< Jób 38 >

1 Tedy odpověděl Hospodin Jobovi z vichru, a řekl:
Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
2 Kdož jest to, jenž zatemňuje radu řečmi neumělými?
“Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
3 Přepaš nyní jako muž bedra svá, a nač se tebe tázati budu, oznam mi.
Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
4 Kdes byl, když jsem zakládal zemi? Pověz, jestliže máš rozum.
“Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
5 Kdo rozměřil ji, víš-li? Aneb kdo vztáhl pravidlo na ni?
Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
6 Na čem podstavkové její upevněni jsou? Aneb kdo založil úhelný kámen její,
Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
7 Když prozpěvovaly spolu hvězdy jitřní, a plésali všickni synové Boží?
pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
8 Aneb kdo zavřel jako dveřmi moře, když vyšlo z života, a zjevilo se?
“Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
9 Když jsem mu položil oblak za oděv, a mrákotu místo plének jeho,
pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
10 Když jsem jemu uložil úsudek svůj, přistaviv závory a dvéře,
pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
11 I řekl jsem: Až potud vycházeti budeš, a dále nic, tu, pravím, skládati budeš dutí vlnobití svého.
Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
12 Zdaž jsi kdy za dnů svých rozkázal jitru? Ukázal-lis záři jitřní místo její,
“Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
13 Aby uchvacovala kraje země, a bezbožní aby z ní vymítáni byli?
kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
14 Tak aby proměnu přijímala jako vosk pečetní, oni pak aby nedlouho stáli jako roucho,
Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
15 A aby bezbožným zbraňováno bylo světla jejich, a rámě vyvýšené zlámáno bylo?
Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
16 Přišel-lis až k hlubinám mořským? A u vnitřnosti propasti chodil-lis?
“Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
17 Jsou-li tobě zjeveny brány smrti? A brány stínu smrti viděl-lis?
Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
18 Shlédl-lis širokosti země? Oznam, jestliže ji znáš všecku.
Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
19 Která jest cesta k obydlí světla, a které místo temností,
“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
20 Že bys je pojal v meze jeho, poněvadž bys srozumíval stezkám domu jeho?
Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
21 Věděl-lis tehdáž, že jsi měl se naroditi, a počet dnů tvých jak veliký býti má?
Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
22 Přišel-lis až ku pokladům sněhu? A poklady krupobití viděl-lis,
“Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
23 Kteréž chovám k času ssoužení, ke dni bitvy a boje?
zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
24 Kterými se cestami rozděluje světlo, kteréž rozhání východní vítr po zemi?
Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
25 Kdo rozdělil povodní tok, a cestu blýskání hromovému,
Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
26 Tak aby pršel déšť i na tu zemi, kdež není lidí, na poušť, kdež není člověka,
kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
27 Aby zapájel místa planá a pustá, a k zrůstu přivodil trávu mladistvou?
kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
28 Má-liž déšť otce? A kdo plodí krůpěje rosy?
Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
29 Z čího života vychází mráz? A jíní nebeské kdo plodí?
Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
30 Až i vody jako v kámen se proměňují, a svrchek propasti zamrzá.
pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
31 Zdali zavázati můžeš rozkoše Kuřátek, aneb stahování Orionovo rozvázati?
“Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
32 Můžeš-li vyvoditi hvězdy polední v čas jistý, aneb Arktura s syny jeho povedeš-li?
Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
33 Znáš-li řád nebes? Můžeš-li spravovati panování jejich na zemi?
Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
34 Můžeš-li pozdvihnouti k oblaku hlasu svého, aby hojnost vod přikryla tebe?
“Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
35 Ty-liž vypustíš blýskání, aby vycházela? Zdaliž řeknou tobě: Aj teď jsme?
Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
36 Kdo složil u vnitřnostech lidských moudrost? Aneb kdo dal rozumu stižitelnost?
Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
37 Kdo vypravovati bude o nebesích moudře? A láhvice nebeské kdo nastrojuje,
Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
38 Aby svlažená země zase stuhnouti mohla, a hrudy se v hromadě držely?
pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
39 Honíš-liž ty lvu loupež? A hltavost lvíčat naplňuješ-liž,
“Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
40 Když se stulují v peleších svých, ustavičně z skrýší čihajíce?
pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
41 Kdo připravuje krkavci pokrm jeho, když mladí jeho k Bohu silnému volají, a toulají se sem i tam pro nedostatek pokrmu?
Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?

< Jób 38 >