< 3 Mojžišova 13 >

1 Mluvil také Hospodin Mojžíšovi a Aronovi, řka:
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
2 Èlověk ješto by na kůži těla jeho byla nějaká oteklina aneb prašivina, aneb poškvrna pobělavá, a bylo by na kůži těla jeho něco podobného k ráně malomocenství: tedy přiveden bude k Aronovi knězi, aneb k některému z synů jeho kněží.
“Munthu akakhala ndi chithupsa, kapena mʼbuko, kapena chikanga pa thupi lake chimene chitha kusanduka nthenda ya khate, abwere naye munthuyo kwa Aaroni wansembe kapena kwa mmodzi mwa ana ake amene ndi ansembe.
3 I pohledí kněz na ránu, kteráž jest na kůži těla jeho. Jestliže chlupové na té ráně zbělejí, a ta rána bude-li na pohledění hlubší nežli jiná kůže těla jeho, rána malomocenství jest. Když tedy spatří ji kněz, za nečistého vyhlásí jej.
Tsono wansembe ayangʼanitsitse nthendayo pa khungupo, ndipo ngati ubweya wa pamalo pamene pali nthendapo wasanduka woyera, komanso kuti nthendayo yazama mʼkati kupitirira khungu, ndiye kuti nthendayo ndi khate. Wansembe akamuonetsetsa alengeze kuti ndi wodetsedwa.
4 Pakli by poškvrna pobělavá byla na kůži těla jeho, a rána ta nebyla by hlubší nežli jiná kůže, a chlupové její nezběleli by: tedy rozkáže zavříti kněz majícího takovou ránu za sedm dní.
Ngati chikanga cha pa khungulo chikuoneka choyera, ndipo kuya kwake sikukuonekera kuti kwapitirira khungu ndi ubweya wake pamalopo sunasanduke woyera, wansembe amuyike wodwalayo padera kwa masiku asanu ndi awiri.
5 Potom pohledí na něj kněz v den sedmý, a jestli rána ta zůstává tak před očima jeho a nerozmáhá se po kůži: tedy rozkáže ho zavříti kněz po druhé za sedm dní.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso bwino wodwalayo. Ndipo ngati waona kuti nthendayo sinasinthe ndipo sinafalikire pa khungu, amuyikenso wodwalayo padera kwa masiku ena asanu ndi awiri.
6 I pohledí na ni kněz v den sedmý po druhé, a jestliže ta rána pozčernalá bude, a nerozmohla by se po kůži: tedy za čistého vyhlásí ho kněz, nebo prašivina jest. I zpéře roucha svá a čistý bude.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembeyo amuonenso bwino munthuyo, ndipo ngati nthendayo yazima ndi kusafalikira pa khungu, wansembe amutchule munthuyo kuti ndi woyera. Umenewo unali mʼbuko chabe. Choncho munthuyo achape zovala zake ndipo adzakhala woyera.
7 Pakliť by se dále rozmohla ta prašivina po kůži jeho, již po ukázání se knězi k očištění svému, tedy ukáže se znovu knězi.
Koma ngati mʼbukowo ufalikira pakhungu atakadzionetsa kale kwa wansembe ndipo wansembeyo nʼkulengeza kuti munthuyo ndi woyeretsedwa, ndiye kuti apitenso kukadzionetsa kwa wansembeyo.
8 I pohledí na něj kněz, a jestliže se rozmohla ta prašivina po kůži jeho, za nečistého vyhlásí jej kněz, nebo malomocenství jest.
Wansembe amuonetsetsenso munthuyo, ndipo ngati mʼbukowo wafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa ndi kuti nthendayo ndi khate.
9 Rána malomocenství když bude na člověku, přiveden bude k knězi.
“Ngati munthu aliyense ali ndi nthenda ya pakhungu yoyipitsa thupi, wodwalayo abwere naye kwa wansembe.
10 I pohledí na něj kněz, a bude-li oteklina bílá na kůži, až by učinila chlupy bílé, byť pak i zdravé maso bylo na té oteklině:
Wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati ali ndi chithupsa chamaonekedwe woyera pa khungupo chimene chasandutsa ubweya wa pamalopo kukhala woyera, ndipo ngati pali zilonda pa chotupacho,
11 Malomocenství zastaralé jest na kůži těla jeho. Protož za nečistého vyhlásí jej kněz, a nedá ho zavříti, nebo zjevně nečistý jest.
limenelo ndi khate lachikhalire la pa khungu, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Asamutsekere munthu woteroyo pakuti ndi wodetsedwa kale.
