< Józua 19 >

1 Potom padl los druhý Simeonovi, pokolení synů Simeonových, po čeledech jejich, a bylo dědictví jejich u prostřed dědictví synů Juda.
Maere achiwiri anagwera mabanja a fuko la Simeoni. Dziko lawo linali mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
2 A přišlo jim v dědictví jejich Bersabé, Seba a Molada;
Dzikolo linaphatikiza zigawo izi: Beeriseba (ndi Seba), Molada,
3 Azarsual a Bala, též Esem;
Hazari-Suwali, Bala, Ezemu,
4 Eltolad a Betul, a Horma;
Elitoladi, Betuli, Horima,
5 Sicelech a Betmarchabot, a Azarsusa;
Zikilagi, Beti-Marikaboti, Hazari-Susa,
6 Betlebaot a Sarohem, měst třinácte i vsi jejich;
Beti-Lebaoti ndi Saruheni. Yonse pamodzi inali mizinda 13 ndi midzi yawo.
7 Ain, Remmon, též Eter a Asan, města čtyři i vsi jejich;
Panalinso mizinda inayi iyi: Aini, Rimoni, Eteri ndi Asani pamodzi ndi midzi yawo.
8 I všecky vsi, kteréž byly vůkolí měst těch, až do Balatber a Rámat poledního. To jest dědictví pokolení synů Simeonových po čeledech jejich.
Dzikolo linaphatikizanso midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baalati-Beeri, ndiye kuti Rama wa kummwera. Ili ndi dziko limene mabanja a fuko la Simeoni analandira kukhala lawo.
9 Z podílu synů Judových bylo dědictví synů Simeonových; nebo díl synů Judových byl jim příliš veliký, protož u prostřed dědictví jejich vzali dědictví synové Simeonovi.
Cholowa cha fuko la Simeoni chinatengedwa kuchokera ku gawo la Yuda chifukwa fuko la Yuda linali lalikulu kwambiri. Izi zinachititsa fuko la Simeoni kukhala mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
10 Potom přišel třetí los synům Zabulon po čeledech jejich, a jest meze dědictví jejich až do Sarid.
Maere achitatu anagwera mabanja a fuko la Zebuloni: Malire a dziko lawo anafika mpaka ku Saridi.
11 Odkudž vstupuje meze jejich podlé moře k Merala, a přichází až do Debaset, a běží až ku potoku, kterýž jest proti Jekonam.
Malirewo anakwera kupita cha kumadzulo ku Marala nakafika ku Dabeseti ndi ku mtsinje wa kummawa kwa Yokineamu.
12 Obrací se pak od Sarid nazpátek k východu slunce, ku pomezí Chazelet Tábor, a odtud táhne se k Daberet, a vstupuje do Jafie.
Kuchokera ku mbali ina ya Saridi malire anakhota kupita kummawa ku malire a Kisiloti-Tabori mpaka ku Daberati nakwera mpaka ku Yafiya.
13 Odtud přechází zase k východu, do Gethefer a do Itakasin, odkudž vychází do Remmon, a točí se k Nea.
Kuchokera kumeneko anabzola kulowa cha kummawa mpaka ku Gati-Heferi ndi ku Eti Kazini ndi kumaloza ku Neya njira ya ku Rimoni.
14 Točí se také táž meze od půlnoci do Anaton, a dochází až k údolí Jeftael;
Mbali ya kumpoto malirewo analoza ku Hanatoni ndipo anakathera ku chigwa cha Ifita Eli.
15 A Katet, Naalol, Simron, Idala a Betlém, měst dvanácte i vsi jejich.
Anaphatikizapo Katati, Nahalala, Simironi, Idala ndi Betelehemu. Mizinda yonse inakwana khumi ndi iwiri pamodzi ndi midzi yake.
16 To jest dědictví synů Zabulonových po čeledech jejich, ta města i vsi jejich.
Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndi imene mabanja a fuko la Zebuloni analandira.
