< Jeremiáš 4 >

1 Budeš-li se míti navrátiti, Izraeli, dí Hospodin, ke mně se navrať. Nebo odejmeš-li ohavnosti své od tváři mé a nebudeš-li se toulati,
“Ngati mukufuna kubwerera, inu Aisraeli, bwererani kwa Ine,” akutero Yehova. “Chotsani mafano anu onyansa pamaso panga ndipo musasocherenso.
2 A budeš-li přisahati právě, náležitě a spravedlivě, říkaje: Živť jest Hospodin, tedy požehnání dávati sobě v něm budou národové, a v něm se chlubiti.
Muzilumbira mokhulupirika ndiponso mwa chilungamo kuti, ‘Pali Yehova wamoyo.’ Mukatero anthu a mitundu ina yonse adzandipempha kuti ndiwadalitse ndipo adzanditamanda.”
3 Nebo takto praví Hospodin mužům Judským a Jeruzalémským: Zořte sobě ouhor, a nerozsívejte do trní.
Zimene Yehova akunena kwa anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu ndi izi: “Limani masala anu musadzale pakati pa minga.
4 Obřežte se Hospodinu, a odejměte neobřízky srdce vašeho, muži Judští a obyvatelé Jeruzalémští, aby nevyšla jako oheň prchlivost má, a nehořela, tak že by nebyl kdo uhasiti, pro nešlechetnost předsevzetí vašich.
Dziperekeni nokha kwa Ine kuti munditumikire ndi mtima wanu wonse, inu anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu. Muzichita zimenezi kuopa kuti mkwiyo wanga ungabuke ngati moto ndi kukutenthani, chifukwa cha ntchito zanu zoyipazo popanda wina wowuzimitsa.
5 Oznamte v Judstvu, a v Jeruzalémě ohlaste, a rcete: Trubte trubou v zemi, svolejte a sbeřte lid, a rcete: Shromažďte se, a vejděme do měst hrazených.
“Lengeza ku Yuda ndi kulalikira mu Yerusalemu kuti, ‘Lizani lipenga mʼdziko lonse!’ Ndipo fuwulani kuti, ‘Sonkhanani! Tiyeni tithawire ku mizinda yotetezedwa!’
6 Vyzdvihněte korouhev na Sionu, zmužile se mějte, nepostávejte; nebo já zlé věci uvedu od půlnoci, a potření veliké.
Kwezani mbendera kuyangʼana ku Ziyoni! Musachedwe, thawani kuti mupulumuke! Pakuti Ine ndikubweretsa chilango kuchokera kumpoto, kudzakhala chiwonongeko choopsa.”
7 Vychází lev z houště své, a ten, kterýž hubí národy, vyšed z místa svého, táhne, aby obrátil zemi tvou v pustinu, a města tvá aby zbořena byla, tak aby nebylo žádného obyvatele.
Monga mkango umatulukira mʼngaka yake momwemonso wowononga mayiko wanyamuka ndi kutuluka ku mbuto yake. Watero kuti awononge dziko lanu. Mizinda yanu idzakhala mabwinja popanda wokhalamo.
8 Protož přepašte se žíněmi, kvělte a naříkejte; nebo není odvrácen hněv prchlivosti Hospodinovy od nás.
Choncho valani ziguduli, lirani ndi kubuwula, pakuti mkwiyo waukulu wa Yehova sunatichokere.
9 Stane se zajisté v ten den, dí Hospodin, že zhyne srdce královo a srdce knížat, užasnou se i kněží, a proroci diviti se budou.
“Pa tsiku limenelo, mfumu ndi nduna zake adzataya mtima, ansembe adzachita mantha kwambiri, ndipo aneneri adzathedwa nzeru,” akutero Yehova.
10 I řekl jsem: Ach, Panovníče Hospodine, jistě že jsi velice podvedl lid tento, i Jeruzalém, říkaje: Pokoj míti budete, a však pronikl meč až k duši.
