< Jób 22 >

1 A odpovídaje Elifaz Temanský, řekl:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 Zdaliž Bohu silnému co prospěšný býti může člověk, když sobě nejmoudřeji počíná?
“Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
3 Zdaliž se kochá Všemohoucí v tom, že ty se ospravedlňuješ? Aneb má-liž zisk, když bys dokonalé ukázal býti cesty své?
Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
4 Zdali, že by se tebe bál, tresce tě, mstě nad tebou?
“Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
5 Zdali zlost tvá není mnohá? Anobrž není konce nepravostem tvým.
Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
6 Nebo jsi brával základ od bratří svých bez příčiny, a roucha z nahých jsi svláčel.
Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
7 Vody ustalému jsi nepodal, a hladovitému zbraňovals chleba.
Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
8 Ale muži boháči přál jsi země, tak aby ten, jehož osoba vzácná, v ní seděl.
ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
9 Vdovy pak pouštěl jsi prázdné, ačkoli ramena sirotků potřína byla.
Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
10 A protož obkličuji tě osídla, a děsí tě strach nenadálý,
Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
11 Aneb tma, abys neviděl, anobrž rozvodnění přikrývá tě.
nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
12 Říkáš: Zdaž Bůh není na výsosti nebeské? Ano shlédni vrch hvězd, jak jsou vysoké.
“Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
13 Protož pravíš: Jak by věděl Bůh silný? Skrze mrákotu-liž by soudil?
Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
14 Oblakové jsou skrýše jeho, tak že nevidí; nebo okršlek nebeský obchází.
Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
15 Šetříš-liž stezky věku předešlého, kterouž kráčeli lidé marní?
Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
16 Kteříž vypléněni jsou před časem, potok vylit jest na základ jejich.
Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
17 Kteříž říkali Bohu silnému: Odejdi od nás. Což by tedy jim učiniti měl Všemohoucí?
Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
18 On zajisté domy jejich naplnil dobrými věcmi, (ale rada bezbožných vzdálena jest ode mne).
Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
19 Což vidouce spravedliví, veselí se, a nevinný posmívá se jim,
“Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
20 Zvlášť když není vypléněno jmění naše, ostatky pak jejich sežral oheň.
Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
21 Přivykejž medle s ním choditi, a pokojněji se míti, skrze to přijde tobě všecko dobré.
“Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
22 Přijmi, prosím, z úst jeho zákon, a slož řeči jeho v srdci svém.
Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
23 Navrátíš-li se k Všemohoucímu, vzdělán budeš, a vzdálíš-li nepravost od stanů svých,
Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
24 Tedy nakladeš na zemi zlata, a místo kamení potočního zlata z Ofir.
ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
25 Nebo bude Všemohoucí nejčistším zlatem tvým, a stříbrem i silou tvou.
Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
26 A tehdáž v Všemohoucím kochati se budeš, a pozdvihna k Bohu tváři své,
Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
27 Pokorně modliti se budeš jemu, a vyslyší tě; pročež sliby své plniti budeš.
Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
28 Nebo cožkoli začneš, budeť se dařiti, anobrž na cestách tvých svítiti bude světlo.
Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
29 Když jiní sníženi budou, tedy díš: Jáť jsem povýšen. Nebo toho, kdož jest očí ponížených, Bůh spasena učiní.
Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
30 Vysvobodí i toho, kterýž není bez viny, vysvobodí, pravím, čistotou rukou tvých.
Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”

< Jób 22 >