< Jób 4 >

1 Jemuž odpovídaje Elifaz Temanský, řekl:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 Počneme-li mluviti s tebou, neponeseš-liž toho těžce? Ale kdož by se zdržeti mohl, aby neměl mluviti?
“Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
3 Aj, učívals mnohé, a rukou opuštěných jsi posiloval.
Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
4 Padajícího pozdvihovals řečmi svými, a kolena zemdlená jsi zmocňoval.
Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
5 Nyní pak, jakž toto přišlo na tebe, těžce to neseš, a jakž tě dotklo, předěšen jsi.
Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
6 Nebylo-liž náboženství tvé nadějí tvou, a upřímost cest tvých očekáváním tvým?
Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
7 Rozpomeň se, prosím, kdo jest kdy nevinný zahynul? Aneb kde upřímí vyhlazeni jsou?
“Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
8 Jakož jsem já vídal ty, kteříž orali nepravost, a rozsívali převrácenost, že ji i žali.
Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
9 Od dchnutí Božího hynou, a duchem prchlivosti jeho v nic obracíni bývají.
Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
10 Řvání lva a hlas lvice a zubové mladých lvíčat setříni bývají.
Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
11 Hyne lev, že nemá loupeže, a lvíčata mladá rozptýlena bývají.
Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
12 Nebo i tajně doneslo se mne slovo, a pochopilo ucho mé něco maličko toho.
“Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
13 V přemyšlováních z vidění nočních, když připadá tvrdý sen na lidi,
Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
14 Strach připadl na mne a lekání, kteréž předěsilo všecky kosti mé.
ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
15 Duch zajisté před tváří mou šel, tak že vlasové vstávali na těle mém.
Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
16 Zastavil se, ale neznal jsem tváři jeho; tvárnost jen byla před očima mýma. Mezi tím mlče, slyšel jsem hlas:
Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
17 Zdaliž může člověk spravedlivějším býti než Bůh, aneb muž čistším nad toho, kterýž ho učinil?
‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
18 Ano mezi služebníky jeho není dokonalosti, a při andělích svých zanechal nedostatku.
Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
19 Èím více při těch, kteříž bydlejí v domích hliněných, jejichž základ jest na prachu, a setříni bývají snáze než mol.
nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
20 Od jitra až do večera stíráni bývají, a kdož toho nerozvažují, na věky zahynou.
Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
21 Zdaliž nepomíjí sláva jejich s nimi? Umírají, ale ne v moudrosti.
Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’

< Jób 4 >