< Jonáš 3 >

1 I stalo se slovo Hospodinovo k Jonášovi podruhé, řkoucí:
Ndipo Yehova anayankhula ndi Yona kachiwiri kuti,
2 Vstaň, jdi do Ninive města toho velikého, a kaž proti němu to, což já poroučím tobě.
“Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire uthenga umene ndikupatsa.”
3 Tedy vstav Jonáš, šel do Ninive podlé slova Hospodinova. (Bylo pak Ninive město velmi veliké, cesty tří dnů.)
Yona anamvera mawu a Yehova ndipo anapita ku Ninive. Tsono Ninive unali mzinda waukulu kwambiri; wofunika masiku atatu kuwudutsa.
4 A jakž počal byl Jonáš jíti po městě cestou dne jednoho a volati, pravě: Po čtyřidcíti dnech Ninive vyvráceno bude,
Yona analowa mu mzindawo, nayenda ulendo wa tsiku limodzi. Iye ankalalikira kuti, “Atsala masiku makumi anayi kuti Ninive awonongedwe.”
5 Tedy uvěřili Ninivitští Bohu, a vyhlásivše půst, oblékli se v žíně, od největšího z nich až do nejmenšího z nich.
Anthu a ku Ninive anakhulupirira Mulungu. Analengeza kuti aliyense, wamkulu ndi wamngʼono yemwe asale zakudya ndipo avale chiguduli.
6 Nebo jakž došla ta řeč krále Ninivitského, vstav s trůnu svého, složil s sebe oděv svůj, a přioděv se žíní, seděl v popele.
Mfumu ya ku Ninive itamva nkhaniyi, inatsika pa mpando wake waufumu, nivula mkanjo wake waufumu ndipo inavala chiguduli ndi kukhala pansi pa fumbi.
7 A dal provolati a oznámiti v Ninive z usouzení královského i knížat svých, takto řka: Lidé i hovada, volové i ovce, neokoušejte ničeho, nepaste se, ani vody nepíte.
Tsono mfumuyo inalengeza mu Ninive kuti, “Mwa lamulo lochokera kwa mfumu ndi akalonga ake: “Munthu aliyense kapenanso nyama, ngʼombe kapena nkhosa, zisadye kanthu kalikonse; musazilole kuti zidye kapena kumwa.
8 Ale přiodějte se žíněmi lidé i hovada, a volejte k Bohu horlivě, a odvrať se jeden každý od cesty své zlé, i loupeže, kteráž jest v rukou jeho.
Koma anthu avale ziguduli, ndipo nyamanso aziveke ziguduli. Munthu aliyense azifuwula kwa Mulungu ndi mphamvu zake zonse. Anthuwo asiye makhalidwe awo oyipa ndi machitidwe achiwawa.
9 Kdo ví, neobrátí-li se a nebude-li želeti toho Bůh; neodvrátí-li se, pravím, od prchlivosti hněvu svého, abychom nezahynuli.
Angadziwe ndani? Mwina Mulungu nʼkutikhululukira ndipo mwa chifundo chake nʼkuleka kutikwiyira, ifeyo osawonongedwa.”
10 I viděl Bůh skutky jejich, že se odvrátili od cesty své zlé, a lítost měl Bůh nad tím zlým, kteréž řekl učiniti jim. A neučinil.
Mulungu ataona zimene anthuwo anachita, ndi mmene anasiyira makhalidwe awo oyipa, anawachitira chifundo ndipo sanabweretse chiwonongeko chimene anawaopseza nacho.

< Jonáš 3 >