< Józua 2 >

1 Poslal pak byl Jozue, syn Nun, z Setim dva muže špehéře tajně, řka: Jděte, shlédněte zemi, zvlášť Jericho. I šli a vešli do domu ženy nevěstky, jejíž jméno bylo Raab, a odpočinuli tu.
Tsono Yoswa mwana wa Nuni anatuma anthu awiri okazonda dziko mwachinsinsi kuchokera ku Sitimu. Iye anawawuza kuti, “Pitani mukaone dzikolo makamaka mzinda wa Yeriko.” Kotero iwo anapita ndipo anakafika ku nyumba ya mkazi wadama dzina lake Rahabe, ndipo anagona kumeneko.
2 Ale jakž oznámeno bylo králi Jericha a povědíno: Aj, muži přišli sem této noci z synů Izraelských, aby shlédli zemi,
Mfumu ya Yeriko inawuzidwa kuti, “Aisraeli ena afika mu mzinda muno usiku uno kudzazonda dziko.”
3 Tedy poslal král Jericha k Raab, řka: Vyveď muže, kteříž přišli k tobě, a vešli do domu tvého, nebo k vyšpehování vší země přišli.
Choncho Mfumu ya Yeriko inatumiza uthenga kwa Rahabe kuti, “Atulutse anthu amene abwera ku nyumba kwakowo chifukwa iwo abwera kuti adzazonde dzikoli.”
4 (Pojavši pak žena ty dva muže, skryla je.) Kteráž odpověděla: Pravda jest, přišliť jsou ke mně muži, ale nevěděla jsem, odkud jsou.
Koma pa nthawiyi nʼkuti mkaziyo atatenga amuna awiriwo ndi kuwabisa. Tsono anayankha kuti, “Inde, anthuwo anafikadi ku nyumba kuno. Koma sindinadziwe kumene anachokera.
5 A když bránu zavírati měli v soumrak, vyšli muži ti, a nevím, kam jsou šli; hoňte je rychle, nebo dostihnete jich.
Iwo achoka kuno ndi chisisira, chipata cha mzinda chili pafupi kutsekedwa. Ndiye sindidziwa kumene alowera. Koma mukawalondola msanga muwapeza.”
6 Ale ona rozkázala jim vstoupiti na střechu, a skryla je v pazdeří lněném, kteréž byla skladla na střeše.
Koma nʼkuti atawakweza pa denga azondiwo ndi kuwabisa pansi pa mapesi a thonje amene iye anawayika pa dengapo.
7 Muži pak vyslaní honili je cestou Jordánskou až k brodům; a zavřína jest brána, jakž vyšli ti, kteříž je honili.
Nthumwi za mfumu zija zitatuluka ndipo chipata chinatsekedwa. Nthumwizo zinapita kukawafunafuna azondi aja mpaka ku dooko la Yorodani.
8 Prvé pak, než usnuli špehéři, vstoupila k nim ona na střechu,
Azondiwo asanagone, Rahabe anakwera pa denga
9 A řekla mužům těm: Vím, že Hospodin dal vám zemi tuto, nebo připadl na nás strach váš, tak že oslábli všickni obyvatelé země před tváří vaší.
ndipo anawawuza kuti, “Ine ndikudziwa kuti Yehova wakupatsani dziko lino ndipo tili ndi mantha. Anthu onse a mʼdziko lino ali ndi mantha chifukwa cha inu.
10 Slyšeli jsme zajisté, jak vysušil Hospodin vody moře Rudého před tváří vaší, když jste vyšli z Egypta, a co jste učinili dvěma králům Amorejským, kteříž byli za Jordánem, Seonovi a Ogovi, kteréž jste zahladili jako proklaté.
Ife tinamva mmene Yehova anawumitsira madzi a Nyanja Yofiira inu mukufika pamene munatuluka mʼdziko la Igupto. Tamvanso zimene munachita kwa Sihoni ndi Ogi, mafumu awiri a Aamori amene ali kummawa kwa Yorodani. Inu munawawononga kotheratu.
11 Což když jsme uslyšeli, osláblo srdce naše, aniž zůstává více v kom duše před tváří vaší, nebo Hospodin Bůh váš jest Bůh na nebi svrchu, i na zemi dole.
Titamva zimenezi, ife tinataya mtima ndipo aliyense wa ife ali ndi mantha chifukwa cha inu. Tikudziwa kuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wa kumwamba ndi dziko lapansi.
12 Nyní tedy, prosím, přisáhněte mi skrze Hospodina, poněvadž jsem učinila vám milosrdenství, že i vy učiníte s domem otce mého milosrdenství, a dáte mi znamení jisté,
Choncho mulumbire pamaso pa Yehova ndi kundipatsa chizindikiro choti mudzachitadi zimene mwalonjeza, kuti monga inu ndakuchitirani chifundo, inunso mudzachitira chifundo a pa banja la abambo anga.
