< 3 Mojžišova 10 >

1 Synové pak Aronovi Nádab a Abiu, vzavše jeden každý kadidlnici svou, dali do nich oheň a položili na něj kadidlo, a obětovali před Hospodinem oheň cizí, čehož jim byl nepřikázal.
Ana a Aaroni, Nadabu ndi Abihu, aliyense anatenga chofukizira lubani chake nayikamo makala a moto ndi kuthiramo lubani. Iwo anapereka pamaso pa Yehova moto wachilendo, moto umene Yehova sanawalamule.
2 Protož sstoupiv oheň od Hospodina, spálil je; a zemřeli tu před Hospodinem.
Choncho moto unatuluka pamaso pa Yehova ndi kuwapsereza, ndipo anafa pamaso pa Yehova.
3 I řekl Mojžíš Aronovi: Toť jest, což mluvil Hospodin, řka: V těch, kteříž přistupují ke mně, posvěcen budu, a před oblíčejem všeho lidu oslaven budu. I mlčel Aron.
Pamenepo Mose anawuza Aaroni kuti, “Pajatu Yehova ananena kuti, “‘Kwa iwo amene amandiyandikira ndidzaonetsa ulemerero wanga; pamaso pa anthu onse ndidzalemekezedwa.’” Aaroni anakhala chete wosayankhula.
4 Tedy povolal Mojžíš Mizaele a Elizafana, synů Uziele, strýce Aronova, a řekl jim: Poďte a vyneste bratří své od svatyně ven za stany.
Mose anayitana Misaeli ndi Elizafani, ana a Uzieli, abambo angʼono a Aaroni, ndipo anawawuza kuti, “Bwerani kuno mudzachotse abale anuwa pa malo wopatulika ndi kuwatulutsira kunja kwa msasa.”
5 I přišli a vynesli je v sukních jejich ven za stany, jakž byl rozkázal Mojžíš.
Choncho anabwera atavala minjiro yawo ndipo anawatenga ndi kuwatulutsa kunja kwa msasawo monga momwe Mose analamulira.
6 Mluvil pak Mojžíš Aronovi, Eleazarovi a Itamarovi, synům jeho: Hlav svých neodkrývejte a roucha svého neroztrhujte, abyste nezemřeli, a aby se Bůh na všecko množství nerozhněval; ale bratří vaši, všecka rodina Izraelská, budou plakati nad tím spálením, kteréž uvedl Hospodin.
Ndipo Mose anawuza Aaroni ndi ana ake Eliezara ndi Itamara kuti, “Musalileke tsitsi lanu nyankhalala ndipo musangʼambe zovala zanu kuti mungafe, ndi mkwiyo wa Yehova ungagwere anthu onsewa. Koma abale anu okha, kutanthauza fuko lonse la Israeli ndiwo ayenera kulira omwalira aja amene Yehova wawapsereza ndi moto.
7 Vy pak ze dveří stánku úmluvy nevycházejte, abyste nezemřeli; nebo olej pomazání Hospodinova jest na vás. I učinili vedlé rozkázaní Mojžíšova.
Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano, mungafe, chifukwa munadzozedwa ndi mafuta a Yehova kukhala ansembe.” Choncho iwo anachita monga Mose ananenera.
8 Mluvil také Hospodin Aronovi, řka:
Pambuyo pake Yehova anayankhula ndi Aaroni nati,
9 Vína a nápoje opojného nebudeš píti, ty ani synové tvoji s tebou, kdyžkoli budete míti vcházeti do stánku úmluvy, abyste nezemřeli, (ustanovení věčné to bude po rodech vašich);
“Iwe ndi ana ako musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa pamene mukulowa mu tenti ya msonkhano kuti mungafe. Ili ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse.
10 Také abyste rozeznati mohli mezi svatým a neposvěceným, a mezi čistým a nečistým;
Muzisiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, pakati pa zinthu zodetsedwa ndi zinthu zoyeretsedwa,
11 Též abyste učili syny Izraelské všechněm ustanovením, kteráž mluvil Hospodin k nim skrze Mojžíše.
ndipo muyenera kuphunzitsa Aisraeli onse malamulo amene Yehova wakupatsani kudzera mwa Mose.”
