< Joel 2 >

1 Trubte trubou na Sionu, a křičte na hoře svaté mé, nechť se třesou všickni obyvatelé této země, nebo přichází den Hospodinův, nebo blízký jest,
Lizani lipenga mu Ziyoni. Chenjezani pa phiri langa loyera. Onse okhala mʼdziko anjenjemere, pakuti tsiku la Yehova likubwera, layandikira;
2 Den temnosti a mračna, den oblaku a mrákoty, jako záře jitřní rozprostřená po horách: Lid mnohý a silný, jemuž rovného nebylo od věků, aniž po něm kdy bude až do let národů i pronárodů.
tsiku la mdima ndi chisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani. Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri, gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera, gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.
3 Před tváří jeho oheň zžírati bude, a za ním plamen plápolati; před ním země tato jako zahrada Eden, ale po něm bude poušť přehrozná, a aniž bude, což by ušlo před ním.
Patsogolo pawo moto ukupsereza, kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu. Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni, kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu, kulibe kanthu kotsalapo.
4 Způsob jeho bude jako způsob koní, a jako jízdní, tak poběhnou.
Maonekedwe awo ali ngati akavalo; akuthamanga ngati akavalo ankhondo.
5 Jako s hřmotem vozů po vrších hor skákati budou, jako hluk plamene ohně zžírajícího strniště, jako lid silný zšikovaný k bitvě.
Akulumpha pamwamba pa mapiri ndi phokoso ngati la magaleta, ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu, ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.
6 Tváři jeho děsiti se budou lidé, všecky tváře zčernají jako hrnec.
Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima; nkhope iliyonse imagwa.
7 Jako rekové poběhnou, jako muži váleční vstoupí na zed, a jeden každý cestou svou půjde, aniž se uchýlí z stezek svých.
Amathamanga ngati ankhondo; amakwera makoma ngati asilikali. Onse amayenda pa mizere, osaphonya njira yawo.
8 Jeden druhého nebude tlačiti, každý silnicí svou půjde, a byť i na meč upadli, nebudou raněni.
Iwo sakankhanakankhana, aliyense amayenda molunjika. Amadutsa malo otchingidwa popanda kumwazikana.
9 Po městě těkati budou, po zdech běhati, na domy vstupovati, a okny polezou jako zloděj.
Amakhamukira mu mzinda, amathamanga mʼmbali mwa khoma. Amakwera nyumba ndi kulowamo; amalowera pa zenera ngati mbala.
10 Před tváří jeho třásti se bude země, pohnou se nebesa, slunce i měsíc se zatmí, a hvězdy potratí blesk svůj.
Patsogolo pawo dziko limagwedezeka, thambo limanjenjemera, dzuwa ndi mwezi zimachita mdima, ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.
11 Hospodin pak sám vydá hlas svůj před vojskem svým, proto že velmi veliký bude tábor jeho, proto že silný ten, kdož vykoná slovo jeho. (Nebo veliký bude den Hospodinův a hrozný náramně), i kdož jej bude moci snésti?
Yehova amabangula patsogolo pawo, gulu lake lankhondo ndi losawerengeka, ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake. Tsiku la Yehova ndi lalikulu; ndi loopsa. Ndani adzapirira pa tsikulo?
12 A protož ještě nyní dí Hospodin: Obraťte se ke mně samému celým srdcem svým, a to s postem a s pláčem i s kvílením.
“Ngakhale tsopano, bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.
13 A roztrhněte srdce vaše, a ne roucha vaše, a navraťte se k Hospodinu Bohu vašemu; neboť jest on milostivý a lítostivý, dlouhočekající a hojný v milosrdenství, a kterýž lituje zlého.
Ngʼambani mtima wanu osati zovala zanu. Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu, pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka, ndipo amaleka kubweretsa mavuto.
14 Kdo ví, neobrátí-li se a nebude-li želeti, a nezůstaví-li po něm požehnání, oběti suché a mokré Hospodinu Bohu vašemu.
Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni, nʼkutisiyira madalitso, a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa kwa Yehova Mulungu wanu.
15 Trubte trubou na Sionu, uložte půst, svolejte shromáždění.
Lizani lipenga mu Ziyoni, lengezani tsiku losala zakudya, itanitsani msonkhano wopatulika.
16 Shromažďte lid, posvěťte shromáždění, shromažďte starce, shromažďte maličké i ty, jenž prsí požívají; nechť vyjde ženich z pokojíka svého a nevěsta z schrany své.