12 Jestliže by se pak vylilo malomocenství po kůži, a přikrylo by malomocenství všecku kůži nemocného, od hlavy jeho až do noh jeho, všudy kdež by kněz očima viděti mohl:
“Ndipo ngati, mʼkuona kwa wansembe, khate lija lafalikira pa khungu lonse moti lamugwira thupi lonse kuyambira kumutu mpaka kumapazi,
13 I pohledí na něj kněz, a přikrylo-li by malomocenství všecko tělo jeho, tedy za čistého vyhlásí nemocného. Nebo všecka ta rána v bělost se změnila, protož čistý jest.
wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati khatero lagwira thupi lake lonse, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Popeza kuti thupi lonse lasanduka loyera, munthuyo ndi woyeretsedwa.
14 Ale kdykoli ukáže se na ní živé maso, nečistý bude.
Koma pa tsiku limene zilonda zidzaoneka pa iye, munthuyo adzakhala wodetsedwa.
15 I pohledí kněz na to živé maso a vyhlásí jej za nečistého, nebo to maso živé nečisté jest, malomocenství jest.
Wansembe aonetsetse zilondazo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zilondazo ndi zodetsedwa ndipo ili ndi khate.
16 Když by pak odešlo zase maso živé a změnilo by se v bělost, tedy přijde k knězi.
Koma zilondazo zikasinthika ndi kusanduka zoyera, munthuyo ayenera kupita kwa wansembe.
17 A vida kněz, že obrátila se rána ta v bělost, za čistou vyhlásí ji; čistá jest.
Wansembe amuonetsetse ndipo ngati zilondazo zasanduka zoyera, wansembe amutchule wodwalayo kuti ndi woyera ndipo adzakhala woyera ndithu.
18 Když by pak byl na kůži těla vřed, a byl by zhojen,
“Ngati pa khungu la munthu wodwalayo pali chithupsa chimene chinapola kale,
19 Byla-li by na místě vředu toho oteklina bílá, aneb poškvrna pobělavá a náryšavá, tedy ukázána bude knězi.
ndipo pamalo pamene panali chithupsacho pakatuluka chotupa choyera kapena banga loyera mofiirira, munthuyo ayenera kukadzionetsa kwa wansembe.
20 A vida kněz, že na pohledění to místo jest nižší nežli jiná kůže, a chlupové na něm by zběleli, za nečistého vyhlásí jej kněz. Rána malomocenství jest, kteráž na vředu vyrostla.
Wansembe aonetsetse bwino ndipo ngati chikuoneka kuti chazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka woyera, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Imeneyo ndi nthenda ya khate imene yatuluka mʼchithupsacho.
21 Pakli, když pohledí na ni kněz, uzří, že chlupové nezběleli na něm, a není nižší nežli jiná kůže, ale že jest pozčernalé místo, tedy zavře ho kněz za sedm dní.
Koma ngati wansembe waonetsetsa napeza kuti palibe ubweya woyera ndipo chithupsacho sichinazame, koma chazimirira, wansembeyo amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
22 Pakliť by šíře se rozmáhala po kůži, za nečistého vyhlásí jej kněz; rána malomocenství jest.
Ngati nthendayo ikufalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limeneli ndi khate.
23 Pakli by ta poškvrna pobělavá zůstávala na místě svém, a nerozmáhala by se, znamení toho vředu jest; protož za čistého vyhlásí jej kněz.
Koma bangalo likakhala malo amodzi, wosafalikira, chimenecho ndi chipsera cha chithupsacho, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera.
24 Tělo, na jehož kůži byla by spálenina od ohně, a po zhojení té spáleniny zůstala by poškvrna pobělavá a náryšavá, anebo bílá toliko:
“Munthu akakhala ndi bala lamoto pa khungu lake, ndipo chilonda cha balalo chikasanduka banga loyera mofiirira kapena loyera,
25 Pohledí na ni kněz, a jestliže chlupové na ní zběleli, a lsknou se, způsob také její jest hlubší nežli jiné kůže vůkol: malomocenství jest, kteréž zrostlo na spálenině; protož za nečistého vyhlásí jej kněz, nebo rána malomocenství jest.
wansembe aonetsetse bangalo, ndipo ngati ubweya wa pa bangapo usanduka woyera, ndipo balalo lioneka kuti ndi lozama, limenelo ndi khate lomwe latuluka pa balalo. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate la pa khungu.
