< Jób 39 >

1 Víš-li, kterého času rodí kamsíkové, a laň ku porodu pracující spatřil-lis?
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
2 Máš-li v počtu měsíce, kteréž vyplňují? Znáš-li, pravím, čas porodu jejich?
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
3 Jak se kladou, plod svůj utiskají, a s bolestí ho pozbývají?
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
4 Jak se zmocňují mladí jejich, i odchovávají picí polní, a vycházejíce, nenavracují se k nim?
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
5 Kdo propustil zvěř, aby byla svobodná? A řemení divokého osla kdo rozvázal?
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
6 Jemuž jsem dal pustinu místo domu jeho, a místo příbytku jeho zemi slatinnou.
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
7 Posmívá se hluku městskému, a na křikání toho, kdož by jej honil, nic nedbá.
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
8 To, což nachází v horách, jest pastva jeho; nebo toliko zeliny hledá.
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
9 Svolí-liž jednorožec, aby tobě sloužil, a u jeslí tvých aby nocoval?
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 Připřáhneš-liž provazem jednorožce k orání? Bude-liž vláčeti brázdy za tebou?
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 Zdaž se na něj ubezpečíš, proto že jest veliká síla jeho, a poručíš jemu svou práci?
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 Zdaž se jemu dověříš, že sveze semeno tvé, a na humno tvé shromáždí?
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
13 Ty-lis dal pávům křídlo pěkné, aneb péro čápu neb pstrosu?
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 A že opouští na zemi vejce svá, ačkoli je v prachu osedí,
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 Nic nemysle, že by je noha potlačiti, aneb zvěř polní pošlapati mohla?
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 Tak se zatvrzuje k mladým svým, jako by jich neměl; jako by neužitečná byla práce jeho, tak jest bez starosti.
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 Nebo nedal jemu Bůh moudrosti, aniž mu udělil rozumnosti.
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
18 Èasem svým zhůru se vznášeje, posmívá se koni i jezdci jeho.
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
19 Zdaž ty dáti můžeš koni sílu? Ty-li ozdobíš šíji jeho řehtáním?
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 Zdali jej zastrašíš jako kobylku? Anobrž frkání chřípí jeho strašlivé jest.
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 Kopá důl, a pléše v síle své, vycházeje vstříc i zbroji.
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 Směje se strachu, aniž se leká, aniž ustupuje zpátkem před ostrostí meče,
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 Ač i toul na něm chřestí, a blyští se dřevce a kopí.
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 S hřmotem a s hněvem kopá zemi, aniž pokojně stojí k zvuku trouby.
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 Anobrž k zvuku trouby řehce, a zdaleka cítí boj, hluk knížat a prokřikování.
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
26 Zdali podlé rozumu tvého létá jestřáb, roztahuje křídla svá na poledne?
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 Zdali k rozkazu tvému zhůru se vznáší orlice, a vysoko se hnízdí?
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 Na skále přebývá, přebývá na špičaté skále jako na hradě,
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 Odkudž hledá pokrmu, kterýž z daleka očima svýma spatřuje.
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
30 Ano i mladí její střebí krev, a kde těla mrtvá, tu i ona jest.
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”

< Jób 39 >