Ndipo ine ndinati, “Haa, Ambuye Yehova, ndithu munawanyenga anthu awa pamodzi ndi Yerusalemu pamene munanena kuti, ‘Mudzakhala pa mtendere,’ chonsecho lupanga lili pakhosi pathu.”
11 V ten čas řečeno bude lidu tomuto i Jeruzalému: Vítr tuhý z míst vysokých na poušti jde upřímo na lid můj, ne aby převíval, ani přečišťoval.
Nthawi imeneyo anthu awa ndi Yerusalemu adzawawuza kuti, “Mphepo yotentha yochokera ku magomo a mʼchipululu ikuwomba pa anthu anga, osati mphepo yopeta kapena yoyeretsa;
12 Vítr silnější než oni přijde mi, nyní já také vypovím jim úsudky.
koma mphepo yamphamvu kwambiri yochokera kwa Ine. Tsono ndi Ineyo amene ndikuwaweruza.”
13 Aj, jako oblakové vystupuje, a jako vicher vozové jeho, rychlejší jsou nežli orlice koni jeho. Běda nám, nebo popléněni jsme.
Taonani, adani akubwera ngati mitambo, magaleta awo akubwera ngati kamvuluvulu, akavalo awo ndi aliwiro kupambana chiwombankhanga. Tsoka ilo! Tawonongeka!
14 Obmej od nešlechetnosti srdce své, Jeruzaléme, abys vysvobozen byl. Dokudž zůstávati budou u prostřed tebe myšlení marnosti tvé?
Iwe Yerusalemu, tsuka mtima wako kuchotsa zoyipa kuti upulumuke. Kodi maganizo ako oyipawo udzakhala nawo mpaka liti?
15 Nebo hlas oznamujícího přichází od Dan, a toho, kterýž ohlašuje nepravost, s hory Efraim.
Pakuti amithenga akulalika mawu mʼdziko la Dani; akulengeza za masautso kuchokera ku mapiri a Efereimu.
16 Připomínejte těmto národům, aj, ohlašujte Jeruzalémským, že strážní táhnou z země daleké, a vydávají proti městům Judským hlas svůj.
Iwo akuti, “Fotokozani zimenezi kwa anthu a mitundu ina, lengezani zimenezi mu Yerusalemu kuti, ‘Ankhondo akubwera kuchokera ku dziko lakutali, akufuwula ndi kudzazinga mizinda ya Yuda.
17 Jako ti, kteříž hlídají polí, položí se proti němu vůkol; nebo jest mi odporný, dí Hospodin.
Azinga Yerusalemu ngati anthu olondera munda, chifukwa Yerusalemu wandiwukira,’” akutero Yehova.
18 Cesta tvá a skutkové tvoji to způsobili tobě; toť nešlechetnost tvá, žeť to hořké jest, a že dosahá až do srdce tvého.
“Makhalidwe anu ndi zochita zanu zakubweretserani zimenezi. Chimenechi ndiye chilango chanu. Nʼchowawa kwambiri! Nʼcholasa mpaka mu mtima!”
19 Ó, střeva má, střeva má, bolest trpím, ó osrdí mé, kormoutí se ve mně srdce mé, nemohuť mlčeti. Nebo hlas trouby slyšíš, duše má, a prokřikování vojenské.
Mayo, mayo, ndikumva kupweteka! Aa, mtima wanga ukupweteka, ukugunda kuti thi, thi, thi. Sindingathe kukhala chete. Pakuti ndamva kulira kwa lipenga; ndamva mfuwu wankhondo.
20 Potření za potřením provolává se, popléněna zajisté bude všecka země, náhle popléněni budou stanové moji, v okamžení kortýny mé.
Tsoka limatsata tsoka linzake; dziko lonse lasanduka bwinja. Mwadzidzidzi matenti athu awonongedwa, mwa kanthawi kochepa nsalu zake zotchinga zagwetsedwa.
21 Až dokud vídati budu korouhev, slýchati hlas trouby?
Kodi ndikhale ndikuona mbendera ya nkhondo, ndi kumva kulira kwa lipenga mpaka liti?
