< Józua 8 >
1 I řekl Hospodin k Jozue: Neboj se, ani se strachuj; pojmi s sebou všecken lid bojovný, a vstana, táhni k Hai. Aj, dal jsem v ruku tvou krále Hai a lid jeho, město i zemi jeho.
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Usachite mantha kapena kutaya mtima. Tenga gulu lonse la nkhondo, ndipo upite ku Ai. Taona, ndapereka mfumu ya Ai pamodzi ndi anthu ake, mzinda wake ndi dziko lake lonse mʼmanja mwako.
2 A učiníš Hai a králi jeho, jako jsi učinil Jerichu a králi jeho, loupež však a dobytky jeho rozbitujete mezi sebe. Zdělejž sobě zálohy k městu po zadu.
Mzinda wa Ai ndi mfumu yake muchite monga munachita ndi mzinda wa Yeriko ndi mfumu yake, koma katundu wa mumzindamo ndi zoweta mukazitenge ndi kuzisunga kuti zikhale zanu. Mukalalire mzinda wa Ai ndi kuwuthira nkhondo kuchokera kumbuyo.”
3 Tedy vstal Jozue a všecken lid bojovný, aby táhli k Hai. I vybral Jozue třidcet tisíců mužů velmi silných, a předeslal je v noci.
Kotero Yoswa ndi gulu lonse la nkhondo anakonzeka kupita ku Ai. Iye anasankha amuna 30,000 odziwa kumenya nkhondo bwino ndipo anawatumiza usiku
4 A přikázal jim, řka: Šetřtež vy, kteříž uděláte zálohy městu po zadní straně města, abyste nebyli příliš daleko od něho, ale buďte všickni pohotově.
nawapatsa malamulo awa kuti, “Mvetsani bwino; mukabisale kuseri kwa mzindawo. Musakapite patali ndi mzindawo, koma nonsenu mukakhale okonzekera nkhondo.
5 Já pak i všecken lid, kterýž se mnou jest, přitáhneme k městu. A když oni nám vyjdou vstříc, jako prvé, utíkati budeme před nimi.
Ine ndi gulu langa lonse tikayamba kuwuputa mzindawu, ndipo akadzangotuluka kudzalimbana nafe, ife tidzawathawa monga tinachitira poyamba.
6 Tedy honiti budou nás, až bychom poodvedli jich od města, (nebo řeknou: Utíkají před námi, jako prvé), utíkajíce před nimi.
Iwo adzatithamangitsa mpaka titawakokera kutali ndi mzindawo, pakuti iwo adzati, ‘Akutithawa monga anachitira poyamba.’ Pamene ife tizidzathawa,
7 Vy mezi tím vyskočíte z záloh, a vyženete ostatní obyvatele města, nebo dá je Hospodin Bůh váš v ruku vaši.
inu mudzatuluke pamene mwabisalapo ndi kulanda mzindawo. Yehova Mulungu wanu adzakupatsani mzindawo.
8 A když vezmete město, zapálíte je ohněm, podlé slova Hospodinova učiníte; šetřtež toho, což jsem přikázal vám.
Mukakawulanda mzindawo mudzawuyatse moto. Mukachite monga mwa mawu a Yehova. Amenewa ndiwo malamulo amene ndakupatsani.”
9 I poslal Jozue, a oni šli k zálohám, a zůstali mezi Bethel a Hai, od západní strany Hai; Jozue pak zůstal té noci u prostřed lidu.
Yoswa atawatumiza, anapita ku malo wokabisalakowo ndipo anadikirira kumeneko. Malowa anali pakati pa Beteli ndi Ai, kumadzulo kwa Ai. Koma Yoswa anagona usiku umenewu pakati pa gulu lake lankhondo.
10 Potom vstav Jozue velmi ráno, sečtl lid, i bral se napřed, on a starší Izraelští před lidem k Hai.
Mmawa mwake, Yoswa anadzuka nayitana asilikali ake. Tsono iye pamodzi ndi akuluakulu a Aisraeli anatsogola kupita ku Ai.
11 Všecken také lid bojovný, kterýž byl s ním, táhnouce, přiblížili se, až přišli naproti městu, a položili se po straně půlnoční Hai; údolí pak bylo mezi nimi a mezi Hai.
Gulu lonse la nkhondo limene linali ndi iye linatsogolako ndi kukamanga zithando pafupi ndi mzindawo chakumpoto mopenyana nawo. Pakati pa iwo ndi mzindawo panali chigwa.
12 Vzal pak byl okolo pěti tisíc mužů, kteréž postavil v zálohách mezi Bethel a Hai, od západní stany města.
Yoswa anali atatenga asilikali 5,000 ndi kuwabisa pakati pa Ai ndi Beteli, kumadzulo kwa mzindawo.
