< Sudcov 21 >

1 Nadto každý z mužů Izraelských přísahou se byli zavázali v Masfa, řkouce: Žádný z nás nedá dcery své Beniaminským za manželku.
Aisraeli anali atalumbira ku Mizipa kuti, “Palibe mmodzi wa ife adzapereke mwana wake wamkazi kuti akwatiwe ndi mwamuna wa fuko la Benjamini.”
2 Protož všel lid do domu Boha silného, a seděli tam až do večera před Bohem, a pozdvihše hlasu svého, plakali pláčem velikým.
Anthu anapita ku Beteli kumene anakakhala pansi pamaso pa Mulungu mpaka madzulo. Iwo anakweza mawu nalira kwambiri.
3 A řekli: Proč Hospodine, Bože Izraelský, stalo se toto v Izraeli, aby dnes ubylo jedno pokolení z Izraele?
Iwo ankanena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli, nʼchifukwa chiyani izi zachitika mʼdziko la Israeli kuti lero fuko limodzi lisowe mu Israeli?”
4 Nazejtří pak ráno vstal lid, a vzdělali tam oltář, a obětovali oběti zápalné a pokojné.
Mmawa mwake anthu anadzuka namanga guwa lansembe ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano.
5 Řekli pak synové Izraelští: Jest-li kdo, ješto nepřišel do shromáždění tohoto ze všech pokolení Izraelských k Hospodinu? (Nebo se byli velice zapřisáhli proti tomu, kdož by nepřišel k Hospodinu do Masfa, řkouce: Bez milosti ať umře.
Kenaka Aisraeli anafunsa kuti, “Kodi ndani pakati pa mafuko a Israeli sanafike ku msonkhano wa Yehova?” Anatero chifukwa anachita malumbiro aakulu okhudza munthu amene alephere kupita ku Mizipa ndi kuti woteroyo ayenera kuphedwa.
6 Nebo litujíce synové Izraelští Beniamina bratra svého, řekli: Dnes vyhlazeno jest jedno pokolení z Izraele.
Tsono Aisraeli anamva chisoni chifukwa cha abale awo, Abenjamini. Iwo anati, “Lero fuko limodzi lachotsedwa mu Israeli.
7 Jakž tedy učiníme s těmi ostatky, aby ženy měli, poněvadž jsme se přísahou zavázali skrze Hospodina, že jim nedáme dcer svých za manželky?)
Kodi tingawapezere bwanji anthu otsalawa akazi woti awakwatire? Paja ife tinalumbira kwa Yehova kuti sitidzapereka ana anthu aakazi kuti awakwatire.
8 Řekli tedy: Jest-li kdo z pokolení Izraelských, ješto nepřišel k Hospodinu do Masfa? A aj, nepřišel byl žádný do vojska z Jábes Galád do shromáždění.
Kenaka anafunsa kuti, ‘Kodi mu fuko la Israeli ndani amene sanabwere pamaso pa Yehova ku Mizipa?’” Tsono panapezeka kuti panalibe ndi mmodzi yemwe wochokera ku Yabesi Giliyadi amene anapita ku msonkhano ku misasa kuja.
9 Nebo když sečten byl lid, a aj, nebylo tam žadného z obyvatelů Jábes Galád.
Pamene anthu anawerengana anangoona kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi palibe.
10 Protož poslalo tam shromáždění to dvanácte tisíc mužů nejsilnějších, a přikázali jim, řkouce: Jděte a pobíte obyvatele Jábes Galád ostrostí meče, ženy i děti.
Choncho msonkhano unatumiza anthu ankhondo 12,000 ndi kuwalamula kuti, “Mukaphe anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi, kuphatikizapo akazi ndi ana.”
11 Toto pak učiníte: Všecky mužského pohlaví, a každou ženu, kteráž muže poznala, zamordujete.
Izi ndi zimene mukachite. “Mukaphe mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense amene anadziwapo mwamuna.”
12 Nalezli tedy mezi obyvateli Jábes Galád čtyři sta děveček panen, kteréž nepoznaly muže, a přivedli je do vojska v Sílo, kteréž bylo v zemi Kananejské.
Iwo anapeza atsikana 400 pakati pa anthu okhala mu Yabesi Giliyadi amene anali asanadziwepo mwamuna ndipo anabwera nawo ku misasa ku Silo mʼdziko la Kanaani.
13 Tedy poslalo všecko to shromáždění, a mluvili k synům Beniamin, kteříž byli v skále Remmon, a povolali jich v pokoji.
Kenaka msonkhano wonse unatumiza uthenga kwa Abenjamini amene ankakhala ku thanthwe la Rimoni kuwawuza kuti nkhondo yatha.