22 Nebo bláznivý lid můj nezná mne, synové nemoudří a nerozumní jsou. Moudří jsou k činění zlého, ale činiti dobře neumějí.
Yehova akuti, “Anthu anga ndi zitsiru; iwo sandidziwa. Iwo ndi ana opanda nzeru; samvetsa chilichonse. Ali ndi luso lochita zoyipa, koma sadziwa kuchita zabwino.”
23 Hledím-li na zemi, a aj, nesličná jest a prázdná; pakli na nebe, není na něm žádného světla.
Ndinayangʼana dziko lapansi, ndipo linali lopanda anthu ndi lopanda kanthu; ndinayangʼana thambo, koma linalibe kuwala kulikonse.
24 Hledím-li na hory, a aj, třesou se, a všickni pahrbkové pohybují se.
Ndinayangʼana mapiri, ndipo ankagwedezeka; magomo onse ankangosunthira uku ndi uku.
25 Hledím-li, a aj, není žádného člověka, a všeliké ptactvo nebeské zaletělo.
Ndinayangʼana, ndipo sindinaone anthu; mbalame iliyonse ya mlengalenga inali itathawa.
26 Hledím-li, a aj, pole úrodné jest pouští, a všecka města jeho zbořena jsou od Hospodina a od hněvu prchlivosti jeho.
Ndinayangʼana, dziko lachonde linali litasanduka chipululu; mizinda yake yonse inali itasanduka bwinja pamaso pa Yehova, chifukwa cha mkwiyo wake.
27 Nebo takto praví Hospodin: Spustne všecka země, a však konce ještě neučiním.
Yehova akuti, “Dziko lonse lidzasanduka chipululu komabe sindidzaliwononga kotheratu.
28 Kvíliti bude nad tím země, a zasmuší se na hoře nebe, proto že jsem mluvil, co jsem myslil, a nelituji, aniž se odvrátím od toho.
Chifukwa chake dziko lapansi lidzalira ndipo thambo lidzachita mdima, pakuti ndayankhula ndipo sindidzafewa mtima, ndatsimikiza ndipo sindidzabwerera mʼmbuyo.”
29 Před hřmotem jezdců a těch, kteříž střílejí z lučiště, uteče všecko město. Vejdou do hustých oblaků, a na skálí vylezou; všecka města opuštěna budou, a žádný nebude bydliti v nich.
Pakumva phokoso la okwera pa akavalo ndi la anthu oponya mivi, anthu a mʼmizinda adzathawa. Ena adzabisala ku nkhalango; ena adzakwera mʼmatanthwe mizinda yonse nʼkuyisiya; popanda munthu wokhalamo.
30 Ty pak pohubena jsuc, což činiti budeš? Ačkoli obláčíš se v šarlat, ačkoli se ozdobuješ ozdobou zlatou, ačkoli líčíš tvář svou líčidlem, darmo se okrašluješ. Pohrdají tebou frejíři, bezživotí tvého hledají.
Iwe Yerusalemu, ndiwe bwinja! Ukutanthauza chiyani kuvala zovala zofiira ndi kuvalanso zokometsera zagolide? Ngakhale udzikonze maso ako powapaka zokometsera, ukungodzivuta chabe. Zibwenzi zako zikukunyoza; zikufuna kuchotsa moyo wako.
31 Nebo slyším hlas jako rodičky, svírání jako té, kteráž po nejprvé ku porodu pracuje, hlas dcery Sionské, ustavičně vzdychající, a lomící rukama svýma, říkající: Běda mně nyní, nebo ustala duše má pro vrahy.
Ndikumva kulira ngati kwa mayi pa nthawi yake yobereka, kubuwula ngati kwa mayi amene akubereka mwana wake woyamba. Kuliraku ndi kwa anthu a mu Ziyoni, wefuwefu. Atambalitsa manja awo nʼkumati, “Kalanga ife! Tikukomoka. Moyo wathu waperekedwa kwa anthu otipha.”

< Jeremiáš 4 >