< Jeremiáš 46 >

1 Slovo Hospodinovo, kteréž se stalo k Jeremiášovi proroku proti národům těmto:
Yehova anamupatsa Yeremiya uthenga wonena za anthu a mitundu ina.
2 O Egyptských. Proti vojsku Faraona Néchy krále Egyptského, (jenž bylo při řece Eufrates u Charkemis, kteréž zbil Nabuchodonozor král Babylonský), léta čtvrtého Joakima syna Joziášova, krále Judského:
Kunena za Igupto: Yehova ananena za gulu lankhondo la Farao Neko mfumu ya ku Igupto limene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni analigonjetsa ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda,
3 Připravtež štít a pavézu, a jděte k boji.
anati, “Konzani zishango zanu ndi malihawo, ndipo yambanipo kupita ku nkhondo!
4 Zapřáhejte koně, a vsedejte jezdci, postavte se s lebkami, vytírejte kopí, zobláčejte se v pancíře.
Mangani akavalo, ndipo kwerani inu okwerapo! Khalani pa mzere mutavala zipewa! Nolani mikondo yanu, valani malaya anu ankhondo!
5 Proč vidím tyto zděšené, zpět obrácené, a nejsilnější jejich potřené, anobrž prudce utíkající, tak že se ani neohlédnou? Strach jest vůkol, dí Hospodin,
Yeremiya anati: Kodi ndikuona chiyani? Achita mantha akubwerera, ankhondo awo agonjetsedwa. Akuthawa mofulumirapo osayangʼananso mʼmbuyo, ndipo agwidwa ndi mantha ponseponse,” akutero Yehova.
6 Aby neutekl čerstvý, a neušel silný, aby na půlnoci o břeh řeky Eufrates zavadili a padli.
Waliwiro sangathe kuthawa ngakhale wankhondo wamphamvu sangathe kupulumuka. Akunka napunthwa ndi kugwa kumpoto kwa mtsinje wa Yufurate.
7 Kdo se to valí jako potok, jako řeky, jejichž vody sebou zmítají?
“Kodi ndani amene akukwera ngati Nailo, ngati mtsinje wa madzi amkokomo?
8 Egypt jako potok se valí a jako řeky, když se vody hýbají, tak pravě: Potáhnu, přikryji zemi, zkazím město i přebývající v něm.
Igupto akusefukira ngati Nailo, ngati mitsinje ya madzi amkokomo. Iye akunena kuti, ‘Ndidzadzuka ndi kuphimba dziko lapansi; ndidzawononga mizinda ndi anthu ake.’
9 Křepčtež, ó koni, a běžte s hřmotem, ó vozové; nechť vytáhnou i silní, Mouřenínové a Putští, kteříž užívají pavézy, i Ludimští, kteříž užívají a natahují lučiště.
Tiyeni, inu akavalo! Thamangani inu magaleta! Tulukani, inu ankhondo, ankhondo a ku Kusi ndi Puti amene mumanyamula zishango, ankhondo a ku Ludi amene mumaponya uta.
10 A však ten den Panovníka Hospodina zástupů bude den pomsty, aby uvedl pomstu na nepřátely své, kteréžto zžíře meč a nasytí se, anobrž opojí se krví jejich; nebo obět Panovníka Hospodina zástupů bude v zemi půlnoční u řeky Eufrates.
Koma tsikulo ndi la Ambuye Yehova Wamphamvuzonse; tsiku lolipsira, lolipsira adani ake. Lupanga lake lidzawononga ndi kukhuta magazi, lidzaledzera ndi magazi. Pakuti Yehova, Yehova Wamphamvuzonse, adzapereka adani ake ngati nsembe mʼdziko la kumpoto mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
11 Vyprav se do Galád, a nabeř masti, panno dcero Egyptská, nadarmo však užíváš mnohého lékařství, nebo ty zhojena býti nemůžeš.
“Pita ku Giliyadi ukatenge mankhwala iwe namwali Igupto. Wayesayesa mankhwala ambiri koma osachira; palibe mankhwala okuchiritsa.
12 Slyšíť národové o zlehčení tvém, a naříkání tvého plná jest země, proto že silný na silném se ustrkuje, tak že spolu zaroveň padají.
Anthu a mitundu ina amva za manyazi ako; kulira kwako kwadzaza dziko lapansi. Ankhondo akunka nagwetsanagwetsana, onse awiri agwa pansi limodzi.”
13 Slovo, kteréž mluvil Hospodin k Jeremiášovi proroku o přitažení Nabuchodonozora krále Babylonského, aby zkazil zemi Egyptskou.
Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za kubwera kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kudzathira nkhondo Igupto ndi uwu:
14 Oznamte v Egyptě, a ohlaste v Magdol, rozhlaste také v Nof, i v Tachpanches rcete: Postůj a připrav se, ale však zžíře meč všecko, což vůkol tebe jest.
“Mulengeze ku Igupto. Mulengeze ku Migidoli. Mulengezenso ku Mefisi ndi ku Tapanesi. Muwawuze anthu akumeneko kuti, ‘Imani pamalo panu ndi kukhala okonzeka kudziteteza, chifukwa lupanga lidzawononga zonse zimene muli nazo.’
15 Proč poražen jest každý z nejsilnějších tvých? Nemůže ostáti, proto že Hospodin pudí jej.
Chifukwa chiyani mulungu wanu wamphamvu uja Apisi wathawa? Iye sakanatha kulimba chifukwa Yehova anamugwetsa.