26 Pakli uzří kněz, an na poškvrně pobělavé není žádného chlupu bílého, a že nižší není nežli jiná kůže, ale že jest pozčernalá, poručí ho zavříti kněz za sedm dní.
Koma ngati wansembe waonetsetsa balalo ndipo palibe ubweya woyera, ndipo ngati balalo silinazame ndi kuti lazirala, wansembe amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
27 I pohledí na ni kněz dne sedmého. Jestliže se více rozmohla po kůži, tedy za nečistého vyhlásí jej; nebo rána malomocenství jest.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso wodwalayo, ndipo ngati bangalo lafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate.
28 Pakli bělost lsknutá na svém místě zůstávati bude, a nerozmůže se po kůži, ale bude pozčernalá: zprýštění od spáleniny jest; za čistého vyhlásí jej kněz, nebo šrám spáleniny jest.
Koma ngati bangalo likhala pa malo amodzi wosafalikira pa khungu, ndipo lazimirira, limenelo ndi thuza la bala lamoto, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Chimenecho ndi chipsera chamoto.
29 Byla-li by pak rána na hlavě aneb na bradě muže neb ženy,
“Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi nthenda kumutu kapena ku chibwano,
30 Tedy pohledí kněz na tu ránu, a jestliže způsob její bude hlubší nežli jiná kůže, a bude na ní vlas prožlutlý a tenký: tedy za nečistého vyhlásí jej kněz, nebo poškvrna černá jest; malomocenství na hlavě aneb na bradě jest.
wansembe aonetsetse balalo ndipo likaoneka kuti lazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka wachikasu ndi wonyololoka, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zimenezo ndi mfundu zonyerenyetsa, khate lakumutu kapena ku chibwano.
31 Když pak pohledí kněz na ránu poškvrny černé a uzří, že způsob její není hlubší nežli jiná kůže, a že není vlasu černého na ní: zavříti dá kněz majícího ránu poškvrny černé za sedm dní.
Koma wansembe akaonetsetsa mfundu zonyerenyetsazo, ndipo zikaoneka kuti sizinazame ndi kuti palibe ubweya wakuda, wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku asanu ndi awiri.
32 I pohledí kněz na tu ránu dne sedmého, a aj, nerozmohla se ta poškvrna černá, a není vlasu žlutého na ní, a způsob té poškvrny černé není hlubší nežli kůže:
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo, ndipo ngati sizinafalikire ndipo palibe ubweya wachikasu pamalopo ndiponso sizinazame,
33 Tedy oholen bude člověk ten, ale poškvrny té černé nedá holiti. I dá zavříti kněz majícího tu poškvrnu za sedm dní po druhé.
wodwalayo ametedwe, koma pamene pali mfunduyo pasametedwe. Wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
34 I pohledí kněz na poškvrnu černou dne sedmého, a jestliže se nerozmohla poškvrna černá dále po kůži, a místo její není-li hlubší nežli jiná kůže: za čistého vyhlásí ho kněz, i zpéře roucha svá a čistý bude.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo ndipo ngati sizinafalikire pa khungu ndi kuti sizinazame, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Tsono achape zovala zake, ndipo adzakhala woyera.
35 Pakli by se dále rozmohla poškvrna ta černá po kůži, již po očištění jeho,
Koma mfundu zonyerenyetsazo zikafalikira pa khungu, wansembe atalengeza kuti ndi woyera,
36 Tedy pohledí na ni kněz, a uzří-li, že se dále rozmohla ta poškvrna černá po kůži, nebude více šetřiti vlasu žlutého; nečistý jest.
wansembe amuonetsetsenso wodwalayo ndipo ngati mfunduzo zafalikira pa khungu, iye asalabadirenso zoyangʼana ngati ubweya uli wachikasu. Munthuyo ndi wodetsedwa.