17 Izacharovi také padl los čtvrtý, totiž synům Izacharovým po čeledech jejich.
Maere achinayi anagwera mabanja a fuko la Isakara.
18 A meze jejich: Jezreel, Kasalat a Sunem;
Dziko lawo linaphatikiza zigawo izi: Yezireeli, Kesuloti, Sunemu,
19 Hafaraim, Sion, též Anaharat;
Hafaraimu, Sioni, Anaharati,
20 Rabbot, Kesion a Abez,
Rabiti, Kisoni, Ebezi,
21 Ramet, Engannim a Enhada, i Betfeses.
Remeti, Eni Ganimu, Eni Hada ndi Beti-Pazezi.
22 Odkudž přibíhá meze k Táboru a k Sehesima a k Betsemes, a dochází až k Jordánu, měst šestnácte i vsi jejich.
Malirewa anakafikanso ku Tabori, Sahazuma ndi Beti-Semesi ndipo anakathera ku Yorodani. Mizinda yonse inalipo 16 ndi midzi yake.
23 To jest dědictví pokolení synů Izacharových po čeledech jejich, ta města i vsi jejich.
Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Isakara.
24 Padl také los pátý pokolení synů Asser po čeledech jejich.
Maere achisanu anagwera mabanja a fuko la Aseri.
25 A byla meze jejich: Helkat a Chali, a Beten, a Achzaf;
Gawo lawo linaphatikiza Helikati, Hali, Beteni, Akisafu,
26 Elmelech, též Amaad a Mesal, a přibíhá až na Karmel k moři, a do Sichor Libnat;
Alameleki, Amadi ndi Misali. Kumadzulo malire anafika ku Karimeli ndi Sihori Libinati.
27 A obrací se k východu slunce do Betdagon, a dosahá k losu Zabulonovu, a do údolí Jeftael k půlnoci, a do Betemek a Nehiel, a táhne se do Kábul na levou stranu,
Kenaka anakhotera kummawa kulowera ku Beti-Dagoni nafika ku dziko la Zebuloni ndi ku chigwa cha Ifita Eli, ndipo anapita kumpoto ku Beti-Emeki ndi Neieli. Anapitirirabe kumpoto mpaka kukafika ku Kabuli,
28 A do Ebron a Rohob, a Hamon a Kána až do Sidonu velikého.
Ebroni, Rehobu, Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni Wamkulu.
29 Odtud se navrací ta meze do Ráma až k městu hrazenému Zor; tu se obrací do Chosa, a skonává se při moři podlé vyměření v Achziba.
Kenaka malirewo anakhotera ku Rama ndi kupita ku mzinda wotetezedwa wa ku Turo. Kuchokera pamenepo malirewo anakhota kupita ku Hosa nakatulukira ku Nyanja, mʼchigawo cha Akizibu,
30 K tomu přísluší Afek a Rohob, měst dvamecítma i vsi jejich.
Uma, Afeki ndi Rehobu. Mizinda yonse inalipo 22 pamodzi ndi midzi yake.
31 To jest dědictví pokolení synů Asser po čeledech jejich, ta města i vsi jejich.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Aseri.
32 Synům Neftalímovým padl los šestý, po čeledech jejich.
Maere achisanu ndi chimodzi anagwera mabanja a fuko la Nafutali.
33 A byla meze jejich od Helef a od Elon do Sananim, a Adami, Nekeb a Jebnael, až do Lekum, a skonává se u Jordánu.
Malire awo anayambira ku Helefu mpaka ku mtengo wa thundu wa ku Zaananimu, ndipo anapitirira nʼkukafika ku Adami Nekebu, Yabineeli mpaka ku Lakumi ndi kukathera ku Yorodani.
34 Potom navracuje se meze na západ k Azanot Tábor, a odtud jde do Hukuka, a vpadá k Zabulonovu od poledne, a k Asserovu přibíhá od západu, a k Judovu při Jordánu na východ slunce.