Sonkhanitsani anthu pamodzi, muwawuze kuti adziyeretse; sonkhanitsani akuluakulu, sonkhanitsani ana, sonkhanitsani ndi oyamwa omwe. Mkwati atuluke mʼchipinda chake, mkwatibwi atuluke mokhala mwake.
17 Kněží, služebníci Hospodinovi, ať plačí mezi síňcí a oltářem, a řeknou: Odpusť, ó Hospodine, lidu svému, a nevydávej dědictví svého v pohanění, tak aby nad nimi panovati měli pohané. Proč mají říkati mezi národy: Kde jest Bůh jejich?
Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova, alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova. Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu. Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka, kuti anthu a mitundu ina awalamulire. Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti, ‘Ali kuti Mulungu wawo?’”
18 I bude horlivou milostí zažžen Hospodin k zemi své, a slituje se nad lidem svým.
Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake ndi kuchitira chisoni anthu ake.
19 A ohlásí se Hospodin, a řekne lidu svému: Aj, já pošli vám obilé, mest a olej, i budete jím nasyceni, aniž vás vydám více v pohanění mezi pohany.
Yehova adzawayankha kuti, “Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta ndipo mudzakhuta ndithu; sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo kwa anthu a mitundu ina.
20 Nebo půlnoční vojsko vzdálím od vás, a zaženu je do země vyprahlé a pusté, přední houf jeho k moři východnímu, konec pak jeho k moři nejdalšímu; i vzejde z něho smrad a puch, jakžkoli sobě mocně počíná.
“Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu, kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu, gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo. Ndipo mitembo yawo idzawola, fungo lake lidzamveka.” Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
21 Neboj se země, plésej a vesel se; neboť mocně dělati bude Hospodin dílo své.
Iwe dziko usachite mantha; sangalala ndipo kondwera. Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
22 Nebojtež se zvířátka polí mých; neboť se zotaví pastviska na poušti, a stromoví přinese ovoce své, fík i vinný kmen vydadí moc svou.
Inu nyama zakuthengo, musachite mantha, pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira. Mitengo ikubala zipatso zake; mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.
23 I vy, synové Sionští, plésejte a veselte se v Hospodinu Bohu vašem; nebo vám dá déšť příhodný, a sešle vám déšť hojný, podzimní i jarní, v čas.
Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani, kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu, pakuti wakupatsani mvula yoyambirira mwachilungamo chake. Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka, mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
24 I budou naplněny stodoly obilím, a oplývati budou presové mstem a olejem.
Pa malo opunthira padzaza tirigu; mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.
25 A tak nahradím vám léta, kteráž sežraly kobylky, brouci, chroustové a housenky, vojsko mé veliké, kteréž jsem posílal na vás.
“Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe, dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono, dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka; gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
26 Budete zajisté míti co jísti, a nasyceni jsouce, chváliti budete jméno Hospodina Boha svého, kterýž učinil s vámi divné věci, aniž zahanben bude lid můj na věky.
Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta, ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu, amene wakuchitirani zodabwitsa; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
27 A poznáte, že já jsem u prostřed Izraele, a že já Hospodin jsem Bohem vaším, a že není žádného jiného; neboť nebude zahanben lid můj na věky.
Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli, kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndi kuti palibenso wina; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
28 I stane se potom, že vyleji Ducha svého na všeliké tělo, a budou prorokovati synové vaši i dcery vaše; starci vaši sny mívati budou, mládenci vaši vidění vídati budou.
“Ndipo patapita nthawi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera, nkhalamba zanu zidzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya.
29 Nýbrž i na služebníky a na služebnice v těch dnech vyleji Ducha svého,
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
30 A ukáži zázraky na nebi i na zemi, krev a oheň a sloupy dymové.
Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi pa dziko lapansi, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
31 Slunce obrátí se v tmu a měsíc v krev, prvé než přijde den Hospodinův veliký a hrozný,
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
32 A však stane se, že kdož by koli vzýval jméno Hospodinovo, vysvobozen bude; nebo na hoře Sion a v Jeruzalémě bude vysvobození, jakož pověděl Hospodin, totiž v ostatcích, kterýchž povolá Hospodin.
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka; pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu, monga Yehova wanenera, pakati pa otsala amene Yehova wawayitana.

< Joel 2 >