< Jób 29 >

1 Ještě dále Job vedl řeč svou, a řekl:
Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 Ó bych byl jako za časů předešlých, za dnů, v nichž mne Bůh zachovával,
“Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
3 Dokudž svítil svící svou nad hlavou mou, při jehož světle chodíval jsem v temnostech,
pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
4 Tak jako jsem byl za dnů mladosti své, dokudž přívětivost Boží byla v stanu mém,
Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
5 Dokudž ještě Všemohoucí byl se mnou, a všudy vůkol mne dítky mé,
nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
6 Když šlepěje mé máslem oplývaly, a skála vylévala mi prameny oleje,
pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
7 Když jsem vycházel k bráně skrze město, a na ulici strojíval sobě stolici svou.
“Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
8 Jakž mne spatřovali mládenci, skrývali se, starci pak povstávali a stáli.
anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
9 Knížata choulili se v řečech, anobrž ruku kladli na ústa svá.
atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
10 Hlas vývod se tratil, a jazyk jejich lnul k dásním jejich.
anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
11 Nebo ucho slyše, blahoslavilo mne, a oko vida, posvědčovalo mi,
Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
12 Že vysvobozuji chudého volajícího, a sirotka, i toho, kterýž nemá spomocníka.
chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
13 Požehnání hynoucího přicházelo na mne, a srdce vdovy k plésání jsem vzbuzoval.
Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
14 V spravedlnost jsem se obláčel, a ona ozdobovala mne; jako plášť a koruna byl soud můj.
Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
15 Místo očí býval jsem slepému, a místo noh kulhavému.
Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
16 Byl jsem otcem nuzných, a na při, jíž jsem nebyl povědom, vyptával jsem se.
Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
17 A tak vylamoval jsem třenovní zuby nešlechetníka, a z zubů jeho vyrážel jsem loupež.
Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
18 A protož jsem říkal: V hnízdě svém umru, a jako písek rozmnožím dny.
“Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
19 Kořen můj rozloží se při vodách, a rosa nocovati bude na ratolestech mých.
Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
20 Sláva má mladnouti bude při mně, a lučiště mé v ruce mé obnovovati se.
Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
21 Poslouchajíce, čekali na mne, a přestávali na radě mé.
“Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
22 Po slovu mém nic neměnili, tak na ně dštila řeč má.
Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
23 Nebo očekávali mne jako deště, a ústa svá otvírali jako k přívalu žádostivému.
Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
24 Žertoval-li jsem s nimi, nevěřili; pročež u vážnosti mne míti neoblevovali.
Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
25 Přišel-li jsem kdy k nim, sedal jsem na předním místě, a tak bydlil jsem jako král v vojště, když smutných potěšuje.
Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”

< Jób 29 >