13 I přiblížil se lid, totiž všecko vojsko, kteréž bylo od půlnoční strany města, a kteříž byli v zálohách jeho od západní strany města; a tak vtáhl Jozue noci té do prostřed údolí.
Anakhazika anthuwo mokonzekera nkhondo. Gulu lalikulu la nkhondo linakamanga zithando zawo kumpoto kwa mzinda, ndipo gulu lina linakamanga zithando zawo kumadzulo kwa mzindawo. Usiku umenewo Yoswa anakagona ku chigwa.
14 I stalo se, že když je uzřel král Hai, pospíšili, a ráno vstavše, vyšli lidé města vstříc Izraelovi k boji, on i všecken lid jeho toho času před rovinu; nevěděl pak, že zálohy udělány byly jemu po zadu města.
Mfumu ya Ai itaona ankhondo a Yoswa, inachita zinthu mofulumira. Inadzuka mmamawa ndipo inapita pamodzi ndi anthu ake ku malo otsika oyangʼanana ndi Araba kuti akachite nkhondo ndi Aisraeli. Koma iyo sinadziwe kuti ayithira nkhondo kudzera kumbuyo kwa mzindawo.
15 I postoupil Jozue a všecken Izrael před nimi, a utíkali cestou pouště.
Yoswa ndi Aisraeli onse anachita ngati agonja ndi kumathawira ku chipululu.
16 I svolán jest všecken lid v městě, aby je honili. I honili Jozue, a vzdálili se od města svého,
Anthu onse a ku Ai anawuzidwa kuti awapirikitse. Ndipo iwo anapirikitsadi Yoswa uja, ndi kupita kutali ndi mzinda wawo.
17 Tak že nezůstal žádný z obyvatelů Hai a Bethel, kdo by nevyšel, aby honil Izraele; a nechali města otevřeného, a honili Izraele.
Palibe munthu wamwamuna wa mzinda wa Ai kapena wa Beteli amene sanatuluke kukapirikitsa Aisraeli. Iwo anasiya mzinda wosatseka ndi kumapirikitsa Aisraeli.
18 Řekl pak Hospodin k Jozue: Zdvihni korouhev, kterouž máš v rukou svých, proti Hai, nebo v ruce tvé dám je. I zdvihl Jozue korouhev, kterouž měl v ruce své, proti městu.
Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Loza mkondo uli mʼdzanja lako ku Ai pakuti ine ndipereka mʼdzanja lanu mzindawo.” Kotero Yoswa analoza mkondowo ku Ai.
19 Tedy, kteříž byli v zálohách, rychle vyskočili z místa svého, a běželi, když pozdvihl ruky své, a všedše do města, vzali je, a spěšně zapálili město ohněm.
Atangotambalitsa dzanja lake, anthu amene anabisala aja ananyamuka msangamsanga pamalo pawo ndi kuthamangira kutsogolo. Iwo analowa mu mzindamo ndi kuwulanda ndipo anawutentha mofulumira.
20 Muži pak města Hai ohlédše se nazpět, uzřeli, a aj, vstupoval dým města k nebi, a neměli místa k utíkání sem ani tam; nebo lid, kterýž utíkati počal k poušti, obrátil se na ty, kteříž je honili.
Anthu a ku Ai aja atangochewukira mʼmbuyo anaona utsi uli tolotolo. Koma mpata woti athawireko panalibe pakuti Aisraeli amene amathawira ku chipululu anabwerera nayamba kuwathamangitsa.
21 Jozue zajisté a všecken Izrael, když viděli, že z záloh vzali město, a že se vznáší dým města, obrátili se, a bili muže Hai.
Yoswa ndi Aisraeli onse ataona kuti obisalira aja alanda mzinda ndipo kuti utsi unali tolotolo, iwo anatembenuka ndi kuyamba kupha anthu a ku Ai.
22 Onino také vyšli z města proti nim, a obklíčil Izrael nepřátely své, jedni odsud, druzí od onud; a zmordovali je, tak že žádný živ nezůstal ani neušel.
Nawonso Aisraeli amene anali mu mzindamo anatuluka kudzalimbana ndi anthu a ku Ai. Choncho iwo anazingidwa mbali zonse ndi Aisraeli ndipo onse anaphedwa. Palibe amene anatsala wamoyo kapena wothawa
23 Ale krále Hai jali živého, a přivedli ho k Jozue.
kupatula mfumu ya ku Ai yokha imene anayigwira nabwera nayo kwa Yoswa.
24 Když pak pomordoval Izrael všecky obyvatele Hai v poli, totiž na poušti, kamž je honili, a padli ti všickni od ostrosti meče, až i zahlazeni jsou: navrátil se všecken Izrael do Hai, a zmordovali ostatky jeho mečem.