13 Že budete živiti otce mého i matku mou, bratří mé i sestry mé a všecko, cožkoli jejich jest, a vysvobodíte duše naše od smrti.
Inu mulonjeze kuti simudzapha abambo anga ndi amayi anga, abale anga ndi alongo anga ndi mabanja awo omwe.”
14 I řekli jí muži ti: Duše naše za vás nechť jsou na smrt; jestliže však nepronesete řeči naší této, takť se jistě stane, že když nám dá Hospodin zemi tuto, tehdy učiníme s tebou milosrdenství a pravdu.
Anthuwo anamuyankha kuti, “Ife ndife okonzeka kufa chifukwa cha inu. Ngati iwe sudzawulula zimene tachitazi, ndiye kuti ife tidzakukomera mtima ndi kusunga pangano lathu ndi iwe, Yehova akadzatipatsa dziko lino.”
15 Protož spustila je oknem po provazu; nebo dům její byl při zdi městské, a na zdi ona bydlila.
Popeza nyumba ya Rahabe inali pa linga la mzindawo, azondi aja anatulukira pa zenera. Rahabe anawatsitsa pansi ndi chingwe.
16 I řekla jim: Jděte k této hoře, aby se nepotkali s vámi, kteříž vás honí, a krejte se tam za tři dni, až se oni zase navrátí, a potom půjdete cestou svou.
Iye anawawuza kuti, “Pitani ku mapiri kuti okuthamangiraniwo asakupezeni. Mukabisale kumeneko masiku atatu mpaka iwo atabwerera, ndipo kenaka muzikapita kwanu.”
17 Tedy řekli muži k ní: Prosti budeme od této přísahy tvé, kterouž jsi zavázala nás,
Anthuwo anati kwa iye, “Lonjezo limene watichititsa ifeli tidzalisungadi
18 Jestliže, když vejdeme do země, neuvážeš provázku tohoto z nití hedbáví červeného dvakrát barveného v tomto okně, jímž jsi nás spustila, také otce svého a matky své, i bratří svých, a všeho domu otce svého neshromáždíš-li k sobě do domu.
tikadzalowa mʼdzikoli, iwe udzamangirire kansalu kofiira pa zenera limene unatitulutsira, ndi kusonkhanitsa abambo ako, amayi ako, abale ako ndi banja lako lonse mʼnyumba muno.
19 Také kdo by vyšel ven ze dveří domu tvého, krev jeho bude na hlavu jeho, ale my budeme bez viny; a každého toho, kdož bude s tebou v domě, jestliže by se kdo rukou dotekl, krev jeho na hlavy naše připadni.
Ngati wina aliyense adzatuluka mʼnyumbamo kuti azikayendayenda mu msewu, magazi ake adzakhala pamutu pake, ife sitidzapalamula kanthu. Koma wina aliyense wokhala mʼnyumba mwakomo akadzaphedwa, mlandu udzakhala wathu.
20 Jestliže pak proneseš tuto řeč naši, budeme prosti od přísahy tvé, kterouž jsi nás zavázala.
Komanso iwe ukangowulula zimene ife tikuchitazi ndiye kuti ife sitidzasunga zimene talonjezazi.”
21 Odpověděla ona: Nechť jest tak, jakž jste řekli. I propustila je a odešli; i uvázala provázek z hedbáví červeného dvakrát barveného v tom okně.
Rahabe anayankha kuti, “Zikhale monga mwaneneramo.” Kenaka iye anawatulutsa ndipo iwowo anapita. Pambuyo pake Rahabe anamangirira kansalu kofiira pa zenera paja.
22 Odšedše pak, přišli na horu, a pobyli tam za tři dni, dokudž se nenavrátili, kteříž je honili; nebo jich hledali ti, kteříž je honili po všech cestách, ale nic nenalezli.
Azondi aja anachoka napita ku mapiri ndipo anakhalako masiku atatu. Apa nʼkuti otumidwa ndi mfumu aja atawafunafuna ponseponse nʼkubwerera osawapeza.
23 Ti pak dva muži sšedše s hory, navrátili se a přeplavili se přes Jordán; i přišli k Jozue, synu Nun, a vypravovali jemu všecko, co se s nimi dálo.
Pambuyo pake azondi awiri aja anayamba ulendo wobwerera kwawo. Anatsika ku mapiri kuja, nawoloka mtsinje mpaka anakafika kwa Yoswa mwana wa Nuni. Ndipo anamuwuza zonse zimene zinawachitikira.
24 A řekli k Jozue: Dalť jest Hospodin v ruce naše všecku zemi, nebo se zděsili všickni obyvatelé země tváři naší.
Iwo anati kwa Yoswa, “Ndithu, Yehova wapereka dziko lonse mʼmanja mwathu. Anthu onse kumeneko akuchita nafe mantha.”

< Józua 2 >