37 Pakli poškvrna černá tak zůstává před očima jeho, a černý vlas vzrostl by na ní, tedy zhojena jest ta poškvrna černá; čistý jest, a za čistého vyhlásí jej kněz.
Koma ngati wansembe waonetsetsa kuti mfunduzo sizinasinthe ndipo ubweya wakuda wamera pa mfundupo, ndiye kuti wodwalayo wachira. Tsono wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa.
38 Když by na kůži těla muže aneb ženy byly poškvrny, totiž poškvrny pobělavé,
“Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi mawanga woyera pa khungu,
39 I pohledí kněz, a jestliže budou na kůži těla jejich poškvrny bílé, pozčernalé, tedy poškvrna bílá jest, kteráž na kůži zrostla; čistý jest.
wansembe aonetsetse mawangawo, ndipo ngati ali otuwa, ndiye kuti ndi mibuko chabe yotuluka pa khungu. Munthuyo ndi woyera.
40 Muž, z jehož by hlavy vlasové slezli, lysý jest a čistý jest.
“Tsitsi la munthu likayoyoka kumutu ndiye kuti ndi dazi limenelo koma munthuyo ndi woyeretsedwa.
41 Jestliže pak po jedné straně obleze hlava jeho, nálysý jest a čistý jest.
Ngati tsitsi lake layoyoka chapamphumi ndiye kuti ndi dazi la pa chipumi limenelo koma munthuyo ndi woyera.
42 Pakli na té lysině, aneb na tom oblysení byla by rána bílá a ryšavá, tedy malomocenství zrostlo na lysině jeho, aneb na oblysení jeho.
Koma ngati pa dazi la pamutu kapena la pa chipumi pakhala chithupsa choyera mofiirira, ndiye kuti ndi khate limenelo lochokera mu dazi la pamutu lija kapena pa chipumi lija.
43 I pohledí na něj kněz, a uzří-li oteklinu rány bílou a ryšavou na lysině jeho, aneb na oblysení jeho, jako způsob malomocenství na kůži těla:
Tsono wansembe amuonetsetse wodwalayo ndipo ngati chithupsa cha pa dazi lapankhongo kapena pa dazi lapachipumicho ndi choyera mofiirira monga nthenda ya khate imaonekera,
44 Èlověk malomocný jest a nečistý jest. Bez meškání za nečistého vyhlásí jej kněz, nebo na hlavě jeho jest malomocenství jeho.
ndiye kuti munthuyo ali ndi khate, motero ndi wodetsedwa. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa chifukwa cha chithupsa cha pamutu pakepo.
45 Malomocný pak, na němž by ta rána byla, bude míti roucho roztržené a hlavu odkrytou a ústa zastřená, a Nečistý, nečistý jsem! volati bude.
“Munthu wa khate lotere avale sanza, tsitsi lake alilekerere, aphimbe mlomo wake wapamwamba ndipo azifuwula kuti, ‘Ndine wodetsedwa, ndine wodetsedwa!’
46 Po všecky dny, v nichž ta rána bude na něm, za nečistého jmín bude; nebo nečistý jest. Sám bydliti bude, vně za stany bude přebývání jeho.
Munthu wodwalayo adzakhala wodetsedwa kwa nthawi yonse imene ali ndi nthendayo. Iye ayenera kumakhala payekha kunja kwa msasa.
47 Když by pak na rouchu byla rána malomocenství, buď na rouchu soukenném aneb na rouchu lněném,
“Nsalu iliyonse ikakhala ndi nguwi,
48 Buď na osnově aneb na outku ze lnu aneb z vlny, buď na kůži aneb na každé věci kožené,
kaya ndi chovala chopangidwa ndi nsalu yathonje kapena yaubweya, yoluka ndi thonje kapena ubweya, yachikopa kapena yopangidwa ndi chikopa,
49 A byla by ta rána zelená neb náryšavá na rouchu aneb na kůži, aneb na osnově, aneb na outku, aneb na kterékoli nádobě kožené: rána malomocenství jest, ukázána bude knězi.
ndipo ngati pamalo pamene pachita nguwiyo pali ndi maonekedwe obiriwira kapena ofiirira imeneyo ndi nguwi yoyipitsa chovala ndipo chovalacho chikaonetsedwe kwa wansembe.
