< Jób 33 >
1 Slyšiž tedy, prosím, Jobe, řeči mé, a všech slov mých ušima svýma pozoruj.
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 Aj, jižť otvírám ústa svá, mluví jazyk můj v ústech mých.
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 Upřímost srdce mého a umění vynesou rtové moji.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 Duch Boha silného učinil mne, a dchnutí Všemohoucího dalo mi život.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 Můžeš-li, odpovídej mi, připrav se proti mně, a postav se.
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 Aj, já podlé žádosti tvé buduť místo Boha silného; z bláta sformován jsem i já.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 Pročež strach ze mne nepředěsí tě, a ruka má nebudeť k obtížení.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 Řekl jsi pak přede mnou, a hlas ten řečí tvých slyšel jsem:
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 Èist jsem, bez přestoupení, nevinný jsem, a nepravosti při mně není.
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 Aj, příčiny ku potření mne shledal Bůh, klade mne sobě za nepřítele,
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 Svírá poutami nohy mé, střeže všech stezek mých.
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 Aj, tím nejsi spravedliv, odpovídám tobě, nebo větší jest Bůh nežli člověk.
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Oč se s ním nesnadníš? Žeť všech svých věcí nezjevuje?
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 Ano jednou mluví Bůh silný, i dvakrát, a nešetří toho člověk.
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 Skrze sny u vidění nočním, když připadá hluboký sen na lidi ve spaní na ložci,
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 Tehdáž odkrývá ucho lidem, a čemu je učí, to zpečeťuje,
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 Aby odtrhl člověka od skutku zlého, a pýchu od muže vzdálil,
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 A zachoval duši jeho od jámy, a život jeho aby netrefil na meč.
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 Tresce i bolestí na lůži jeho, a všecky kosti jeho násilnou nemocí,
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 Tak že sobě život jeho oškliví pokrm, a duše jeho krmi nejlahodnější.
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 Hyne tělo jeho patrně, a vyhlédají kosti jeho, jichž prvé nebylo vídati.
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 A tak bývá blízká hrobu duše jeho, a život jeho smrtelných ran.
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 Však bude-li míti anděla vykladače jednoho z tisíce, kterýž by za člověka oznámil pokání jeho:
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 Tedy smiluje se nad ním, a dí: Vyprosť jej, ať nesstoupí do porušení, oblíbilť jsem mzdu vyplacení.
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 I odmladne tělo jeho nad dítěcí, a navrátí se ke dnům mladosti své.
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 Kořiti se bude Bohu, a zamiluje jej, a patřiti bude na něj tváří ochotnou; nadto navrátí člověku spravedlnost jeho.
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 Kterýž hledě na lidi, řekne: Zhřešilť jsem byl, a to, což pravého bylo, převrátil jsem, ale nebylo mi to prospěšné.
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 Bůh však vykoupil duši mou, aby nešla do jámy, a život můj, aby světlo spatřoval.
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 Aj, všeckoť to dělá Bůh silný dvakrát i třikrát při člověku,
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 Aby odvrátil duši jeho od jámy, a aby osvícen byl světlem živých.
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 Pozoruj, Jobe, poslouchej mne, mlč, ať já mluvím.
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 Jestliže máš slova, odpovídej mi, nebo bych chtěl ospravedlniti tebe.
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 Pakli nic, ty mne poslouchej; mlč, a poučím tě moudrosti.
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”