Tsono malirewo anakhotera kumadzulo kupita ku Azinoti-Tabori. Kuchoka kumeneko anapita ku Hukoki, modutsa Zebuloni cha kummwera, Aseri cha kumadzulo ndi mtsinje wa Yorodani cha kummawa.
35 Města pak hrazená jsou: Assedim, Ser a Emat, Rechat a Ceneret;
Mizinda yotetezedwa inali Zidimi, Zeri, Hamati, Rakati, Kinereti,
36 Adama, Ráma a Azor;
Adama, Rama, Hazori,
37 Kedes, Edrei a Enazor;
Kedesi, Ederi, Eni Hazori,
38 Jeron, Magdalel, Horem, Betanat a Betsemes, měst devatenácte i vsi jejich.
Yironi, Migidali Eli, Horemu, Beti-Anati ndi Beti-Semesi. Yonse pamodzi inalipo mizinda 19 ndi midzi yake.
39 To jest dědictví pokolení synů Neftalím po čeledech jejich, ta města s vesnicemi svými.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yawo ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Nafutali.
40 Na pokolení synů Dan po čeledech jejich padl los sedmý.
Maere achisanu ndi chiwiri anagwera mabanja a fuko la Dani.
41 A byla meze dědictví jejich: Zaraha a Estaol, a Hirsemes;
Gawo lawo linaphatikiza mizinda iyi: Zora, Esitaoli, Iri Semesi,
42 Salbin, Aialon a Jetela;
Saalabini, Ayaloni, Itira,
43 Elon, Tamna a Ekron;
Eloni, Timna, Ekroni,
44 Elteke, Gebbeton a Baalat;
Eliteke, Gibetoni, Baalati,
45 Jehud, Beneberak a Getremmon;
Yehudi, Beni Beraki, Gati-Rimoni,
46 Mehaiarkon a Rakon s pomezím, kteréž jest naproti Joppe.
Me-Yarikoni ndi Rakoni, pamodzi ndi dera loyangʼanana ndi Yopa.
47 Přišlo pak pomezí synům Dan příliš malé. Protož vstoupili synové Dan, a bojovali proti Lesen, a dobyvše ho, pobili obyvatele ostrostí meče, a vzavše je v dědictví, bydlili tam, a přezděli Lesenu Dan, vedlé jména Dan otce svého.
Anthu a fuko la Dani atalandidwa dziko lawo, anapita kukathira nkhondo Lesemu. Iwo anapha anthu ake onse, nawulandiratu mzindawo, kuwusandutsa wawo ndi kumakhalamo. Tsono anatcha mzindawo dzina loti Dani popeza ndilo linali dzina la kholo lawo.
48 To jest dědictví pokolení synů Dan po čeledech jejich, ta města i vsi jejich.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Dani.
49 Když pak přestali děliti se zemí po mezech jejích, dali synové Izraelští dědictví Jozue, synu Nun, mezi sebou.
Atatha kugawana zigawo zosiyanasiyana za dzikolo, Aisraeli anamupatsa Yoswa mwana wa Nuni chigawo chake.
50 Podlé rozkázaní Hospodinova dali jemu město, kteréhož žádal, Tamnatsára, na hoře Efraim. I vystavěl město, a přebýval v něm.
Potsata zimene Yehova anawalamula, anamupatsa mzinda wa Timnati-Sera umene anawupempha. Mzindawu unali mʼdziko lamapiri la Efereimu. Iye anawumanga mzindawu ndi kukhazikikako.
51 Ta jsou dědictví, kteráž dali k vládařství Eleazar kněz a Jozue syn Nun, i přední z otců pokolení synů Izraelských, losem v Sílo před Hospodinem, u dveří stánku úmluvy, a tak dokonali rozdělování země.
Wansembe Eliezara, Yoswa ndi atsogoleri a mabanja onse a Israeli anagawa dziko lija zigawozigawo pogwiritsa ntchito maere pamaso pa Yehova. Izi zinachitika ku Silo pa khomo la tenti ya msonkhano. Choncho anamaliza kugawa dzikolo.

< Józua 19 >