< Jób 15 >

1 Tedy odpovídaje Elifaz Temanský, řekl:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 Zdali moudrý vynášeti má umění povětrné, aneb naplňovati východním větrem břicho své,
“Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
3 Hádaje se slovy neprospěšnými, aneb řečmi neužitečnými?
Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
4 Anobrž vyprazdňuješ i bázeň Boží, a modliteb k Bohu činiti se zbraňuješ.
Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
5 Osvědčujíť zajisté nepravost tvou ústa tvá, ač jsi koli sobě zvolil jazyk chytrých.
Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
6 Potupují tě ústa tvá, a ne já, a rtové tvoji svědčí proti tobě.
Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
7 Zdaliž ty nejprv z lidí zplozen jsi, aneb prvé než pahrbkové sformován?
“Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
8 Zdaliž jsi tajemství Boží slyšel, že u sebe zavíráš moudrost?
Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
9 Co víš, čehož bychom nevěděli? Èemu rozumíš, aby toho při nás nebylo?
Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
10 I šedivýť i stařec mezi námi jest, ano i starší věkem než otec tvůj.
Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
11 Zdali malá jsou tobě potěšování Boha silného, čili něco je zastěňuje tobě?
Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
12 Tak-liž tě jalo srdce tvé, a tak-liž blíkají oči tvé,
Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
13 Že smíš odpovídati Bohu silnému tak pyšně, a vypouštěti z úst svých ty řeči?
moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
14 Nebo což jest člověk, aby se mohl očistiti, aneb spravedliv býti narozený z ženy?
“Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
15 An při svatých jeho není dokonalosti, a nebesa nejsou čistá před očima jeho,
Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
16 Nadto ohavný a neužitečný člověk, kterýž pije nepravost jako vodu.
nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
17 Já oznámím tobě, poslyš mne; to zajisté, což jsem viděl, vypravovati budu,
“Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
18 Což moudří vynesli a nezatajili, slýchavše od předků svých.
zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
19 Jimž samým dána byla země, aniž přejíti mohl cizí prostředkem jejich.
(Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
20 Po všecky své dny bezbožný sám se bolestí trápí, po všecka, pravím léta, skrytá před ukrutníkem.
Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
21 Zvuk strachu jest v uších jeho, že i v čas pokoje zhoubce připadne na něj.
Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
22 Nevěří, by se měl navrátiti z temností, ustavičně očekávaje na sebe meče.
Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
23 Bývá i tulákem, chleba hledaje, kde by byl, cítě, že pro něj nastrojen jest den temností.
Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
24 Děsí jej nátisk a ssoužení, kteréž se silí proti němu, jako král s vojskem sšikovaným.
Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
25 Nebo vztáhl proti Bohu silnému ruku svou, a proti Všemohoucímu postavil se.
chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
26 Útok učinil na něj, na šíji jeho s množstvím zdvižených štítů svých.
Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
27 Nebo přiodíl tvář svou tukem svým, tak že se mu nadělalo faldů na slabinách.
“Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
28 A bydlil v městech zkažených, a v domích, v nichž žádný nebydlil, kteráž v hromady rumu obrácena byla.
munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
29 Avšak nezbohatneť, aniž stane moc jeho, aniž se rozšíří na zemi dokonalost takových.
Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
30 Nevyjde z temností, mladistvou ratolest jeho usuší plamen, a tak zahyne od ducha úst svých.
Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
31 Ale nevěří, že v marnosti jest ten, jenž bloudí, a že marnost bude směna jeho.
Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
32 Před časem svým vyťat bude, a ratolest jeho nebude se zelenati.
Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
33 Zmaří, jako vinný kmen nezralý hrozen svůj, a svrže květ svůj jako oliva.
Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
34 Nebo shromáždění pokrytce spustne, a oheň spálí stany oslepených dary.
Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
35 Kteřížto když počali ssužování, a porodili nepravost, hned břicho jejich strojí jinou lest.
Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”

< Jób 15 >