12 Mluvil pak Mojžíš Aronovi, Eleazarovi a Itamarovi, synům jeho, kteříž živi zůstali: Vezměte obět suchou, kteráž zůstala z ohnivých obětí Hospodinových, a jezte ji s přesnicemi u oltáře; nebo svatá svatých jest.
Mose anawuza Aaroni ndi ana ake otsalawo, Eliezara ndi Itamara kuti, “Tengani zopereka zachakudya zopanda yisiti zimene zatsala pa nsembe zopsereza za kwa Yehova ndipo muzidye pafupi ndi guwa pakuti ndi zopatulika kwambiri.
13 Protož jísti budete ji na místě svatém, nebo to jest právo tvé a právo synů tvých z ohnivých obětí Hospodinových; tak zajisté jest mi přikázáno.
Muzidye pa malo wopatulika chifukwa zimenezi ndi gawo lako ndi la ana ako pa zopereka zopsereza kwa Yehova. Izitu ndi zimene Yehova anandilamulira.
14 Hrudí pak sem i tam obracení, a plece vznášení jísti budete na místě čistém, ty i synové tvoji, i dcery tvé s tebou; nebo to právem tobě a synům tvým dáno jest z pokojných obětí synů Izraelských.
Koma iwe pamodzi ndi ana ako aamuna ndi aakazi muzidya chidale chimene chinaweyulidwa ndi ntchafu zimene zinaperekedwa nsembe. Muzidye pamalo woyeretsedwa. Zimenezi zaperekedwa kwa iwe ndi ana ako monga gawo lanu pa zopereka zachiyanjano zimene apereka Aisraeli.
15 Plece vzhůru vznášení a hrudí sem i tam obracení s obětmi ohnivými tuků, kteréž přinesou, aby sem i tam obracíno bylo, tak jako obět obracení před Hospodinem, bude tobě i synům tvým s tebou právem věčným, jakož přikázal Hospodin.
Ntchafu imene inaperekedwayo ndi chidale chomwe chinaweyulidwacho abwere nazo pamodzi ndi nsembe ya mafuta ya Yehova yotentha pa moto, ndipo uziweyule kuti zikhale zopereka zoweyula pamaso pa Yehova. Zimenezi zizikhala zako ndi ana ako nthawi zonse monga walamulira Yehova.”
16 Mojžíš pak hledal pilně kozla k oběti za hřích, a hle, již spálen byl. Tedy rozhněval se na Eleazara a Itamara, syny Aronovy pozůstalé, a řekl:
Pambuyo pake Mose anafunafuna mbuzi ya nsembe yopepesera machimo koma anapeza kuti anayitentha kale. Apa Mose anakalipira Eliezara ndi Itamara, ana a Aaroni otsala aja nati,
17 Pročež jste nejedli oběti za hřích na místě svatém? Nebo svatá svatých byla, poněvadž ji dal vám, abyste nesli nepravost všeho množství k očištění jejich před Hospodinem.
“Chifukwa chiyani simunadyere pamalo wopatulika nsembe yopepesera machimo ija? Kodi imene ija siyopatulika? Kodi Yehova sanapereke nyamayo kwa inu kuti muchotse machimo a mpingo wonse powachitira mwambo wa nsembe yopepesera machimo pamaso pa Yehova?
18 A hle, ani krev její není vnesena do vnitřku svatyně. Jísti jste měli ji v svatyni, jakož jsem byl přikázal.
Pakuti magazi ake sanalowe nawo ku Malo Wopatulika, mukanadya nyama ya mbuziyo pa malo wopatulikawo monga Yehova analamulira.”
19 Tedy odpověděl Aron Mojžíšovi: Aj, dnes obětovali obět svou za hřích a obět svou zápalnou před Hospodinem, ale přihodila se mně taková věc, že, kdybych byl jedl obět za hřích dnes, zdali by se to líbilo Hospodinu?
Aaroni anamuyankha Mose kuti, “Lero anthu apereka nsembe yawo yopepesera machimo ndiponso nsembe yawo yopsereza pamaso pa Yehova komabe zinthu zoterezi zandichitikira. Kodi Yehova akanakondwa ndikanadya nsembe yopepesera machimo lero?”
20 Což když uslyšel Mojžíš, přestal na tom.
Pamene Mose anamva zimenezi, anakhutira.

< 3 Mojžišova 10 >