16 Mnohoť bude těch, kteříž klesnou a padnou jeden na druhého, a řeknou: Vstaň, a navraťme se k lidu svému, a do země, v níž jsme se zrodili, před mečem toho zhoubce.
Ankhondo anu apunthwa ndi kugwa. Aliyense akuwuza mnzake kuti, ‘Tiyeni tibwerere kwathu, ku dziko kumene tinabadwira, tithawe lupanga la adani athu.’
17 Budou křičeti tam: Faraona krále Egyptského není než sám chřest, jižť pominul volný jeho čas.
Kumeneku iwo adzafuwula kuti, ‘Farao, mfumu ya ku Igupto mupatseni dzina lakuti, Waphokoso, Wotaya mwayi wake.’
18 Živť jsem já, (dí král ten, jehož jméno Hospodin zástupů), že jakž jest Tábor mezi horami, a jako Karmel při moři, tak toto přijde.
“Pali Ine wamoyo,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse, “wina adzabwera amene ali ngati Tabori phiri lopambana mapiri ena, ngati phiri la Karimeli loti njoo mʼmbali mwa nyanja.
19 Připraviž sobě to, co bys s sebou vystěhovati měla, ó ty, kteráž jsi usadila se, dcero Egyptská; neboť Nof v poušť obrácen a vypálen bude, tak že nebude tam žádného obyvatele.
Konzani katundu wanu wopita naye ku ukapolo inu anthu a ku Igupto, pakuti Mefisi adzasanduka chipululu ndipo adzakhala bwinja mopanda wokhalamo.
20 Velmi pěkná jalovice jest Egypt, ale zabití její od půlnoci jistotně přijde.
“Igupto ali ngati mwana wangʼombe wokongola, koma chimphanga chikubwera kuchokera kumpoto kudzalimbana naye.
21 Ano i nájemníci jeho u prostřed něho jsou jako telata vytylá, ale takéť i ti obrátíce se, utekou. Neostojí, když den bídy jejich přijde na ně, v čas navštívení jejich.
Ngakhale ankhondo aganyu amene ali naye ali ngati ana angʼombe onenepa. Nawonso abwerera mʼmbuyo, nathawa pamodzi. Palibe amene wachirimika. Ndithu, tsiku la tsoka lawafikira; ndiyo nthawi yowalanga.
22 Hlas jeho jako hadí siptěti bude, když s vojskem přitáhnou, a s sekerami přijdou na něj jako ti, kteříž sekají dříví.
Aigupto akuthawa ndi liwu lawo lili ngati la njoka yothawa pamene adani abwera ndi zida zawo, abwera ndi nkhwangwa ngati anthu odula mitengo.
23 Posekají les jeho, dí Hospodin, ačkoli mu konce není; více jest jich než kobylek, aniž mají počtu.
Iwo adzadula nkhalango ya Igupto,” akutero Yehova, “ngakhale kuti ndi yowirira. Anthuwo ndi ochuluka kupambana dzombe, moti sangatheke kuwerengeka.
24 Zahanbenať bude dcera Egyptská, vydána bude v ruku lidu půlnočního.
Anthu a ku Igupto achita manyazi atengedwa ukapolo ndi anthu a kumpoto.”
25 Praví Hospodin zástupů, Bůh Izraelský: Aj, já navštívím lidné město No, též Faraona i Egypt s bohy jeho a králíky jeho, Faraona, pravím, a ty, kteříž v něm doufají.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, “Ndili pafupi kulanga Amoni mulungu wa Tebesi. Ndidzalanganso Farao ndi Igupto pamodzi ndi milungu yake yonse, mafumu ake ndi onse amene amamukhulupirira.
26 A vydám je v ruku těch, kteříž hledají bezživotí jejich, totiž v ruku Nabuchodonozora krále Babylonského, a v ruku služebníků jeho; potom však bydleno bude v něm, jako za dnů starodávních, dí Hospodin.
Ndidzawapereka kwa amene akufuna kuwapha, ndiye kuti kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi atsogoleri ake ankhondo. Komabe, mʼtsogolomo Igupto adzakhalanso ndi anthu monga kale,” akutero Yehova.
27 Ale ty neboj se, služebníče můj Jákobe, aniž se strachuj, ó Izraeli; nebo aj, já vysvobodím tě zdaleka, i símě tvé z země zajetí jejich. I navrátí se Jákob, aby odpočíval a pokoj měl, a aby nebylo žádného, kdo by předěsil.
“Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha; usataye mtima, iwe Israeli. Ndithu Ine ndidzakupulumutsa kuchokera ku mayiko akutali, ndidzapulumutsanso zidzukulu zako kuchokera ku mayiko kumene anapita nazo ku ukapolo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala motakasuka ndi pa mtendere, ndipo palibenso wina amene adzamuopsa.
28 Ty, pravím, neboj se, služebníče můj Jákobe, dí Hospodin; neboť jsem s tebou. Učiním zajisté konec všechněm národům, mezi kteréž tě zaženu, tobě pak neučiním konce, ale budu tě trestati v soudu, ačkoli tě naprosto bez trestání nenechám.
Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe,” akutero Yehova. “Ndidzawonongeratu mitundu yonse ya anthu a ku mayiko kumene ndakupirikitsira, Koma iwe sindidzakuwononga kotheratu. Ndidzakulanga iwe ndithu koma moyenerera; sindidzakulekerera osakulanga.”

< Jeremiáš 46 >