndiwo malamulo a nthenda zonse za khate.

< 3 Mojžišova 14 >