< Jób 28 >

1 Máť zajisté stříbro prameny své, a zlato místo k přehánění.
Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
2 Železo z země vzato bývá, a kámen rozpuštěný dává měď.
Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
3 Cíl ukládá temnostem, a všelikou dokonalost člověk vystihá, kámen mrákoty a stínu smrti.
Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
4 Protrhuje se řeka na obyvatele, tak že ji nemůže žádný přebřesti, a svozována bývá uměním smrtelného člověka, i odchází.
Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
5 Z země vychází chléb, ačkoli pod ní jest něco rozdílného, podobného k ohni.
Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
6 V některé zemi jest kamení zafirové a prach zlatý,
miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
7 K čemuž stezky nezná žádný pták, aniž ji spatřilo oko luňáka,
Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
8 Kteréž nešlapala mladá zvěř, aniž šel po ní lev.
Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
9 K škřemeni vztahuje ruku svou, a z kořene převrací hory.
Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
10 Z skálí vyvodí potůčky, a všecko, což jest drahého, spatřuje oko jeho.
Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
11 Vylévati se řekám zbraňuje, a tak cožkoli skrytého jest, na světlo vynáší.
Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
12 Ale moudrost kde nalezena bývá? A kde jest místo rozumnosti?
“Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
13 Neví smrtelný člověk ceny její, aniž bývá nalezena v zemi živých.
Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
14 Propast praví: Není ve mně, moře také dí: Není u mne.
Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
15 Nedává se zlata čistého za ni, aniž odváženo bývá stříbro za směnu její.
Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
16 Nemůže býti ceněna za zlato z Ofir, ani za onychin drahý a zafir.
Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
17 Nevrovná se jí zlato ani drahý kámen, aniž směněna býti může za nádobu z ryzího zlata.
Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
18 Korálů pak a perel se nepřipomíná; nebo nabytí moudrosti dražší jest nad klénoty.
Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
19 Není jí rovný v ceně smaragd z Mouřenínské země, aniž za čisté zlato může ceněna býti.
Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
20 Odkudž tedy moudrost přichází? A kde jest místo rozumnosti?
“Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
21 Poněvadž skryta jest před očima všelikého živého, i před nebeským ptactvem ukryta jest.
Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
22 Zahynutí i smrt praví: Ušima svýma slyšely jsme pověst o ní.
Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
23 Sám Bůh rozumí cestě její, a on ví místo její.
Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
24 Nebo on končiny země spatřuje, a všecko, což jest pod nebem, vidí,
pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
25 Tak že větru váhu dává, a vody v míru odvažuje.
Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
26 On též vyměřuje dešti právo, i cestu blýskání hromů.
atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
27 Hned tehdáž viděl ji, a rozhlásil ji, připravil ji, a vystihl ji.
pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
28 Èlověku pak řekl: Aj, bázeň Páně jest moudrost, a odstoupiti od zlého rozumnost.
Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”

< Jób 28 >