14 Protož navrátili se Beniaminští toho času. I dali jim ženy, kteréž živé zachovali z žen Jábes Galád, ale ani tak se jim nedostávalo jich.
Choncho Abenjamini anabwera nthawi imeneyo ndipo Aisraeli anawapatsa akazi a ku Yabesi Giliyadi amene sanaphedwe. Koma sanapezeke owakwanira.
15 Lidu pak líto bylo Beniamina, proto že učinil Hospodin mezeru v pokoleních Izraelských.
Aisraeli anamvera chisoni Abenjamini, chifukwa Yehova anachita ngati waligwerula dzino fuko la Israeli.
16 Řekli tedy starší shromáždění toho: Jak učiníme s těmi pozůstalými, aby měli ženy? Nebo vyhlazeny jsou ženy z pokolení Beniamin.
Choncho akuluakulu a msonkhano anati, “Kodi tikawapezera kuti akazi anthu otsalirawa kuti awakwatire popeza kuti akazi a fuko la Benjamini anaphedwa?”
17 Řekli také: Dědictví Beniaminovo pozůstalým náleží, aby nezahynulo pokolení z Izraele.
Iwo anati, “Abenjamini amene anapulumukawa ayenera kukhala ndi zidzukulu, kuti mtundu wa Israeli usafafanizike.
18 My pak nemůžeme jim dáti dcer svých za manželky; (nebo se byli přísahou zavázali synové Izraelští, řkouce: Zlořečený buď, kdož by dal manželku synům Beniamin.)
Ife sitingathe kuwapatsa ana anthu aakazi kuti akwatire. Paja tinalumbira kuti, ‘Akhale wotembereredwa aliyense amene adzapereka mwana wake wamkazi kwa mwamuna wa fuko la Benjamini kuti akwatire.’
19 Potom řekli: Aj, slavnost Hospodinova bývá v Sílo každého roku na místě, kteréž jest s půlnoční strany domu Boha silného, k východu slunce cestě, kterouž se chodí od domu Boha silného do Sichem, a Lebnu jest na poledne.
Ndipo anati, ‘Paja ku Silo kuli chikondwerero cha chaka ndi chaka cholemekeza Yehova. Tsono Silo ali kumpoto kwa Beteli, kummawa kwa msewu wochokera ku Beteli kupita ku Sekemu, ndiponso kummwera kwa Lebona.’”
20 Přikázali tedy synům Beniamin, řkouce: Jděte a skrejte se v vinicích.
Choncho anawalamulira Abenjamini aja kuti, “Pitani mukabisale mʼminda ya mpesa
21 A šetřte, a aj, když vyjdou dcery Sílo plésati v houfích, tedy vyskočíte z vinic a pochytíte sobě každý manželku svou ze dcer Sílo, a odejdete do země Beniamin.
ndipo mukakhale tcheru. Ana aakazi a ku Silo akadzatulukira kudzavina nawo magule, pomwepo inu mutuluke minda ya mpesa ndi kukawagwira aliyense wake ndi kupita nawo ku dziko la Benjamini.
22 Když pak přijdou otcové jejich aneb bratří jejich, aby se před námi soudili, tedy řekneme jim: Slitujte se nad námi místo nich, nebo v té válce nevzali jsme pro každého z nich manželky; také jste vy jim nedali jich, a tak nebudete nic vinni.
Ngati abambo awo kapena alongo awo adzabwera kudzadandaula kwa ife, tidzawawuza kuti, ‘Chonde, tikomereni mtima powalola kuti atenga ana anu aakaziwo popeza kuti ife sitinawapezere akazi pomenya nkhondo. Inunso simunachite kuwapatsa. Mukanatero ndiye mukanapalamula.’”
23 Tedy učinili tak synové Beniamin, a přivedli sobě manželky vedlé počtu svého z těch plésajících, kteréž uchvátili; a odšedše, navrátili se k dědictví svému, a vzdělavše zase města svá, bydlili v nich.
Abenjamini anachitadi zimenezi. Mwa akazi amene ankavina aja anagwirapo ena, malingana ndi chiwerengero chawo, nawatenga kuti akhale akazi awo. Kenaka ananyamuka kubwerera ku dziko la kwawo, nakamanganso mizinda yawo ndi kumakhalamo.
24 A tak odešli odtud synové Izraelští toho času, jeden každý k svému pokolení a k čeledi své; a vrátili se odtud jeden každý k dědictví svému.
Pambuyo pake Aisraeli anachoka kumeneko ndi kubwerera kwawo, ku mafuko ndi ku mabanja awo, aliyense ku dera la cholowa chake.
25 Těch dnů nebylo krále v Izraeli, ale každý, což se mu vidělo, to činil.
Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense ankangochita zimene zomukomera yekha.

< Sudcov 21 >