Aisraeli aja atatha kupha anthu onse a ku Ai amene anali mʼthengo ndi mʼchipululu kumene anawapirikitsira, onse anabwerera ku Ai ndi kupha onse amene anali mu mzindamo.
25 A bylo všech, kteříž padli v ten den, od muže až do ženy, dvanácte tisíců; všickni ti byli z Hai.
Chiwerengero cha anthu onse a ku Ai, amuna ndi akazi, amene anaphedwa pa tsiku limeneli chinali 12,000.
26 Ale Jozue nespustil ruky své, kterouž vyzdvihl korouhev, dokudž nebyli zmordováni všickni obyvatelé Hai.
Yoswa sanatsitse dzanja lake limene ananyamula mkondo mpaka ataona kuti onse amene amakhala mu mzinda wa Ai aphedwa.
27 Toliko hovada a loupež města toho rozbitovali mezi sebou synové Izraelští podlé slova Hospodinova, kteréž on přikázal Jozue.
Tsono Aisraeli anatenga zoweta ndi katundu yense wa anthu ophedwa aja, monga momwe Yehova analamulira Yoswa.
28 Tedy vypálil Jozue Hai, a položil je v hromadu věčnou a pustinu, až do tohoto dne.
Pambuyo pake Yoswa anawutentha mzinda wa Ai ndi kuwusiya bwinja monga ulili leromu.
29 Krále pak Hai oběsil na dřevě, a nechal ho tam až do večera. A když zapadlo slunce, rozkázal Jozue, aby složili tělo jeho s dřeva, a povrhli je u brány města, a nametali na ně hromadu kamení velikou, kteráž trvá až do dnešního dne.
Iye anapachika pa mtengo mfumu ya Ai ndipo anayisiya mpaka madzulo. Pomwe dzuwa linalowa Yoswa analamula kuti akachotse mtembowo ndi kukawutaya ku chipata cha mzindawo. Pamwamba pa mtembowo anawunjikapo mulu waukulu wa miyala. Muluwo ulipobe mpaka lero lino.
30 Tedy vzdělal Jozue oltář Hospodinu Bohu Izraelskému na hoře Hébal,
Ndipo Yoswa anamanga guwa lansembe la Yehova Mulungu wa Israeli pa phiri la Ebala.
31 (Jakož přikázal Mojžíš, služebník Hospodinův, synům Izraelským, jakož psáno jest v knize zákona Mojžíšova, ) oltář z kamení celého, nad nímž nebylo zdviženo železo, a obětovali na něm oběti zápalné Hospodinu, obětovali i oběti pokojné.
Analimanga motsata zimene Mose mtumiki wa Yehova analamulira Aisraeli, ndiponso potsata zomwe zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose kuti guwa lansembe likhale la miyala yosasemedwa ndi chitsulo. Pa guwalo anapereka kwa Yehova nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano.
32 Napsal také tam na kameních výpis zákona Mojžíšova, kterýž psal před syny Izraelskými.
Kenaka anthu onse akupenya, Yoswa analemba pa miyala chitsanzo cha malamulo amene Mose analemba.
33 Všecken pak Izrael a starší jeho, i správcové i soudcové jeho stáli po obou stranách truhly před kněžími Levítskými, kteříž nosili truhlu smlouvy Hospodinovy, tak cizí jako doma zrozený, polovice jich proti hoře Garizim, a polovice proti hoře Hébal, jakož byl prvé přikázal Mojžíš, služebník Hospodinův, aby dobrořečil lidu Izraelskému nejprvé.
Aisraeli onse, akuluakulu awo, atsogoleri awo ndi oweruza awo, alendo pamodzi ndi mbadwa, anayimirira mbali zonse ziwiri za Bokosi la Chipangano la Yehova, ena uku ena uku moyangʼanana ndi ansembe a Chilevi. Theka la anthu linayima patsogolo pa phiri la Gerizimu ndipo theka lina patsogolo pa phiri la Ebala, monga momwe Mose mtumiki wa Yehova anawalamulira mʼmbuyomo pamene anawapatsa malangizo podalitsa Aisraeli.
34 A potom četl všecka slova zákona, požehnání i zlořečení, tak jakž psáno jest v knize zákona.
Pambuyo pake Yoswa anawerenga mawu onse a malamulo, madalitso ndi matemberero monga momwe zinalembedwera mʼbuku la malamulo a Mose.
35 Nebylo ani slova ze všeho, což přikázal Mojžíš, jehož by nečetl Jozue přede vším shromážděním Izraelským, i ženami i dětmi i příchozími, kteříž šli u prostřed nich.
Yoswa anawerenga mawu onse amene Mose analamula, gulu lonse la Israeli limene linasonkhana likumva. Amayi, ana ndi alendo omwe okhala pakati pawo anali pomwepo.