< Jób 23 >

1 Tedy odpověděl Job a řekl:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Což vždy předce naříkání mé za zpouru jmíno bude, ješto bída má těžší jest nežli lkání mé?
“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
3 Ó bych věděl, kde ho najíti, šel bych až k trůnu jeho.
Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
4 Pořádně bych před ním vedl při, a ústa svá naplnil bych důvody.
Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
5 Zvěděl bych, jakými slovy by mně odpověděl, a porozuměl bych, co by mi řekl.
Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
6 Zdaliž by podlé veliké síly své rozepři vedl se mnou? Nikoli, nýbrž on sám dal by mi sílu.
Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
7 Tuť by upřímý hádati se mohl s ním, a byl bych osvobozen všelijak od soudce svého.
Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
8 Ale aj, půjdu-li upřímo dále, tam ho není; pakli nazpět, nepostihnu ho.
“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
9 By i čím zaměstknán byl na levo, předce ho nespatřím; zastře-li se na pravo, ovšem ho neuzřím.
Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
10 Nebo on zná cestu, kteráž jest při mně; bude-li mne zkušovati, jako zlato se ukáži.
Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
11 Šlepějí zajisté jeho přídržela se noha má, cesty jeho šetřil jsem, abych se s ní neuchyloval.
Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
12 Aniž od přikázaní rtů jeho uchýlil jsem se, nýbrž ustaviv se na tom, schované jsem měl řeči úst jeho.
Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
13 On pak jestliže při čem stojí, kdo jej odvrátí? Ano duše jeho čehož jen žádá, toho hned dovodí.
“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
14 A vykoná uložení své o mně; nebo takových příkladů mnoho jest při něm.
Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
15 Pročež před tváří jeho děsím se; když to rozvažuji, lekám se ho.
Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
16 Bůh zajisté zemdlil srdce mé, a Všemohoucí předěsil mne,
Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
17 Tak že sotva jsem nezahynul v těch temnostech; nebo před tváří mou nezakryl mrákoty.
Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.

< Jób 23 >