< Jób 40 >

1 A tak odpovídaje Hospodin Jobovi, řekl:
Yehova anati kwa Yobu:
2 Zdali hádající se s Všemohoucím obviní jej? Kdo chce viniti Boha, nechť odpoví na to.
“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
3 Tehdy odpověděl Job Hospodinu a řekl:
Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
4 Aj, chaternýť jsem, což bych odpovídal tobě? Ruku svou kladu na ústa svá.
“Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
5 Jednou jsem mluvil, ale nebudu již odmlouvati, nýbrž i podruhé, ale nebudu více přidávati.
Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
6 Ještě odpovídaje Hospodin z vichru Jobovi, i řekl:
Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
7 Přepaš nyní jako muž bedra svá, a nač se tebe tázati budu, oznam mi.
“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
8 Zdaliž pak i soud můj zrušiti chceš? Což mne odsoudíš, jen abys se sám ospravedlnil?
“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
9 Èili máš rámě jako Bůh silný, a hlasem jako on hřímáš?
Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
10 Ozdobiž se nyní vyvýšeností a důstojností, v slávu a okrasu oblec se.
Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
11 Rozprostři prchlivost hněvu svého, a pohleď na všelikého pyšného, a sniž ho.
Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
12 Pohleď, pravím, na všelikého pyšného, a sehni jej, anobrž setři bezbožné na místě jejich.
Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
13 Skrej je v prachu spolu, tvář jejich zavěž v skrytě.
Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
14 A tak i já budu tě oslavovati, že tě zachovává pravice tvá.
Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
15 Aj, hle slon, jejž jsem jako i tebe učinil, trávu jí jako vůl.
“Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
16 Aj, hle moc jeho v bedrách jeho, a síla jeho v pupku břicha jeho.
Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
17 Jak chce, ohání ocasem svým, ačkoli jest jako cedr; žily lůna jeho jako ratolesti jsou spletené.
Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
18 Kosti jeho jako trouby měděné, hnátové jeho jako sochor železný.
Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
19 Onť jest přední z účinků Boha silného, učinitel jeho sám na něj doložiti může meč svůj.
Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
20 Hory zajisté přinášejí mu pastvu, a všecka zvěř polní hrá tam.
Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
21 V stínu léhá, v soukromí mezi třtím a bahnem.
Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
22 Dříví stín dávající stínem svým jej přikrývá, a vrbí potoční obkličuje jej.
Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
23 Aj, zadržuje řeku tak, že nemůže pospíchati; tuší sobě, že požře Jordán v ústa svá.
Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
24 Zdaž kdo před očima jeho polapí jej, aneb provazy protáhne chřípě jeho?
Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?

< Jób 40 >