50 I pohledí kněz na tu ránu, a dá zavříti tu věc mající ránu za sedm dní.
Wansembeyo ayionetsetse nguwiyo ndipo chovalacho achiyike padera kwa masiku asanu ndi awiri.
51 A pohledě na tu ránu dne sedmého, uzří-li, že se dále rozmohla ta rána na rouchu, neb po osnově anebo po outku, aneb na kůži, k čemuž by jí koli užíváno bylo: rána ta malomocenství rozjídavá jest, věc nečistá jest.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri ayionetsetsenso nguwiyo ndipo ngati nguwiyo yafalikira pa chovalacho, chathonje kapena chaubweya, kapena pa chikopacho, kaya ndi cha ntchito ya mtundu wanji, imeneyo ndi nguwi yoopsa ndipo chovalacho ndi chodetsedwa.
52 I spálí to roucho aneb osnovu, aneb outek z vlny neb ze lnu, aneb jakoukoli nádobu koženou, na níž by byla rána ta; nebo malomocenství škodlivé jest, protož ohněm spáleno bude.
Wansembe atenthe chovala chathonje kapena chaubweya chija, ngakhalenso chinthu chachikopa chija popeza nguwiyo yachidetsa. Nguwiyo ndi yoopsa choncho chinthucho achitenthe.
53 Pakli pohledě kněz, uzřel by, že se nerozmohla rána ta na rouchu, aneb na osnově, aneb na outku, aneb na kterékoli nádobě kožené:
“Koma ngati wansembe akayangʼanitsitsa nguwiyo apeza kuti sinafalikire pa chovalacho kapena pa chinthu chilichonse chachikopa,
54 Rozkáže kněz, aby zeprali tu věc, na níž byla by rána, i káže ji zavříti za sedm dní po druhé.
iye alamulire kuti chinthu choyipitsidwacho achichape. Akatero achiyike padera kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
55 I pohledí kněz po zeprání té věci na ránu. Jestliže nezměnila rána barvy své, byť se pak nerozmohla dále, předce nečistá jest. Ohněm spálíš ji; nebo rozjídavá věc jest na vrchní neb spodní straně její.
Chovalacho chitachapidwa, wansembe achionenso ndipo ngati nguwiyo sinasinthe maonekedwe ake, ngakhale kuti sinafalikire, chovalacho ndi chodetsedwa ndithu. Muchitenthe, ngakhale kuti nguwiyo ili kumbuyo kapena kumaso kwa chinthucho.
56 Pakli pohledě kněz, uzřel by, an pozčernala rána po zeprání svém, odtrhne ji od roucha aneb od kůže, aneb od osnovy, aneb od outku.
Koma ngati wansembe aonetsetsa nʼkupeza kuti nguwi ija yathimbirira pa chovala chija kapena pa chinthu chachikopa chija atachichapa, ndiye angʼambeko chinthucho pa banga la nguwiyo.
57 Jestliže se pak ukáže ještě na rouchu aneb na osnově, aneb na outku, aneb na kterékoli nádobě kožené, malomocenství rozjídající se jest. Ohněm spálíš věc tu, na kteréž by ta rána byla.
Koma ngati nguwiyo iwonekanso pa chovala chathonje kapena chaubweya ndiye kuti nguwiyo ikufalikira. Chilichonse chimene chili ndi nguwi chiyenera kutenthedwa.
58 Roucho pak aneb osnovu, aneb outek, aneb kteroukoli nádobu koženou, když bys zepral, a odešla by od ní ta rána, ještě po druhé zpéřeš, a čisté bude.
Chovala chathonje kapena chaubweya, ngakhale chinthu china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, mukachichapa nguwi yake nʼkuchoka muchichapenso kawiri ndipo chidzakhala choyeretsedwa.”
59 Tenť jest zákon o ráně malomocenství na rouchu soukenném aneb lněném, aneb na osnově, aneb na outku, aneb na kterékoli nádobě kožené, kterak má za čistou aneb za nečistou uznána býti.
Amenewa ndiwo malamulo a nguwi yokhala pa chovala chaubweya kapena pa chovala chathonje, kapenanso pa chinthu chilichonse chopangidwa ndi chikopa kuti muzitha kulekanitsa choyeretsedwa ndi chodetsedwa.

< 3 Mojžišova 13 >